< 1 Mbiri 18 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
Y después de esto, David atacó a los filisteos y los venció, y tomó a Gat con sus aldeas de las manos de los filisteos.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
Y venció a Moab, y los moabitas se convirtieron en sus sirvientes y tuvieron que dar ofrendas a David.
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
Entonces David venció a Hadadezer, rey de Soba, cerca de Hamat, cuando iba a hacer ver su poder junto al río Eufrates.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
Y le quitó David mil carruajes de guerra, siete mil jinetes y veinte mil de infantería; y le cortaron los músculos de las patas de todos los caballos, conservando sólo lo suficiente para un centenar de carruajes de guerra.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
Y cuando los sirios de Damasco acudieron en ayuda de Hadadezer, rey de Soba, David puso a filo de espada veintidós mil arameos.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
Entonces David puso fuerzas armadas en Damasco, y los sirios se convirtieron en sus sirvientes y le dieron ofrendas. Y él Señor le dio la victoria a David dondequiera que iba.
7 Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
Y los escudos de oro de los siervos de Hadadezer, David los tomó, y los llevó a Jerusalén.
8 Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
Y de Tibhat y de Cun, ciudades de Hadadezer, David tomó una gran cantidad de bronce, de los cuales Salomón hizo la gran vasija de agua de bronce y las columnas y recipientes de bronce.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
Cuando Toi, rey de Hamat, tuvo noticias de que David había vencido a todo el ejército de Hadadezer, rey de Sobá,
10 anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
Envió a su hijo Hadoram al rey David para darle palabras de paz y bendición, porque había vencido a Hadadezer en la lucha, porque Hadadezer había estado en guerra con Toi; y le dio todo tipo de vasos de oro, plata y bronce.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
Este rey David santificó al Señor, junto con la plata y el oro que había tomado de todas las naciones; de Edom y Moab y de los hijos de Amón y de los filisteos y de Amalec.
12 Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
Ademas Abisai, hijo de Sarvia, derrotó a filo de espada dieciocho mil de los edomitas en el valle de la sal,
13 Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
David puso fuerzas armadas en todas las ciudades de Edom; y todos los edomitas se convirtieron en siervos de David. El Señor hizo que David venciera dondequiera que iba.
14 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
Así que David fue rey sobre todo Israel, juzgando y dando las decisiones correctas para todo su pueblo.
15 Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
Y Joab, hijo de Sarvia, era el jefe del ejército; y Josafat, hijo de Ahilud, era el guardián de los registros.
16 Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
Y Sadoc, hijo de Ahitob; y Ahimelec, el hijo de Abiatar, eran sacerdotes; y Savsa era el escriba;
17 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.
Y Benaía, hijo de Joiada, estaba sobre los cereteos y los peleteos; y los hijos de David fueron los principales de aquellos cuyos lugares estaban al lado del rey.

< 1 Mbiri 18 >