< 1 Mbiri 18 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
Some time later, David’s [army] attacked the army of Philistia and defeated them. They captured Gath [city] and the surrounding villages.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
His [army] also defeated [the army of] the Moab [people-group]. The people were forced to accept David as their ruler, and also to pay money [each year to David’s government, in order that David’s army would protect them].
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
David’s [army] also fought against [the army of] Hadadezer, the king of [the] Zobah [region in Syria] near Hamath [city], when Hadadezer was trying to establish control over the area near the Euphrates River.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
David’s [army] captured 1,000 of Hadadezer’s chariots, 7,000 chariot-drivers, and 20,000 soldiers. They hamstrung/crippled most of their horses; there were only 100 horses that they did not cripple.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
When the army of Syria came from Damascus [city] to help Hadadezer’s [army], David’s soldiers killed 22,000 of them.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
Then David stationed groups of his soldiers in Damascus, and the people of Syria were forced to accept David as their ruler, and to pay to David’s government [each year] the payment/tax that he demanded. And Yahweh enabled David’s [army] to win battles everywhere they went.
7 Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
David soldiers took the gold shields that were carried by the officers of Hadadezer’s [army] and brought them to Jerusalem.
8 Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
They also brought from Tebah (OR, Tibhath) and Cun, two towns that belonged to Hadadezer, a lot of bronze, which [David’s son] Solomon [later] used to make the huge bronze basin and the pillars and other bronze items [for the temple].
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
When Tou, the king of Hamath [city in Syria], heard that David’s [army] had defeated the entire army of King Hadadezer,
10 anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
he sent his son Hadoram to King David, to greet him and (congratulate him/tell him that he was happy) about his defeating Hadadezer’s army, which had been fighting [the army of] Tou. Hadoram brought to David many items/gifts made of gold, silver, and bronze.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
King David dedicated those things to Yahweh, like he had done with the silver and gold that his soldiers had taken from [the] Edom and Moab [people-groups], and from the Ammon people-group and from the people of Philistia, and from [the descendants of] Amalek.
12 Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
[One of David’s army commanders, ] Abishai, whose mother was Zeruiah, went with his army and killed 18,000 soldiers from Edom in the Salt Valley.
13 Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
Then David stationed groups of his soldiers there in Edom, and the people of Edom were forced to accept David as their king and to pay money to David’s government [every year]. And Yahweh enabled David’s [army] to win battles wherever they went.
14 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
David ruled over all the Israeli people, and he always did for them what was just and fair.
15 Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
Zeruiah’s son Joab was the chief army commander. Jehoshaphat the son of Ahilud was the record-keeper.
16 Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
Zadok the son of Ahitub and Ahimelech the son of Abiathar were the Supreme Priests. Shavsha was the official secretary.
17 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.
Benaiah the son of Jehoiada ruled over the Kereth and Peleth groups [who were David’s bodyguards]. And David’s sons were his most important officials.

< 1 Mbiri 18 >