< 1 Mbiri 18 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
And it was after thus and he struck down David [the] Philistines and he subdued them and he took Gath and daughters its from [the] hand of [the] Philistines.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
And he struck down Moab and they became Moab subjects of David bearers of tribute.
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
And he struck down David Hadadezer [the] king of Zobah Hamath towards when went he to establish monument his at [the] river of Euphrates.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
And he captured David from him one thousand chariot[s] and seven thousand horsemen and twenty thousand man on foot and he hamstrung David all the chariotry and he left of it one hundred chariot[s].
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
And it came Aram Damascus to help Hadadezer [the] king of Zobah and he struck down David in Aram twenty and two thousand man.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
And he put David in Aram Damascus and it became Aram of David subjects bearers of tribute and he gave victory Yahweh to David in every where he went.
7 Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
And he took David [the] shields of gold which they were on [the] servants of Hadadezer and he brought them Jerusalem.
8 Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
And from Tibhath and from Kun [the] cities of Hadadezer he took David bronze much very with it - he made Solomon [the] sea of bronze and the pillars and [the] articles of bronze.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
And he heard Tou [the] king of Hamath that he had struck down David all [the] army of Hadadezer [the] king of Zobah.
10 anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
And he sent Hadoram son his to the king David (to ask *Q(k)*) of him to welfare and to bless him on that he had fought against Hadadezer and he had defeated him for man of wars of Tou he was Hadadezer and all articles of gold and silver and bronze.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
Also them he consecrated the king David to Yahweh with the silver and the gold which he had taken away from all the nations from Edom and from Moab and from [the] people of Ammon and from [the] Philistines and from Amalek.
12 Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
And Abishai [the] son of Zeruiah he struck down Edom in [the] Valley of Salt eight-teen thousand.
13 Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
And he put in Edom garrisons and they became all Edom subjects of David and he gave victory to Yahweh David in every where he went.
14 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
And he reigned David over all Israel and he was doing justice and righteousness for all people his.
15 Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
And Joab [the] son of Zeruiah [was] over the army and Jehoshaphat [the] son of Ahilud [was the] recorder.
16 Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
And Zadok [the] son of Ahitub and Abimelech [the] son of Abiathar [were] priests and Shavsha [was the] scribe.
17 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.
And Benaiah [the] son of Jehoiada [was] over the Kerethite[s] and the Pelethite[s] and [the] sons of David [were] the first to [the] side of the king.

< 1 Mbiri 18 >