< 1 Mbiri 17 >

1 Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
А кад Давид сеђаше код куће своје, рече Давид Натану пророку: Гле, ја стојим у кући од кедровог дрвета, а ковчег завета Господњег под завесима.
2 Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
А Натан рече Давиду: Шта ти је год у срцу, чини, јер је Бог с тобом.
3 Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
Али ону ноћ дође реч Божја Натану говорећи:
4 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
Иди и реци Давиду слузи мом: Овако вели Господ: Ти ми нећеш сазидати куће да у њој наставам.
5 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
Кад нисам наставао у кући откад изведох Израиља до данас, него сам ишао од шатора до шатора и од наслона до наслона,
6 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
Куда сам год ходио са свим Израиљем, јесам ли једну реч рекао коме између судија Израиљевих којима заповедах да пасу народ мој, и казао: Зашто ми не начините кућу од кедра?
7 Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
Овако, дакле, реци слузи мом Давиду: Овако вели Господ над војскама: Ја те узех од тора, од оваца, да будеш вођ народу мом Израиљу.
8 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
И бејах с тобом куда си год ишао, и истребих све непријатеље твоје испред тебе, и стекох ти име као што је име великих људи на земљи.
9 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
И одредићу место народу свом Израиљу, и посадићу га, те ће наставати у свом месту, и неће се више претресати; нити ће им више досађивати неправедници као пре,
10 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
И од оног дана када сам поставио судије над народом својим Израиљем; и покорих све непријатеље твоје; него ти јављам да ће ти Господ сазидати кућу.
11 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
И кад се наврше дани твоји да отидеш к оцима својим, подигнућу семе твоје након тебе, које ће бити између синова твојих, и утврдићу царство његово.
12 Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
Они ће ми сазидати дом, и утврдићу престо његов довека.
13 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
Ја ћу му бити Отац, и он ће ми бити син; а милости своје нећу уклонити од њега као што сам уклонио од оног који беше пре тебе.
14 Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
Него ћу га утврдити у дому свом и у царству свом довека, и престо ће његов стајати довека.
15 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
По свим овим речима и по свој овој утвари каза Натан Давиду.
16 Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
Тада дође цар Давид и стаде пред Господом, и рече: Ко сам ја, Господе Боже, и шта је дом мој, те си ме довео довде?
17 Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
И то ти се чини мало, Боже, него си говорио и за дом слуге свог на дуго времена, и постарао си се за ту славу законом човечијим, Господе Боже.
18 “Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
Шта ће још Давид да Ти говори о части слуге Твог, кад Ти знаш слугу свог?
19 Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
Господе, слуге свог ради и по срцу свом чиниш сву ову велику ствар, обзнањујући све ове велике ствари.
20 “Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
Господе, нема таквог какав си Ти, и нема Бога осим Тебе, по свему сто чусмо својим ушима.
21 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
Јер који је народ на земљи као Твој народ Израиљ? Ради кога је Бог ишао да га искупи да му буде народ, и да стече себи име великим и страшним делима изгонећи народе испред народа свог, који си искупио из Мисира
22 Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
Јер си учинио народ свој Израиља својим народом довека; а Ти си им, Господе, Бог.
23 “Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
И тако, Господе, реч коју си обрекао слузи свом и дому његовом нека буде тврда довека, и учини како си рекао.
24 kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
Нека буде тврда, да се велича име Твоје довека и да се говори: Господ над војскама, Бог Израиљев јесте Бог над Израиљем, и дом Давида слуге Твог нека стоји тврдо пред Тобом.
25 “Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
Јер си Ти, Боже мој, јавио слузи свом да ћеш му сазидати дом, зато се слуга Твој усуди да Ти се помоли.
26 Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
Тако Господе, Ти си Бог, и обрекао си слузи свом то добро.
27 Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
Буди дакле вољан и благослови дом слуге свог да буде довека пред Тобом; јер кад Ти, Господе, благословиш, биће благословен довека.

< 1 Mbiri 17 >