< 1 Mbiri 17 >
1 Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
Napasamak daytoy kalpasan a nagnaeden ti ari iti balayna, kinunana kenni Natan a propeta, “Kitaem, agnanaedak iti balay a naaramid iti sedro, ngem adda iti sirok ti tolda ti lakasa ti tulag ni Yahweh.”
2 Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
Ket kinuna ni Natan kenni David, “Mapanka, ket aramidem ti adda dita pusom, ta adda kenka ti Dios.
3 Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
Ngem iti dayta met laeng a rabii, dimteng kenni Natan ti sao ti Dios a kinunana,
4 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
“Mapanka ket ibagam kenni David nga adipenko, 'Kastoy ti kinuna ni Yahweh: Saannak nga ipatakderan iti balay a pagnaedak.
5 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
Ta saanak a nagnaed iti maysa a balay manipud iti aldaw nga impanawko ti Israel idiay Egipto agingga iti agdama nga aldaw. Ngem ketdi, nagnanaedak iti tolda, iti maysa a tabernakulo, kadagiti naduma-duma a luglugar.
6 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
Kadagiti amin a lugar nga immakarak a kadduak ti entero nga Israel, adda kadi ti aniaman nga imbagak iti siasinoman kadagiti mangidadaulo iti Israel a dinutokak a mangaywan kadagiti tattaok, a kunak, “'Apay a saandak nga impatakderan iti balay a naaramid iti sedro?"”'
7 Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
“Ita ngarud, ibagam iti adipenko a ni David, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh a Mannakabalin-amin: “Innalaka manipud iti pagpaaraban, manipud iti panangsursurotmo kadagiti karnero, tapno sika iti mangituray kadagiti tattaok nga Israelita.
8 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
Ket addaak a kanayon kenka sadinoman a napanam ket pinasagko amin dagiti kabusormo iti sangoanam. Ket iyaramidanka iti nagan, kas iti nagan dagiti naindaklan a tattao nga adda iti rabaw iti daga.
9 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
Mangpiliakto iti lugar a pagnaedan dagiti tattaok nga Israelita ket pagtalinaedekto isuda sadiay, tapno agnaeddanto iti kabukbukodanda a lugar ket saandanton a pulos a mariribuk pay. Saanton nga idadanes ida dagiti nadangkes a tattao, a kas iti inaramidda idi,
10 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
kas iti ar-aramidenda manipud kadagiti al-aldaw a binilinko dagiti uk-ukom a mangituray kadagiti tattaok nga Israelita. Ket parmekekto dagiti amin a kabusormo. Kas kanayonanna, ibagak kenka, Siak a ni Yahweh ket ipatakderankanto iti balay.
11 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
Mapasamakto dayta inton malpasen dagiti al-aldawmo ket mapankan iti ayan dagiti ammam, itag-aykonto ti kaputotam a sumaruno kenka, ket maysa kadagiti kaputotam, pagtalinaedekto ti pagarianna.
12 Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
Ipatakderannakto iti balay, ket pagtalinaedekto ti tronona iti agnanayon.
13 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
Siakto ti amana, ket isunanto ti anakko. Saankonto a babawyen manipud kenkuana ti kinapudnok iti tulagko a kas iti panangibabawik manipud kenni Saul, a nagturay sakbay kenka.
14 Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
Isaadkonto isuna a mangituray iti balayko ken iti pagariak iti agnanayon, ket agtalinaedto ti tronona iti agnanayon."”'
15 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
Nakisao ni Natan kenni David ket impadamagna kenkuana amin dagitoy a sasao, ket imbagana kenkuana ti sibubukel a sirmata.
16 Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
Ket simrek ni David, nagtugaw iti sangoanan ni Yahweh; kinunana, “Siasinoak, O Yahweh a Dios, ken ania ti pamiliak, ta impannak iti daytoy a kasasaad?
17 Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
Ket bassit daytoy a banag iti imatangmo, O Dios. Imbagam dagiti naindaklan a banbanag a mapasamakto iti masakbayan kadagiti pamilia toy adipenmo, ket impakitam kaniak dagiti masakbayan a henerasion, O Yahweh a Dios.
18 “Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
Ania pay ti maibagak kenka, siak a ni David? Pinadayawam daytoy adipenmo. Inikkam daytoy adipenmo iti naisangsangayan a pammadayaw.
19 Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
O Yahweh, para iti pagimbagan daytoy adipenmo, ken tapno matungpal ti bukodmo a panggep, inaramidmo daytoy a naindaklan a banag tapno ipakitam dagiti amin a naindaklan nga aramidmo.
20 “Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
O Yahweh, awanen iti kas kenka, ken awanen iti Dios malaksid kenka, kas iti kanayon a mangmangngegmi.
21 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
Ken ania a nasion ditoy daga ti kas kadagiti tattaom nga Israelita, a sika, O Dios, ti nangispal manipud idiay Egipto kas tattaom, tapno aglatak ti naganmo babaen kadagiti naindaklan ken nakaskasdaaw nga ar-aramid? Pinapanawmo dagiti nasion manipud iti sangoanan dagiti tattaom, nga inispalmo manipud idiay Egipto.
22 Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
Pinagbalinmo a tattaom iti agnanayon dagiti Israelita, ket sika, O Yahweh, ti nagbalin a Diosda.
23 “Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
Isu nga ita, O Yahweh, matungpal koma iti agnanayon ti inkarim iti adipenmo ken iti pamiliana. Aramidem koma kas insaom.
24 kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
Maitan-ok koma ti naganmo iti agnanayon ket agbalin a naindaklan, tapno ibaga dagiti tattao, 'Ni Yahweh a Mannakabalin-amin ket isu ti Dios ti Israel,' kabayatan a ti balayko, siak a ni David nga adipenmo ket agtalinaed iti sangoanam.
25 “Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
Ta sika, O Diosko ti nangipakaammo iti adipenmo nga ipatakderam isuna iti balayna. Isu a, siak nga adipenmo, ket timmured nga agkararag kenka.
26 Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
Ita O Yahweh, sika ti Dios, a nangikari iti nasayaat a kari iti adipenmo:
27 Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
Ita, naay-ayoka a mangbendision iti balay daytoy adipenmo, nga agtultuloy koma iti agnanayon iti sangoanam. Sika O Yahweh ti nangbendision iti daytoy, ket nagasatto daytoy iti agnanayon.”