< 1 Mbiri 17 >
1 Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
And it came to pass as David lived in his house, that David said to Nathan the prophet, Behold, I dwell in a house of cedar, but the ark of the covenant of the Lord [is] under [curtains] of skins.
2 Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
And Nathan said to David, Do all that is in your heart; for God [is] with you.
3 Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
And it came to pass in that night, that the word of the Lord came to Nathan, [saying],
4 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
Go and say to David my servant, Thus said the Lord, You shall not build me a house for me to dwell in it.
5 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
For I have not lived in a house from the day that I brought up Israel until this day, but I have been in a tabernacle and a tent,
6 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
in all places through which I have gone with all Israel: did I ever speak to [any] one tribe of Israel whom I commanded to feed my people, saying, [Why is it] that you have not built me a house of cedar?
7 Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
And now thus shall you say to my servant David, Thus says the Lord Almighty, I took you from the sheepfold, from following the flocks, to be a ruler over my people Israel:
8 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
and I was with you in all places whither you went, and I destroyed all your enemies from before you, and I made for you a name according to the name of the great ones that are upon the earth.
9 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
And I will appoint a place for my people Israel, and I will plant him, and he shall dwell by himself, and shall no longer be anxious; and the son of iniquity shall no longer afflict him, as at the beginning,
10 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
and from the days when I appointed judges over my people Israel. Also I have humbled all your enemies, and I will increase you, and the Lord will build you a house.
11 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
And it shall come to pass when your days shall be fulfilled, and you shall sleep with your fathers, that I will raise up your seed after you, which shall be of your bowels, and I will establish his kingdom.
12 Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
He shall build me a house, and I will set up his throne for ever.
13 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
I will be to him a father, and he shall be to me a son: and my mercy will I not withdraw from him, as I withdrew [it] from them that were before you.
14 Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
And I will establish him in my house and in his kingdom for ever; and his throne shall be set up for ever.
15 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
According to all these words, and according to all this vision, so spoke Nathan to David.
16 Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
And king David came and sat before the Lord, and said, Who am I, O Lord God? and what [is] my house, that you have loved me for ever?
17 Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
And these things were little in your sight, O God: you have also spoken concerning the house of your servant for a long time to come, and you have looked upon me as a man looks upon his fellow, and have exalted me, O Lord God.
18 “Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
What shall David do more toward you to glorify [you]? and you know your servant.
19 Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
And you have wrought all this greatness according to your heart.
20 “Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
O Lord, there is none like you, and there is no God beside you, according to all things which we have heard with our ears.
21 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
Neither is there another nation upon the earth [such] as your people Israel, whereas God led him in the way, to redeem a people for himself, to make for himself a great and glorious name, to cast out nations from before your people, whom you redeemed out of Egypt.
22 Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
And you have appointed your people Israel as a people to yourself for ever; and you, Lord, did become a God to them.
23 “Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
And now, Lord, let the word which you spoke to your servant, and concerning his house, be confirmed for ever, and do you as you have spoken.
24 kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
And let your name [be] established and magnified for ever, [men] saying, Lord, Lord, Almighty God of Israel: and [let] the house of your servant David [be] established before you.
25 “Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
For you, O Lord my God, have revealed to the ear of your servant that you will build him a house; therefore your servant has found a willingness to pray before you.
26 Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
And now, Lord, you yourself are God, and you have spoken these good things concerning your servant.
27 Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
And now you have begun to bless the house of your servant, so that it should continue for ever before you: for you, Lord, have blessed [it], and do you bless [it] for ever.