< 1 Mbiri 17 >

1 Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”
Bangʼ ka Daudi nosedonjo e ode mar ruoth, nowacho ni Nathan janabi niya, “Koro anto adak e od ruoth moger gi yiend sida, to Sandug Muma mar singruok mar Jehova Nyasaye to osiko e bwo hema.”
2 Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”
Nathan nodwoko Daudi niya, “gimoro amora manie chunyi to dhi nyime mondo itim nikech Nyasaye ni kodi.”
3 Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,
Otienono wach mar Nyasaye nobiro ni Nathan kawacho niya,
4 “Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’
“Dhiyo mondo inyis jatichna Daudi niya, ‘Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: In ok nigerna ot mondo adagie.
5 Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena.
Pok adak e ot chakre ndalo mane agolo jo-Israel e piny Misri nyaka kawuono. Asebedo kawuotho e kuonde mogurie hema ka adar e kuonde dak mopogore.
6 Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
Kuonde duto masewuothoe gi jo-Israel duto, bende asewachoe ni jotendgi mane aketo jokwadh joga niya, “Angʼo momiyo pok ugerona ot mar yiend sida?”’
7 Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli.
“Omiyo koro wach ni jatichna Daudi niya, ‘Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego wacho kama: Ne agoli e lek kuma ne ikwayoe rombe mondo ibed jatend joga Israel.
8 Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
Asebedo kodi kuonde duto misedhiye, kendo asetieko wasiki duto e nyimi. Koro abiro miyo nyingi bed kaka humb jomadongo manie piny.
9 Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja;
Kendo abiro chiwo piny ni joga Israel kendo abiro gurogi mondo gibed gi pinygi giwegi mondo kik chandgi kendo. Jomahundu ok nochak osandgi kendo kaka negitimonegi mokwongo,
10 monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse. “‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako.
kendo kaka gisetimo nyaka chakre ne ayier jotelo marito joga Israel. Bende abiro loyo wasiki duto. “‘Awachoni ni Jehova Nyasaye biro geroni ot:
11 Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
Ka ndaloni orumo mitho kendo iluwo kwereni, to abiro keto kothi moro mondo okaw kari, achiel kuom yawuoti minywolo kendo anagur pinyruodhe.
12 Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
En ema noger ot ni nyinga kendo anagur lochne osik nyaka chiengʼ.
13 Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo.
Anabed wuon-gi, to enobed wuoda. Ok nagol herana kuome kaka ne agolo herana kuom ruoth mane ikawo loch kuome.
14 Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’”
Anakete motegno e oda kendo kuom pinyruodhe nyaka chiengʼ, lochne nogur motegno manyaka chiengʼ.’”
15 Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
Nathan nonyiso Daudi weche duto mane ofwenyne.
16 Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati, “Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?
Eka Ruoth Daudi nodonjo e hema mobet piny e nyim Jehova Nyasaye mowacho niya, “An to an ngʼa, yaye Jehova Nyasaye, to jooda to gin ngʼa gini momiyo isetimona gigi duto?
17 Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”
To ka gima kamano ok oromo e nyim wangʼi, yaye Jehova Nyasaye, to isewuoyo kuom gima biro timore e od jatichni. Isengʼiya mana ka gima an ngʼat motingʼ malo moloyo ji duto, yaye Jehova Nyasaye.
18 “Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu.
“En angʼo ma Daudi dimed wachoni kuom duongʼ ma isemiyo jatichni? Nikech ingʼeyo jatichni,
19 Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.
yaye Jehova Nyasaye. Nikech wach misewacho kendo koluwore gi dwaroni, isetimo tim maduongʼni bende isemiyo singruok madongogi ongʼere.
20 “Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu.
“Yaye Jehova Nyasaye, onge ngʼama chalo kodi kendo onge Nyasaye moro makmana in, mana kaka wasewinjo gi itwa wawegi.
21 Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
Ere oganda machal gi jogi Israel? Bende nitiere oganda moro mane Nyasache osedhi moreso ka gin wasumbini milokogi jogi? Donge isemiyo nyingi duongʼ kuom timbe madongo kendo malich, nimar iseriembo ogendini mamoko e nyim jogi mane ireso kigolo Misri?
22 Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
Ne imiyo jogi ma jo-Israel obedo jogi iwuon nyaka chiengʼ to bende in Jehova Nyasaye isebedo Nyasachgi.
23 “Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera,
“To koro Jehova Nyasaye, mi singruok misetimo kuom jatichni kod ode mondo ogurre nyaka chiengʼ. Tim mana kaka ne isingori,
24 kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
mondo mi ogurre kendo nyingi obed maduongʼ nyaka chiengʼ. Eka ji biro wacho ni, ‘Jehova Nyasaye Maratego, en Nyasach jo-Israel!’ Kendo dhood jatichni Daudi nogurre e nyimi.
25 “Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
“In, Nyasacha isefwenyo ni jatichni ni ibiro gerona ot omiyo jatichni osebet gi chir mondo olami.
26 Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
Yaye Jehova Nyasaye, in e Nyasaye! Kendo isesingo gik mabeyogi ni jatichni.
27 Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”
Emomiyo iseyie mondo igwedh od jatichni mondo osik e nyimi nyaka chiengʼ nikech isegwedhe kendo inigwedhe nyaka chiengʼ, yaye Jehova Nyasaye.”

< 1 Mbiri 17 >