< 1 Mbiri 16 >

1 Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
Basebewuletha umtshokotsho kaNkulunkulu, bawumisa phakathi kwethente uDavida ayelimisele wona; basebenikela iminikelo yokutshiswa leminikelo yokuthula phambi kukaNkulunkulu.
2 Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
UDavida eseqedile ukunikela umnikelo wokutshiswa leminikelo yokuthula wababusisa abantu ebizweni leNkosi.
3 Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
Wasesabela wonke umuntu wakoIsrayeli kusukela kowesilisa kuze kube kowesifazana, kwaba ngulowo lalowo isinkwa esisodwa, leqatha lenyama, lesinkwa sezithelo zevini ezonyisiweyo.
4 Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
Wasemisa izikhonzi kumaLevi phambi komtshokotsho weNkosi, ngitsho ukukhumbula lokubonga lokudumisa iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli.
5 Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
UAsafi inhloko, lowesibili kuye uZekhariya, uJeyiyeli, loShemiramothi, loJehiyeli, loMathithiya, loEliyabi, loBhenaya, loObedi-Edoma, loJeyiyeli belezinto zezigubhu zezintambo njalo lamachacho; uAsafi wasezizwakalisa ngezinsimbi ezincencethayo;
6 ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
loBhenaya loJahaziyeli abapristi ngezimpondo njalonjalo phambi komtshokotsho wesivumelwano sikaNkulunkulu.
7 Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
Ngalesosikhathi ngalolosuku uDavida wanika kuqala lesisihlabelelo ukudumisa iNkosi ngesandla sikaAsafi labafowabo:
8 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
Bongani iNkosi, libize ibizo layo, lazise phakathi kwabantu izenzo zayo.
9 Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
Hlabelelani kuyo, liyihubele amahubo, lilandise ngezenzo zayo ezimangalisayo.
10 Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
Zincomeni ebizweni layo elingcwele, kayithokoze inhliziyo yabo abadinga iNkosi.
11 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
Dingani iNkosi lamandla ayo, lidinge ubuso bayo njalonjalo.
12 Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
Khumbulani izimangaliso zayo eyazenzayo, izibonakaliso zayo, lezahlulelo zomlomo wayo,
13 inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
nzalo kaIsrayeli inceku yayo, bantwana bakaJakobe, abakhethiweyo bayo.
14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
IyiNkosi uNkulunkulu wethu; izahlulelo zayo zisemhlabeni wonke.
15 Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
Khumbulani isivumelwano sayo kuze kube nininini, ilizwi eyalilaya kuzinkulungwane zezizukulwana,
16 pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
eyasenza loAbrahama, lesifungo sakhe kuIsaka,
17 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
eyasiqinisa lakuJakobe saba yisimiso, kuIsrayeli saba yisivumelwano esilaphakade,
18 “Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
isithi: Ngizakunika ilizwe leKhanani, inkatho yelifa lakho.
19 Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
Lapho lalibalutshwana ngenani, yebo libalutshwana, njalo liyizihambi kulo.
20 iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
Basebezula besuka esizweni besiya esizweni, besuka embusweni besiya kwabanye abantu.
21 Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
Kayivumelanga muntu ukubacindezela; yebo yakhuza amakhosi ngenxa yabo:
22 “Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
Lingathinti abagcotshiweyo bami, lingoni abaprofethi bami.
23 Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Hlabelelani eNkosini, mhlaba wonke, litshumayele insuku ngensuku usindiso lwayo.
24 Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
Landisani udumo lwayo phakathi kwezizwe, izimangaliso zayo phakathi kwabantu bonke.
25 Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
Ngoba yinkulu iNkosi, ifanele ukudunyiswa kakhulu, iyesabeka phezu kwabonkulunkulu bonke.
26 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
Ngoba bonke onkulunkulu bezizwe bayizithombe; kodwa iNkosi yenza amazulu.
27 Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
Udumo lenkazimulo kuphambi kwayo, amandla lentokozo kusendaweni yayo.
28 Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
Inikeni iNkosi, zizukulwana zezizwe, inikeni iNkosi udumo lamandla.
29 perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
Inikeni iNkosi udumo lwebizo layo, lethani umnikelo lize phambi kwayo. Ikhonzeni iNkosi ebuhleni bobungcwele.
30 Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
Lithuthumele phambi kwayo, mhlaba wonke; njalo umhlaba uzaqiniswa, kawuyikunyikinyeka.
31 Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
Kawathokoze amazulu, lomhlaba ujabule, kabatsho phakathi kwezizwe ukuthi: INkosi iyabusa.
32 Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
Kaluhlokome ulwandle lokugcwala kwalo, iganga kalithabe lakho konke okukulo.
33 Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
Khona zizahlabelela ngentokozo izihlahla zehlathi phambi kweNkosi, ngoba iyeza ukwahlulela umhlaba.
34 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
Bongani iNkosi ngoba ilungile, ngoba umusa wayo umi kuze kube phakade.
35 Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
Lithi futhi: Sisindise, Nkulunkulu wosindiso lwethu, usibuthe usikhulule ezizweni, ukuze sibonge ibizo lakho elingcwele, sizincome kudumo lwakho.
36 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
Kayibusiswe iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, kusukela phakade kuze kube phakade. Bonke abantu basebesithi: Ameni. Basebeyidumisa iNkosi.
37 Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
Wasetshiya lapho phambi komtshokotsho wesivumelwano seNkosi oAsafi labafowabo ukukhonza phambi komtshokotsho njalonjalo njengodaba losuku ngosuku lwalo.
38 Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
LoObedi-Edoma kanye labafowabo, abangamatshumi ayisithupha lesificaminwembili; uObedi-Edoma indodana kaJeduthuni loHosa babengabagcini bamasango.
39 Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
LoZadoki umpristi labafowabo abapristi phambi kwethabhanekele leNkosi endaweni ephakemeyo eyayiseGibeyoni,
40 kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
ukuze banikele iminikelo yokutshiswa eNkosini phezu kwelathi lomnikelo wokutshiswa njalonjalo ekuseni lakusihlwa, lanjengakho konke okubhaliweyo emlayweni weNkosi, eyawulaya uIsrayeli.
41 Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
Njalo kanye labo oHemani loJeduthuni labanye ababekhethiwe abamiswa ngamabizo ukubonga iNkosi, ngoba umusa wayo umi kuze kube phakade.
42 Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
Njalo kanye labo oHemani loJeduthuni babelezimpondo lezinsimbi ezincencethayo zalabo abazizwakalisayo, lezinto zokuhlabelela zikaNkulunkulu. Lamadodana kaJeduthuni ayesesangweni.
43 Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.
Basebehamba bonke abantu, ngulowo lalowo waya endlini yakhe. UDavida wasebuyela ukubusisa indlu yakhe.

< 1 Mbiri 16 >