< 1 Mbiri 15 >
1 Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
David si je v Davidovem mestu zgradil hiše in pripravil kraj za Božjo skrinjo in zanjo razpel šotor.
2 Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
Potem je David rekel: »Božje skrinje ne bi smel nositi nihče razen Lévijevcev, kajti njih je Gospod izbral, da nosijo Božjo skrinjo in da mu služijo na veke.«
3 Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
David je skupaj zbral ves Izrael v Jeruzalemu, da prinese gor Gospodovo skrinjo na kraj, ki ga je pripravil zanjo.
4 Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
David je zbral Aronove otroke in Lévijevce.
5 kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
Izmed Kehátovih sinov vodja Uriéla in sto dvajset njegovih bratov;
6 Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
izmed Meraríjevih sinov vodja Asajája in dvesto dvajset njegovih bratov;
7 kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
izmed Geršómovih sinov vodja Joéla in sto trideset njegovih bratov;
8 kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
izmed Elicafánovih sinov vodja Šemajá in dvesto njegovih bratov;
9 kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
izmed Hebrónovih sinov vodja Eliéla in osemdeset njegovih bratov;
10 kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
izmed Uziélovih sinov vodja Aminadába in sto dvanajst njegovih bratov.
11 Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
David je dal poklicati Cadóka, duhovnika Abjatárja in Lévijevce Uriéla, Asajá, Joéla, Šemajá, Eliéla in Aminadába
12 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
ter jim rekel: »Vi ste vodje očetov Lévijevcev. Posvetite se tako vi kakor vaši bratje, da boste lahko prinesli gor skrinjo Gospoda, Izraelovega Boga, na kraj, ki sem ga pripravil zanjo.
13 Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
Kajti ker tega niste najprej storili, je Gospod, naš Bog, nad nami naredil vrzel, ker ga nismo iskali po predpisanem redu.«
14 Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
Tako so se duhovniki in Lévijevci posvetili, da prinesejo gor skrinjo Gospoda, Izraelovega Boga.
15 Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
Lévijevi otroci so na svojih ramenih nosili Božjo skrinjo z njenima drogovoma v njej, kakor je zapovedal Mojzes, glede na Gospodovo besedo.
16 Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
David je spregovoril vodju Lévijevcev, da določi svoje brate, da bodo pevci z glasbenimi instrumenti, plunkami, harfami in cimbalami, z dvigovanjem zvenečega radostnega glasu.
17 Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
Tako so Lévijevci določili Joélovega sina Hemána in izmed njegovih bratov Berehjájevega sina Asáfa in izmed Meraríjevih sinov, njihovih bratov, Kušajájevega sina Etána
18 ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
in z njimi njihove brate druge stopnje: Zeharjája, Bena, Jaaziéla, Šemiramóta, Jehiéla, Uníja, Eliába, Benajája, Maasejája, Matitjája, Elifeléhuja, Miknejája, Obéd Edóma in Jeiéla, vratarje.
19 Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
Tako so bili pevci Hemán, Asáf in Etán določeni, da igrajo na cimbale iz brona,
20 Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
Zeharjá, Jaaziél, Šemiramót, Jehiél, Uní, Eliáb, Maasejá in Benajá s plunkami na sopran,
21 ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
in Matitjá, Elifeléhu, Miknejá, Obéd Edóm, Jeiél in Azazjá s harfami v oktavi, da vodijo.
22 Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
Kenanjá, vodja Lévijevcev, je bil za pesem. Poučil je glede pesmi, ker je bil vešč.
23 Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
Berehjá in Elkaná sta bila vratarja za skrinjo.
24 Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
Duhovniki Šebanjá, Józafat, Netanél, Amasáj, Zeharjá, Benajá in Eliézer so s trobentami trobili pred Božjo skrinjo; Obéd Edóm in Jehijá pa sta bila vratarja za skrinjo.
25 Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
Tako so David, Izraelove starešine in tisočniki odšli, da iz hiše Obéd Edóma z radostjo prinesejo gor Gospodovo skrinjo zaveze.
26 Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
Pripetilo se je, ko je Bog pomagal Lévijevcem, da so nosili skrinjo Gospodove zaveze, da so darovali sedem bikcev in sedem ovnov.
27 Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
David je bil oblečen s svečanim oblačilom iz tankega lanenega platna in vsi Lévijevci, ki so nosili skrinjo, pevci in Kenanjá, mojster pesmi s pevci; tudi David je imel na sebi efód iz lana.
28 Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
Tako je ves Izrael prinesel gor Gospodovo skrinjo zaveze z vriskanjem, z zvokom kornéta, s trobentami, cimbalami in igrali so s plunkami in harfami.
29 Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.
Pripetilo se je, medtem ko je Gospodova skrinja prišla v Davidovo mesto, da je Savlova hči Mihála, zroč skozi okno, videla kralja Davida plesati in igrati in ga v svojem srcu prezirala.