< 1 Mbiri 15 >

1 Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
A gdy [Dawid] zbudował sobie domy w mieście Dawida, przygotował miejsce dla arki Boga i rozbił jej namiot.
2 Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
Wtedy Dawid powiedział: Nie [wolno nikomu] nosić arki Boga oprócz Lewitów. Ich bowiem wybrał PAN, aby nosili arkę Boga i aby służyli mu na wieki.
3 Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
Dawid więc zebrał całego Izraela w Jerozolimie, aby przenieść arkę PANA na miejsce, które dla niej przygotował.
4 Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
Zgromadził też Dawid synów Aarona i Lewitów:
5 kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
Z synów Kehata: Uriela naczelnika i jego braci – stu dwudziestu;
6 Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
Z synów Merariego: Asajasza naczelnika i jego braci – dwustu dwudziestu;
7 kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
Z synów Gerszoma: Joela naczelnika i jego braci – stu trzydziestu;
8 kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
Z synów Elisafana: Szemajasza naczelnika i jego braci – dwustu;
9 kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
Z synów Chebrona: Eliela naczelnika i jego braci – osiemdziesięciu;
10 kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
Z synów Uzziela: Amminadaba naczelnika i jego braci – stu dwunastu.
11 Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
Wtedy Dawid wezwał kapłanów Sadoka i Abiatara oraz Lewitów: Uriela, Asajasza, Joela, Szemajasza, Eliela i Amminadaba;
12 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
I powiedział do nich: Jesteście naczelnikami rodów lewickich. Poświęćcie się wy i wasi bracia, abyście mogli przenieść arkę PANA, Boga Izraela, na miejsce, które dla niej przygotowałem.
13 Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
Ponieważ za pierwszym razem tego nie uczyniliście, PAN, nasz Bóg, zesłał na nas nieszczęście, bo nie szukaliśmy go tak, jak należy.
14 Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
Poświęcili się więc kapłani i Lewici, aby przenieść arkę PANA, Boga Izraela.
15 Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
Synowie Lewitów nieśli arkę Boga, jak rozkazał Mojżesz według słowa PANA, na swoich ramionach na drążkach, które przy niej były.
16 Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
Potem Dawid rozkazał naczelnikom Lewitów, aby ustanowili swoich braci śpiewakami przy instrumentach muzycznych: cytrach, harfach i cymbałach, aby rozbrzmiewał donośny głos pełen radości.
17 Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
Lewici ustanowili Hemana, syna Joela, a z jego braci – Asafa, syna Berechiasza, a z synów Merariego, ich braci – Etana, syna Kuszajasza;
18 ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
A z nimi braci ich drugiego [stopnia]: Zachariasza, Bena, Jaaziela, Szemiramota, Jechiela, Unniego, Eliaba, Benajasza, Maasejasza, Mattitiasza, Elifela, Miknejasza, Obed-Edoma i Jejela – odźwiernych.
19 Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
A śpiewacy Heman, Asaf i Etan grali głośno na cymbałach z brązu.
20 Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
Zachariasz, Jaziel, Szemiramot, Jechiel, Unni, Elijab, Maasejasz i Benajasz [grali] na cytrach na Alamot.
21 ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
A Mattitiasz, Elifel, Miknejasz, Obed-Edom, Jejel i Azaziasz [grali] na harfach na Seminit i prowadzili śpiew.
22 Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
A Kenaniasz, naczelnik Lewitów, odpowiadał za pieśni. Kierował śpiewaniem, bo był uzdolniony.
23 Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
Berekiasz i Elkana [byli] odźwiernymi przy arce.
24 Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
A kapłani: Szebaniasz, Joszafat, Netaneel, Amasaj, Zachariasz, Benajasz i Eliezer grali na trąbach przed arką Boga, a Obed-Edom i Jechiasz [byli] odźwiernymi przy arce.
25 Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
Tak więc Dawid, starsi Izraela i tysiącznicy wyruszyli, aby z radością przenieść arkę przymierza PANA z domu Obed-Edoma.
26 Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
I kiedy Bóg wspomógł Lewitów niosących arkę przymierza PANA, złożyli w ofierze siedem wołów i siedem baranów.
27 Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
A Dawid [był] ubrany w szatę z bisioru, podobnie jak wszyscy Lewici, którzy nieśli arkę, śpiewacy i Kenaniasz, kierujący śpiewem. Dawid miał także na sobie lniany efod.
28 Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
I w ten sposób cały Izrael prowadził arkę przymierza PANA wśród radosnych okrzyków, przy dźwięku kornetu, trąb i cymbałów, grając na cytrach i harfach.
29 Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.
I kiedy arka przymierza PANA wchodziła do miasta Dawida, Mikal, córka Saula, wyglądała przez okno i zobaczyła króla Dawida tańczącego i grającego. I wzgardziła nim w swoim sercu.

< 1 Mbiri 15 >