< 1 Mbiri 15 >

1 Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
Et il fit pour lui des maisons dans la ville de David, et prépara un lieu pour l’arche de Dieu, et tendit une tente pour elle.
2 Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
Alors David dit: Il ne convient pas que l’arche de Dieu soit portée par personne excepté les Lévites; car l’Éternel les a choisis pour porter l’arche de Dieu et pour en faire le service à toujours.
3 Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
Et David assembla tout Israël à Jérusalem, pour faire monter l’arche de l’Éternel au lieu qu’il lui avait préparé.
4 Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
Et David assembla les fils d’Aaron et les Lévites:
5 kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
des fils de Kehath, Uriel, le chef, et ses frères, 120 [hommes];
6 Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
des fils de Merari, Asçaïa, le chef, et ses frères, 220;
7 kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
des fils de Guershom, Joël, le chef, et ses frères, 130;
8 kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
des fils d’Élitsaphan, Shemahia, le chef, et ses frères, 200;
9 kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
des fils de Hébron, Éliel, le chef, et ses frères, 80;
10 kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
des fils d’Uziel, Amminadab, le chef, et ses frères, 112.
11 Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
Et David appela Tsadok et Abiathar, les sacrificateurs, et les Lévites, Uriel, Asçaïa, et Joël, Shemahia, et Éliel, et Amminadab;
12 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
et il leur dit: Vous êtes les chefs des pères des Lévites; sanctifiez-vous, vous et vos frères, et faites monter l’arche de l’Éternel, le Dieu d’Israël, au [lieu que] je lui ai préparé.
13 Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
Car, parce que vous ne l’avez pas [fait] la première fois, l’Éternel, notre Dieu, a fait une brèche parmi nous; car nous ne l’avons pas recherché conformément à l’ordonnance.
14 Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
Et les sacrificateurs et les Lévites se sanctifièrent pour faire monter l’arche de l’Éternel, le Dieu d’Israël.
15 Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
Et les fils des Lévites portèrent l’arche de Dieu sur leurs épaules, avec les barres sur eux, comme Moïse l’avait commandé, selon la parole de l’Éternel.
16 Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
Et David dit aux chefs des Lévites d’établir leurs frères, les chantres, avec des instruments de musique, des luths, et des harpes, et des cymbales, qu’ils feraient retentir en élevant leur voix avec joie.
17 Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
Et les Lévites établirent Héman, fils de Joël; et, d’entre ses frères, Asaph, fils de Bérékia; et, d’entre les fils de Merari, leurs frères, Éthan, fils de Kushaïa;
18 ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
et avec eux leurs frères du second rang: Zacharie, Ben, et Jaaziel, et Shemiramoth, et Jekhiel, et Unni, Éliab, et Benaïa, et Maascéïa, et Matthithia, et Éliphelé, et Miknéïa, et Obed-Édom, et Jehiel, les portiers.
19 Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
Et les chantres, Héman, Asaph, et Éthan, avec des cymbales d’airain, pour les faire retentir;
20 Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
et Zacharie, et Aziel, et Shemiramoth, et Jekhiel, et Unni, et Éliab, et Maascéïa, et Benaïa, avec des luths, sur [le mode] d’Alamoth;
21 ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
et Matthithia, et Éliphelé, et Miknéïa, et Obed-Édom, et Jehiel, et Azazia, avec des harpes sur [le mode] de Sheminith, pour diriger le chant.
22 Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
Et Kenania, le chef des Lévites pour la musique, enseignait la musique; car il était intelligent.
23 Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
Et Bérékia et Elkana étaient portiers pour l’arche.
24 Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
Et Shebania, et Josaphat, et Nethaneël, et Amasçaï, et Zacharie, et Benaïa, et Éliézer, les sacrificateurs, sonnaient avec des trompettes devant l’arche de Dieu; et Obed-Édom et Jekhija étaient portiers pour l’arche.
25 Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
Et David, et les anciens d’Israël, et les chefs de milliers, allèrent pour faire monter l’arche de l’alliance de l’Éternel, de la maison d’Obed-Édom, avec joie:
26 Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
et il arriva que, quand Dieu aida les Lévites qui portaient l’arche de l’alliance de l’Éternel, ils sacrifièrent sept veaux et sept béliers.
27 Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Et David était vêtu d’une robe de byssus, ainsi que tous les Lévites qui portaient l’arche, et les chantres, et Kenania, le chef de la musique des chantres; et David avait sur lui un éphod de lin.
28 Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
Et tout Israël faisait monter l’arche de l’alliance de l’Éternel avec des cris de joie, et au son du cor, et avec des trompettes et des cymbales, et en faisant retentir des luths et des harpes.
29 Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.
Et comme l’arche de l’alliance de l’Éternel arrivait à la ville de David, Mical, fille de Saül, regarda par la fenêtre, et elle vit le roi David sautant et jouant, et elle le méprisa dans son cœur.

< 1 Mbiri 15 >