< 1 Mbiri 15 >

1 Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
David made himself houses in David’s city; and he prepared a place for God’s ark, and pitched a tent for it.
2 Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
Then David said, “No one ought to carry God’s ark but the Levites. For the LORD has chosen them to carry God’s ark, and to minister to him forever.”
3 Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
David assembled all Israel at Jerusalem, to bring up the LORD’s ark to its place, which he had prepared for it.
4 Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
David gathered together the sons of Aaron and the Levites:
5 kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
of the sons of Kohath, Uriel the chief, and his brothers one hundred and twenty;
6 Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
of the sons of Merari, Asaiah the chief, and his brothers two hundred and twenty;
7 kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
of the sons of Gershom, Joel the chief, and his brothers one hundred and thirty;
8 kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
of the sons of Elizaphan, Shemaiah the chief, and his brothers two hundred;
9 kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
of the sons of Hebron, Eliel the chief, and his brothers eighty;
10 kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
of the sons of Uzziel, Amminadab the chief, and his brothers one hundred and twelve.
11 Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
David called for Zadok and Abiathar the priests, and for the Levites: for Uriel, Asaiah, Joel, Shemaiah, Eliel, and Amminadab,
12 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
and said to them, “You are the heads of the fathers’ households of the Levites. Sanctify yourselves, both you and your brothers, that you may bring the ark of the LORD, the God of Israel, up to the place that I have prepared for it.
13 Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
For because you didn’t carry it at first, the LORD our God broke out in anger against us, because we didn’t seek him according to the ordinance.”
14 Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
So the priests and the Levites sanctified themselves to bring up the ark of the LORD, the God of Israel.
15 Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
The children of the Levites bore God’s ark on their shoulders with its poles, as Moses commanded according to the LORD’s word.
16 Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
David spoke to the chief of the Levites to appoint their brothers as singers with instruments of music, stringed instruments, harps, and cymbals, sounding aloud and lifting up their voices with joy.
17 Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
So the Levites appointed Heman the son of Joel; and of his brothers, Asaph the son of Berechiah; and of the sons of Merari their brothers, Ethan the son of Kushaiah;
18 ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
and with them their brothers of the second rank: Zechariah, Ben, Jaaziel, Shemiramoth, Jehiel, Unni, Eliab, Benaiah, Maaseiah, Mattithiah, Eliphelehu, Mikneiah, Obed-Edom, and Jeiel, the doorkeepers.
19 Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
So the singers, Heman, Asaph, and Ethan, were given cymbals of bronze to sound aloud;
20 Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
and Zechariah, Aziel, Shemiramoth, Jehiel, Unni, Eliab, Maaseiah, and Benaiah, with stringed instruments set to Alamoth;
21 ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
and Mattithiah, Eliphelehu, Mikneiah, Obed-Edom, Jeiel, and Azaziah, with harps tuned to the eight-stringed lyre, to lead.
22 Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
Chenaniah, chief of the Levites, was over the singing. He taught the singers, because he was skilful.
23 Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
Berechiah and Elkanah were doorkeepers for the ark.
24 Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
Shebaniah, Joshaphat, Nethanel, Amasai, Zechariah, Benaiah, and Eliezer, the priests, blew the shofars before God’s ark; and Obed-Edom and Jehiah were doorkeepers for the ark.
25 Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
So David, the elders of Israel, and the captains over thousands went to bring the ark of the LORD’s covenant up out of the house of Obed-Edom with joy.
26 Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
When God helped the Levites who bore the ark of the LORD’s covenant, they sacrificed seven bulls and seven rams.
27 Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
David was clothed with a robe of fine linen, as were all the Levites who bore the ark, the singers, and Chenaniah the choir master with the singers; and David had an ephod of linen on him.
28 Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
Thus all Israel brought the ark of the LORD’s covenant up with shouting, with sound of the cornet, with shofars, and with cymbals, sounding aloud with stringed instruments and harps.
29 Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.
As the ark of the LORD’s covenant came to David’s city, Michal the daughter of Saul looked out at the window, and saw king David dancing and playing; and she despised him in her heart.

< 1 Mbiri 15 >