< 1 Mbiri 15 >

1 Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
Siden byggede han sig Huse i Davidsbyen og beredte Guds Ark et Sted, idet han rejste den et Telt
2 Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
Ved den Lejlighed sagde David: "Ingen andre end Leviterne må bære Guds Ark, thi dem har HERREN udvalgt til at bære Guds Ark og til at gøre Tjeneste for ham til evig Tid."
3 Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
Og David samlede hele Israel i Jerusalem for at føre HERRENs Ark op til det Sted, han havde beredt den.
4 Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
Og David samlede Arons Sønner og Leviterne:
5 kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
Af Kehatiterne Øversten Uriel og hans Brødre, 120;
6 Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
af Merariterne Øversten Asaja og hans Brødre, 220;
7 kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
af Gersoniterne Øversten Joel og hans Brødre, 130;
8 kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
af Elizafans Sønner Øversten Sjemaja og hans Brødre, 200;
9 kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
af Hebrons Sønner Øversten Eliel og hans Brødre, 80;
10 kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
af Uzziels Sønner Øversten Amminadab og hans Brødre, 112.
11 Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
Så lod David Præsterne Zadok og Ebjatar og Leviterne Uriel, Asaja, Joel, Sjemaja, Eliel og Amminadab kalde
12 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
og sagde til dem: "I er Overhoveder for Leviternes Fædrenehuse; helliger eder tillige med eders Brødre og før HERRENs, Israels Guds, Ark op til det Sted, jeg har beredt den;
13 Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
det var jo, fordi I ikke var med første Gang, at HERREN vor Gud tilføjede os et Brud; thi vi søgte ham ikke på rette Måde."
14 Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
Så helligede Præsferne og Leviterne sig for at føre HERRENs, Israels Guds, Ark op;
15 Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
og Levis Sønner løftede med Bærestængerne Guds Ark op på Skuldrene, som Moses havde påbudt efter HERRENS Ord.
16 Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
Fremdeles bød David Leviternes Øverster at lade deres Brødre Sangerne stille sig op med Musikinstrumenter, Harper, Citre og Cymbler og lade høje Jubeltoner klinge.
17 Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
Så lod Leviterne Heman, Joels Søn, og af hans Brødre Asaf, Berekjas Søn, og af deres Brødre Merariterne Etan, Husjajas Søn, stille sig op
18 ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
og ved Siden af dem deres Brødre af anden Rang Zekarja, Uzziel, Sjemiramot, Jehiel, Unni, Eliab, Benaja, Ma'aseja, Mattitja, Elipelehu og Miknejahu og Dørvogterne Obed-Edom og Je'iel;
19 Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
Sangerne Heman, Asaf og Etan skulde spille på Kobbercymbler,
20 Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
Zekarja, Uzziel, Sjemiramot, Jehiel, Unni, Eliab, Ma'aseja og Benaja på Harper al-alamot;
21 ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
Mattitja, Elipelehu, Miknejahu, Obed-Edom og Je'iel skulde lede Sangen med Citre al-hassjeminit;
22 Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
Konanja, Leviternes Øverste over dem, der bar, skulde lede disse, da han forstod sig derpå;
23 Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
Berekja og Elkana skulde være Dørvogtere ved Arken;
24 Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
Præsterne Sjebanja, Josjafat, Netan'el, Amasaj, Zekarja, Benaja og Eliezer skulde blæse i Trompeterne foran Guds Ark; og Obed-Edom og Jehija skulde være Dørvogtere ved Arken.
25 Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
Derpå drog David, Israels Ældste og Tusindførerne hen for under Festglæde at lade HERRENs Pagts Ark bringe op fra Obed-Edoms Hus,
26 Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
og da Gud hjalp Leviterne, der har HERRENs Pagts Ark, ofrede man syv Tyre og syv Vædre.
27 Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
David har en fin linned Kappe, ligeledes alle Leviterne, der har Arken, og Sangerne og Konanja, som ledede dem, der bar. Og David var iført en linned Efod.
28 Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
Og hele Israel bragte HERRENs Pagts Ark op under Festjubel og til Hornets, Trompeternes og Cymblernes Klang, under Harpe- og Citerspil.
29 Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.
Men da HERRENs Pagts Ark kom til Davidsbyen, så Sauls Datter Mikal ud af Vinduet, og da hun så Kong David springe og danse, ringeagtede hun ham i sit Hjerte.

< 1 Mbiri 15 >