< 1 Mbiri 14 >

1 Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu.
Hiram king of Tyre sent messengers to David, and cedar trees, and craftsmen of a wall, and craftsmen of wood, to build him a palace.
2 Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
And David knew that the LORD had established him king over Israel; for his kingdom was exalted on high, for his people Israel's sake.
3 Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
David took more wives at Jerusalem; and David became the father of more sons and daughters.
4 Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
These are the names of the children whom he had in Jerusalem: Shammua, and Shobab, Nathan, and Solomon,
5 Ibihari, Elisua, Elipeleti,
and Ibhar, and Elishua, and Eliphelet,
6 Noga, Nefegi, Yafiya,
and Nogah, and Nepheg, and Japhia,
7 Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.
and Elishama, and Baaliada, and Eliphelet.
8 Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo.
When the Philistines heard that David was anointed king over all Israel, all the Philistines went up to seek David: and David heard of it, and went out against them.
9 Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu.
Now the Philistines had come and made a raid in the Valley of Rephaim.
10 Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”
David inquired of God, saying, "Shall I go up against the Philistines? Will you deliver them into my hand?" The LORD said to him, "Go up; for I will deliver them into your hand."
11 Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu.
So they came up to Baal Perazim, and David struck them there; and David said, God has broken through my enemies by my hand, like a breakthrough of waters. Therefore they called the name of that place Baal Perazim.
12 Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.
They left their gods there; and David gave commandment, and they were burned with fire.
13 Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo.
The Philistines yet again made a raid in the valley.
14 Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
And David inquired again of God; and God said to him, "You shall not go up after them. Turn away from them, and come at them opposite the poplar trees.
15 Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
And it shall be, when you hear the sound of marching in the tops of the poplar trees, that then you shall go out to battle; for God has gone out before you to strike the army of the Philistines."
16 Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.
David did as God commanded him, and he struck the army of the Philistines from Gibeon even to Gezer.
17 Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.
The fame of David went out into all lands; and the LORD brought the fear of him on all nations.

< 1 Mbiri 14 >