< 1 Mbiri 13 >

1 Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
И Давид учини веће с хиљадницима и са стотиницима и са свим војводама,
2 Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
И рече Давид свему збору Израиљевом: Ако вам је по вољи, и ако је од Господа Бога нашег, да пошаљемо на све стране к браћи својој осталој по свим крајевима Израиљевим, и к свештеницима и Левитима по градовима и подграђима њиховим да се скупе к нама,
3 Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
Па да донесемо к себи ковчег Бога свог, јер Га не тражисмо за времена Сауловог.
4 Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
А сав збор рече да се тако учини, јер то би по вољи свему народу.
5 Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
И тако Давид сабра сав народ Израиљев од Сихора мисирског дори до Емата, да донесу ковчег Божији из Киријат-Јарима.
6 Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
И отиде Давид са свим Израиљем у Валу, у Киријат-Јарим Јудин, да пренесу оданде ковчег Бога Господа, који седи на херувимима, чије се име призива.
7 Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
И повезоше ковчег Божији на новим колима из куће Авинадавове; а Уза и Ахијо управљаху колима.
8 Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
А Давид и сав народ Израиљем играху пред Богом из све снаге певајући и ударајући у гусле и у псалтире и у бубње и у кимвале и трубећи у трубе.
9 Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
А кад дођоше до гумна Хидоновог, Уза се маши руком да прихвати ковчег јер волови потегоше на страну.
10 Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
И Господ се разгневи на Узу, и удари га што се маши руком за ковчег, те умре онде пред Богом.
11 Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
И ожалости се Давид што Господ уби Узу: Зато се прозва оно место Фарес-Уза до данас.
12 Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
И уплаши се Давид од Бога у онај дан, и рече: Како ћу донети к себи ковчег Божји?
13 Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
И не пренесе Давид ковчег к себи у град Давидов, него га склони у кућу Овид-Едома Гетејина.
14 Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.
И оста ковчег Божји код породице Овид-Едомове у кући његовој три месеци. И Господ благослови дом Овид-Едомов и све што имаше.

< 1 Mbiri 13 >