< 1 Mbiri 13 >

1 Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
Or David tint conseil avec les chefs de milliers et de centaines, avec tous les conducteurs du peuple.
2 Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
Et David dit à toute l'assemblée d'Israël: S'il vous semble bon, et que cela vienne de l'Éternel, notre Dieu, envoyons de tous côtés vers nos autres frères qui restent dans toutes les contrées d'Israël, et aussi vers les sacrificateurs et les Lévites, dans leurs villes à banlieues, afin qu'ils se réunissent à nous,
3 Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
Et ramenons auprès de nous l'arche de notre Dieu; car nous ne l'avons point recherchée du temps de Saül.
4 Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
Et toute l'assemblée décida de faire ainsi, car la chose fut approuvée par tout le peuple.
5 Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
David assembla donc tout Israël, depuis le Shichor d'Égypte, jusqu'à l'entrée de Hamath, pour ramener l'arche de Dieu de Kirjath-Jearim.
6 Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
Et David monta avec tout Israël à Baala, à Kirjath-Jearim qui est à Juda, pour faire monter de là l'arche de Dieu, l'Éternel, qui habite entre les chérubins, et dont le nom y est invoqué.
7 Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
Ils mirent donc l'arche de Dieu sur un chariot neuf, et l'emmenèrent de la maison d'Abinadab; et Uzza et Achjo conduisaient le chariot.
8 Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
Et David et tout Israël dansaient devant Dieu de toute leur force, en chantant, et en jouant des harpes, des lyres, des tambourins, des cymbales et des trompettes.
9 Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
Quand ils furent venus jusqu'à l'aire de Kidon, Uzza étendit la main pour retenir l'arche, parce que les bœufs regimbaient.
10 Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
Mais la colère de l'Éternel s'enflamma contre Uzza, et il le frappa, parce qu'il avait étendu la main sur l'arche; et il mourut là devant Dieu.
11 Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
Et David fut affligé de ce que l'Éternel avait fait une brèche, en la personne d'Uzza; et on a appelé jusqu'à ce jour ce lieu Pérets-Uzza (Brèche d'Uzza).
12 Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
David eut peur de Dieu en ce jour-là, et il dit: Comment ferais-je entrer chez moi l'arche de Dieu?
13 Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
Aussi David ne retira pas l'arche chez lui, dans la cité de David; mais il la fit conduire dans la maison d'Obed-Édom, le Guitthien.
14 Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.
L'arche de Dieu resta trois mois avec la famille d'Obed-Édom, dans sa maison. Et l'Éternel bénit la maison d'Obed-Édom et tout ce qui était à lui.

< 1 Mbiri 13 >