< 1 Mbiri 12 >

1 Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
Och dessa voro de som kommo till David i Siklag, medan han ännu höll sig undan för Saul, Kis' son; de hörde till de hjältar som bistodo honom under kriget.
2 Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
De voro väpnade med båge och skickliga i att, både med höger och med vänster hand, slunga stenar och avskjuta pilar från bågen. Av Sauls stamfränder, benjaminiterna, kommo:
3 Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
Ahieser, den förnämste, och Joas, gibeatiten Hassemaas söner; Jesuel och Pelet, Asmavets söner; Beraka; anatotiten Jehu;
4 ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
gibeoniten Jismaja, en av de trettio hjältarna, anförare för de trettio; Jeremia; Jahasiel; Johanan; gederatiten Josabad;
5 Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
Eleusai; Jerimot; Bealja; Semarja; harufiten Sefatja;
6 Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
koraiterna Elkana, Jissia, Asarel, Joeser och Jasobeam;
7 ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
Joela och Sebadja, söner till Jeroham, av strövskaran.
8 Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
Och av gaditerna avföllo några och gingo till David i bergfästet i öknen, tappra män, krigsmän skickliga att strida, rustade med sköld och spjut; de hade en uppsyn såsom lejon och voro snabba såsom gaseller på bergen:
9 Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
Eser, den förnämste, Obadja, den andre, Eliab, den tredje,
10 wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
Masmanna, den fjärde, Jeremia, den femte,
11 wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
Attai, den sjätte, Eliel, den sjunde,
12 wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
Johanan, den åttonde, Elsabad, den nionde,
13 wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
Jeremia, den tionde, Makbannai, den elfte.
14 Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
Dessa hörde till Gads barn och till de förnämsta i hären; den ringaste av dem var ensam så god som hundra, men den ypperste så god som tusen.
15 Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
Dessa voro de som i första månaden gingo över Jordan, när den var full över alla sina bräddar, och som förjagade alla dem som bodde i dalarna, åt öster och åt väster.
16 Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
Av Benjamins och Juda barn kommo några män till David ända till bergfästet.
17 Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
Då gick David ut emot dem och tog till orda och sade till dem: "Om I kommen till mig i fredlig avsikt och viljen bistå mig, så är mitt hjärta redo till förening med eder; men om I kommen för att förråda mig åt mina ovänner, fastän ingen orätt är i mina händer, då må våra fäders Gud se därtill och straffa det."
18 Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
Men Amasai, den förnämste bland de trettio, hade blivit beklädd med andekraft, och han sade: "Dina äro vi, David, och med dig stå vi, du Isais son. Frid vare med dig, frid, och frid vare med dem som bistå dig ty din Gud har bistått dig!" Och David tog emot dem och gav dem plats bland de förnämsta i sin skara.
19 Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
Från Manasse gingo några över till David, när han med filistéerna drog ut i strid mot Saul, dock fingo de icke bistå dessa; ty när filistéernas hövdingar hade rådplägat, skickade de bort honom, i det de sade: "Det gäller huvudet för oss, om han går över till sin herre Saul.
20 Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
När han då drog till Siklag, gingo dessa från Manasse över till honom: Adna, Josabad, Jediael, Mikael, Josabad, Elihu och Silletai, huvudmän för de ätter som tillhörde Manasse.
21 Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
Dessa bistodo David mot strövskaran, ty de voro allasammans tappra stridsmän och blevo hövitsmän i hären.
22 Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
Dag efter dag kommo nämligen allt flera till David för att bistå honom, så att hans läger blev övermåttan stort.
23 Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
Detta är de tal som angiva summorna av det väpnade krigsfolk som kom till David i Hebron, för att efter HERRENS befallning flytta Sauls konungamakt över på honom:
24 Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
Juda barn, som buro sköld och spjut, sex tusen åtta hundra, väpnade till strid;
25 Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
av Simeons barn tappra krigsmän, sju tusen ett hundra;
26 Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
av Levi barn fyra tusen sex hundra;
27 mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
därtill Jojada, fursten inom Arons släkt, och med honom tre tusen sju hundra;
28 ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
så ock Sadok, en tapper yngling, med sin familj, tjugutvå hövitsmän;
29 Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
av Benjamins barn, Sauls stamfränder, tre tusen (ty ännu vid den tiden höllo de flesta av dem troget med Sauls hus);
30 Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
av Efraims barn tjugu tusen åtta hundra, tappra stridsmän, namnkunniga män i sina familjer;
31 Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
av ena hälften av Manasse stam aderton tusen namngivna män, som kommo för att göra David till konung;
32 Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
av Isaskars barn kommo män som väl förstodo tidstecknen och insågo vad Israel borde göra, två hundra huvudmän, därtill alla deras stamfränder under deras befäl;
33 Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
av Sebulon stridbara män, rustade till krig med alla slags vapen, femtio tusen, som samlades endräktigt;
34 Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
av Naftali ett tusen hövitsmän, och med dem trettiosju tusen, väpnade med sköld och spjut;
35 Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
av daniterna krigsrustade män, tjuguåtta tusen sex hundra;
36 Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
av Aser stridbara män, rustade till krig, fyrtio tusen;
37 Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
och från andra sidan Jordan, av rubeniterna, gaditerna och andra hälften av Manasse stam, ett hundra tjugu tusen, väpnade med alla slags vapen som brukas vid krigföring.
38 Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
Alla dessa krigsmän, ordnade till strid, kommo i sina hjärtans hängivenhet till Hebron för att göra David till konung över hela Israel. Också hela det övriga Israel var enigt i att göra David till konung.
39 Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
Och de voro där hos David i tre dagar och åto och drucko, ty deras bröder hade försett dem med livsmedel.
40 Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.
De som bodde närmast dem, ända upp till Isaskar, Sebulon och Naftali, tillförde dem ock på åsnor, kameler, mulåsnor och oxar livsmedel i myckenhet till föda: mjöl, fikonkakor och russinkakor, vin och olja, fäkreatur och småboskap; ty glädje rådde i Israel.

< 1 Mbiri 12 >