< 1 Mbiri 12 >

1 Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
A IA hoi ka poe i hele mai io Davida la ma Zikelaga, i kona manawa i noho paa ai no Saula ke keiki a Kisa; iwaena lakou o na kanaka ikaika, ka poe i kokua i ke kaua.
2 Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
Ua makaukau lakou i na kakaka, a ua hiki no ia lakou ke nou aku i na pohaku, a me ka pana pua mailoko aku o ke kakaka, me ka lima akau a me ka lima hema, no ka hanauna lakou o Saula, no ka Beniamina.
3 Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
O Ahiezera ka luna, alaila o Ioasa, na keiki laua a Hasemaa no Gibea: o Ieziela hoi, a o Peleta, nakeiki a Azemavota; o Beraka hoi, a o Iehu no Anetota.
4 ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
A o Isemaia no Gibeona, he kanaka ikaika iwaena o ke kanakolu; a o Ieremia, o Iahaziela, o Iohanana, a o Iosabada, no Gederata,
5 Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
O Eluzai, o Ierimota, o Bealia o Semaria, a o Sepatia no Harupa,
6 Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
O Elekana, o Iesia, o Azareela, o Ioezera, o Iasobeama, no ka Kora;
7 ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
O loela, o Zebadia, na keiki a Ierohama no Gedora.
8 Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
A hookaawale mai la kekahi poe Gada ia lakou iho no Davida ma kahi paa ma ka waonahele, he poe kanaka ikaika, kanaka kaua e kaua ai; e hiki ia lakou ke lawe i palekaua a me ka ihe, a o na helehelena o lakou, me he helehelena liona la, a ua like lakou me ka dia o na mauna ka mama:
9 Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
O Ezera ka mua, o Obadia ka lua, o Eliaba ke kolu,
10 wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
O Misemana ka ha, o Ieremia ka lima,
11 wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
O Atai ke ono, o Eliela ka hiku,
12 wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
O Iohanana ka walu, o Elezabada ka iwa,
13 wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
O Ieremia ka umi, a o Makebanai ka umikumamakahi.
14 Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
O lakou he poe mamo a Gada, na luna o ka poe kaua: o kekahi mea uuku iho, maluna ia o ka haneri; a o ka mea nui loa, maluna ia o ka tausani.
15 Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
O lakou ka poe i hele ma kela kapa o Ioredane i ka malama mua, i ka manawa i hoopiha ai ia maluna o kona mau kapa a pan: a hoopuehu aku la lakou i na mea a pau o na awawa ma ka hikina a ma ke komohana.
16 Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
A hele mai la kekahi poe mamo a Beniamina a me Iuda i kahi paa io Davida la.
17 Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
Hele aku la o Davida iwaho e halawai me lakou; olelo aku la ia, i aku la ia lakou, Ina e hele aloha mai no oukou io'u nei e kokua mai ia'u, e hookahi ana ko'u naau me ko oukou: aka, ina no ka haawi aku ia'u i ko'u poe enemi, na ke Akua o ko kakou poe kupuna e nana mai, a e papa mai; no ka mea, aole i loaa ka hewa ma ko'u mau lima.
18 Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
Alaila kau mai la ka Uhane maluna iho o Amasai, ke pookela o na lunakoa, Nou no makou, e Davida, a ma kou aoao hoi, e ke keiki a Iese, aloha, aloha ia oe, aloha hoi i na kokua mahope ou; no ka mea, o kou Akua ke kokua mai ia oe. Alaila, hookipa ae la o Davida ia lakou, a hoonoho ia lakou i mau luna o na koa.
19 Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
A kaana mai la kekahi poe o Manase ia Davida, ia ia i hele pu ai me ko Pilisetia i ke kaua ia Saula: aka, aole i kokua aku lakou nei mamuli o lakou, no ka mea, na na 'lii o ko Pilisetia i kukakuka pu, a hoihoi aku ia ia, me ka i ana, E kaa aku auanei ia i kona haku ia Saula, maluna o ko kakou mau poo.
20 Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
I kona hele ana i Zikelaga, kaana mai la kekahi poe o ka Manase ia ia, o Adena, o Iozabada, o Iediaela, o Mikaela, o Iozabada, o Elihu, a o Ziletai, na luna tausani o ka Manase.
21 Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
A kokua mai la lakou mamuli o Davida me kekahi poe koa; no ka mea, he poe kanaka koa ikaika lakou a pau, a he mau luna iwaena o ka poe koa.
22 Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
Ia manawa no, ia la ae, ia la ae, haele mai la [na kanaka] io Davida la, a lilo ae la lakou i poe koa nui, e like me ka puali o ke Akua.
23 Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
Eia ka helu ana i na poe i makaukau no ke kaua, i hele mai io Davida la ma Heberona, e hoohuli ae i ke aupuni o Saula io na la, e like me ka olelo ana a Iehova,
24 Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
O na mamo a Iuda i lawe i ka palekaua a me ka ihe, he eono tausani lakou a me na haneri keu ewalu, i makaukau no ke kaua.
25 Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
O na mamo a Simeona, na kanaka koa ikaika no ke kaua, ehiku tausani lakou, a me ka haneri keu.
26 Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
O na mamo a Levi, eha tausani a me na haneri keu eono.
27 mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
O Iehoiada ke alakai o ka poe mamo a Aarona, a me ia pu na tausani ekolu a me na haneri keu ehiku.
28 ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
A o Zadoka, he kanaka hou, he koa ikaika, a he iwakaluakumamalua na luna koa o ka ohana a kona makuakane.
29 Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
A o na mamo a Beniamina, na hoahanau o Saula, ekolu tausani; no ka mea, mamua he poe kiai ka nui o lakou i ka hale o Saula.
30 Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
A o na mamo a Eperaima, he iwakalua tausani a me na haneri keu ewalu, na kanaka koa ikaika, ua kaulana mawaena o ka ohana o ko lakou mau kupuna.
31 Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
A o ka ohana hapa a Manase, he umikumamawalu tausani, i kaheaia ma ka inoa e hele mai e hooalii ia Davida.
32 Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
A o na mamo a Isakara, ka poe hoomaopopo i na ouli o na manawa, e ike ai i na mea pono a ka Iseraela e hana'i: elua haneri na pookela o lakou; a nana ae la ko lakou poe hoahanau a pau i ka lakou olelo.
33 Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
O ka Zebuluna, ka poe hele aku i ke kaua, i makaukau i ke kaua me na mea kaua a pan, he kanalima tausani o lakou i ike i ka hoouka kaua, aole he naau lua.
34 Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
A o ka Napetali, hookahi tausani luna koa, a me lakou he kanakolukumamahiku tausani, me na palekaua a me na ihe.
35 Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
A o ka Dana i makaukau i ke kaua, he iawakaluakumamawalu tausani, a me na haneri keu eono.
36 Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
A o ka Asera, ka poe hele aku i ke kaua, i makaukau i ke kaua, he kanaha tausani.
37 Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
A ma kela aoao o Ioredane, o ka Reubena, a o ka Gada, a o ka ohana hapa a Manase, me na mea kaua a pau e kaua ai, he haneri a me ka iwakalua tausani.
38 Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
O keia poe kanaka kaua a pau, i ike i ka hoouka i ke kaua, i hele mai me ka naau lokahi ma Heberona, e hoalii ia Davida maluna o ka Iseraela a pau: a ua lokahi hoi ka naau o ka Iseraela a pau i koe e hoalii ia Davida.
39 Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
Ilaila lakou me Davida, ekolu la, e ai ana a e inu ana: no ka mea, ua hoomakaukau ko lakou poe hoahanau na lakou.
40 Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.
Oia hoi, o ka poe o kokoke ana me lakou, a hiki aku i ka Isakara, a i ka Zebuluna, a i ka Napetali, lawe mai la lakou i ka berena maluna o na miula, a o na kamelo, a o na hoki, a o na bipi; me ka ai a me ka palaoa, me na pai huafiku, a me na pai huawaina, me ka waina, ka aila, na bipi a me na hipa he nui loa: no ka mea, he olioli iloko o ka Iseraela.

< 1 Mbiri 12 >