< 1 Mbiri 12 >

1 Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
Also these camen to Dauid in Sichelech, whanne he fledde yit fro Saul, the sone of Cys; whiche weren strongeste men and noble fiyterys,
2 Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
beendynge bouwe, and castynge stoonys with slyngis with euer either hond, and dressynge arowis; of the britheren of Saul of Beniamyn,
3 Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
the prince Achieser, and Joas, the sones of Samaa of Gabaath, and Jazachel, and Phallech, the sones of Azmod, and Barachie, and Jehu of Anathot;
4 ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
also Samay of Gabaon was the strongeste among thretti and aboue thretti; Jeremy, and Jezihel, and Johannan, and Zebadga Zerothites,
5 Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
Elusay, and Jerymoth, and Baalia, and Samaria, and Saphia Araphites,
6 Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
Elchana, and Jesia, and Azrahel, and Jezer, and Jesbaam of Taremy,
7 ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
and Joelam, and Sabadia, the sones of Jeroam of Jedor.
8 Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
But also of Gaddi strongeste men, and beste fiyteris, holdynge scheld and spere, fledden ouer to Dauid, whanne he was hid in deseert; the faces of hem as the face of a lioun, and thei weren swift as capretis in hillis.
9 Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
Ozer was the prince, Obdias the secounde, Eliab the thridde,
10 wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
Masmana the fourthe, Jeremye the fyuethe,
11 wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
Becchi the sixte, Heliel the seuenthe,
12 wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
Johannan the eiythe, Helzedad the nynthe,
13 wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
Jeremye the tenthe, Bachana the euleuenthe;
14 Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
these of the sones of Gad weren princes of the oost; the laste was souereyn ouer an hundrid knyytis, and the moost was souereyn ouer a thousynde.
15 Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
These it ben that passiden ouer Jordan in the firste monethe, whanne it was wont to flowe ouer hise brynkis; and thei dryueden awei alle men that dwelliden in the valeis at the eest coost and west coost.
16 Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
Sotheli also men of Beniamyn and of Juda camen to the stronge hoold, whereyn Dauid dwellide.
17 Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
And Dauid yede out ayens hem, and seide, If ye `ben comyn pesible to me, for to helpe me, myn herte be ioyned to you; forsothe if ye setten aspies to me for myn aduersaries, sithen Y haue not wickidnesse in the hondis, God of our fadris se and deme.
18 Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
Forsothe the spirit clothide Amasay, the prynce among thritti, and he seide, A! Dauid, we ben thin, and thou, sone of Ysai, we schulen be with thee; pees, pees to thee, and pees to thin helperis, for thi Lord God helpith thee. Therfor Dauid resseyuede hem, and made princes of the cumpeny.
19 Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
Forsothe men of Manasses fledden ouer to Dauid, whanne he cam with Filisteis to fiyte ayens Saul, and he fauyte not with hem, for after that the princes of Filisteis hadden take counsel, thei senten hym ayen, and seiden, With perel of oure heed he schal turne ayen to Saul his lord.
20 Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
Therfor whanne Dauid turnede ayen in to Sichelech, men of Manasses fledden ouer to hym, Eduas, and Jozabad, Jedihel, and Mychael, and Naas, and Jozabath, and Helyu, and Salathi, princes of knyytis in Manasses.
21 Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
These men yauen help to Dauid ayens theues; for alle weren strongeste men, and thei weren maad prynces in the oost.
22 Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
But also bi ech dai men camen to Dauid, for to helpe hym, til that the noumbre was maad greet as the oost of God.
23 Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
Also this is the noumbre of princes of the oost that camen to Dauid, whanne he was in Ebron, that thei schulden translate the rewme of Saul to hym, bi the word of the Lord; the sones of Juda,
24 Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
berynge scheeld and spere, sixe thousynde and eiyte hundrid, redi to batel;
25 Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
of the sones of Simeon, seuene thousinde and an hundrid, of strongeste men to fiyte;
26 Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
of the sones of Leuy, foure thousynde and sixe hundrid;
27 mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
also Joiada, prince of the generacioun of Aaron, and thre thousynd and seuene hundrid with hym;
28 ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
also Sadoch, a child of noble wit, and the hows of his fadir, twei and twenti princes;
29 Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
forsothe of the sones of Beniamyn, britheren of Saul, thre thousynde; for a greet part of hem suede yit the hows of Saul;
30 Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
forsothe of the sones of Effraym, twenti thousynde and eiyte hundrid, strongeste men in bodili myyt, men named in her meynees;
31 Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
and of the half part of the lynage of Manasses, eiytene thousynde; alle camen bi her names, to make Dauid kyng;
32 Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
also of the sones of Ysacar, two hundrid princes, lernd men, that knewen ech tyme to comaunde what the puple of Israel ouyt to do; sotheli al the residue lynage suede the counseils of hem;
33 Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
forsothe of Zabulon camen fifti thousynde in to helpe, not in double herte, which yeden out to batel, and stoden in the scheltrun, and weren maad redi with armuris of batel;
34 Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
and of Neptalym a thousynde prynces, and with hem camen seuene and thritti thousynde men, arayed with scheeld and speere;
35 Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
also of Dan, eiyte and twenti thousynde and sixe hundrid men, maad redi to batel;
36 Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
and of Aser fourti thousynde men, goynge out to batel, and stirynge to batel in the scheltrun.
37 Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
Forsothe biyende Jordan, of the sones of Ruben, and of Gad, and of the half part of the lynage of Manasses, sixe scoore thousynde men, araied with armuris of batel.
38 Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
Alle these men werriouris and redi to batel camen with perfit herte in to Ebron, to make Dauid kyng on al Israel; but also alle the residue of Israel weren of oon herte, that Dauid schulde be maad king on al Israel.
39 Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
And thei weren ther at Dauid thre daies, and eten and drunken; for her britheren hadden maad redi to hem;
40 Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.
but also thei that weren niy hem, til to Isacar and Zabulon and Neptalym, brouyten looues on assis, and camelis, and mulis, and oxis, for to ete; mele, bundelis of pressid figis, dried grapis, wyn, oile, oxis and wetheres, to al plentee; for ioy was in Israel.

< 1 Mbiri 12 >