< 1 Mbiri 12 >

1 Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
Now these are they that came to David to Siceleg, while he yet fled from Saul the son of Cia, and they were most valiant and excellent warriors,
2 Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
Bending the bow, and using either hand in hurling stones with slings, and shooting arrows: of the brethren of Saul of Benjamin.
3 Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
The chief was Ahiezer, and Joas, the sons of Samaa of Gabaath, and Jaziel, and Phallet the sons of Azmoth, and Beracha, and Jehu an Anathothite.
4 ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
And Samaias of Gabaon, the stoutest amongst the thirty and over the thirty; Jeremias, and Jeheziel, and Johanan, and Jezabad of Gaderoth;
5 Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
And Eluzai, and Jerimuth, and Baalia, and Samaria, and Saphatia the Haruphite;
6 Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
Elcana, and Jesia, and Azareel, and Joezer, and Jesbaam of Carehim:
7 ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
And Joela, and Zabadia the sons of Jeroham of Gedor.
8 Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
From Gaddi also there went over to David, when he lay hid in the wilderness most valiant men, and excellent warriors, holding shield and spear: whose faces were like the faces of a lion, and they were swift like the roebucks on the mountains.
9 Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
Ezer the chief, Obdias the second, Eliab the third,
10 wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
Masmana the fourth, Jeremias the fifth.
11 wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
Ethi the sixth, Eliel the seventh,
12 wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
Johanan the eighth, Elzebad the ninth,
13 wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
Jerenias the tenth, Machbani the eleventh,
14 Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
These were of the sons of Gad, captains of the army: the least of them was captain over a hundred soldiers, and the greatest over a thousand.
15 Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
These are they who passed over the Jordan in the first month, when it is used to how over its banks: and they put to flight all that dwelt in the valleys both toward the east and toward the west.
16 Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
And there came also of the men of Benjamin, and of Juda to the hold, in which David abode.
17 Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
And David went out to meet them, and said: If you are come peaceably to me to help me, let my heart be joined to you: but if you plot against me for my enemies whereas I have no iniquity in my hands, let the God of our fathers see, and judge.
18 Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
But the spirit came upon Amasai the chief among thirty, and he said: We are thine, O David, and for thee, O son of Isai: peace, peace be to thee, and peace to thy helpers. For thy God helpeth thee. So David received them, and made them captains of the band.
19 Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
And there were some of Manasses that went over to David, when he came with the Philistines against Saul to fight: but he did not fight with them: because the lords of the Philistines taking counsel sent him back, saying: With the danger of our heads he will return to his master Saul.
20 Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
So when he went back to Siceleg, there fled to him of Manasses, Ednas and Jozabad, and Jedihel, and Michael, and Ednas, and Jozabad, and Eliu, and Salathi, captains of thousands in Manasses.
21 Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
These helped David against the rovers: for they were all most valiant men, and were made commanders in the army.
22 Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
Moreover day by day there came some to David to help him till they became a great number, like the army of God.
23 Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
And this is the number of the chiefs of the army who came to David, when he was in Hebron, to transfer to him the kingdom of Saul, according to the word of the Lord.
24 Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
The sons of Juda bearing shield and spear, six thousand eight hundred well appointed to war.
25 Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
Of the sons of Simeon valiant men for war, seven thousand one hundred.
26 Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
Of the sons of Levi, four thousand six hundred.
27 mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
And Joiada prince of the race of Aaron, and with him three thousand seven hundred.
28 ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
Sadoc also a young man of excellent disposition, and the house of his father, twenty-two principal men.
29 Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
And of the sons of Benjamin the brethren of Saul, three thousand: for hitherto a great part of them followed the house of Saul.
30 Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
And of the sons of Ephraim twenty thousand eight hundred, men of great valour renowned in their kindreds.
31 Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
And of the half tribe of Manasses, eighteen thousand, every one by their names, came to make David king.
32 Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
Also of the sons of Issachar men of understanding, that knew all times to order what Israel should do, two hundred principal men: and all the rest of the tribe followed their counsel.
33 Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
And of Zabulon such as went forth to battle, and stood in array well appointed with armour for war, there came fifty thousand to his aid, with no double heart.
34 Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
And of Nephtali, a thousand leaders: and with them seven and thirty thousand, furnished with shield and spear.
35 Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
Of Dan also twenty-eight thousand six hundred prepared for battle.
36 Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
And of Aser forty thousand going forth to fight, and challenging in battle.
37 Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
And on the other side of the Jordan of the sons of Ruben, and of Gad, and of the half of the tribe of Manasses a hundred and twenty thousand, furnished with arms for war.
38 Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
All these men of war well appointed to fight, came with a perfect heart to Hebron, to make David king over all Israel: and all the rest also of Israel, were of one heart to make David king.
39 Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
And they were there with David three days eating and drinking: for their brethren had prepared for them.
40 Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.
Moreover they that were near them even as far as Issachar, and Zabulon, and Nephtali, brought leaves on asses, and on camels, and on mules, and on oxen, to eat: meal, figs, raisins, wine, oil, and oxen, and sheep in abundance, for there was joy in Israel.

< 1 Mbiri 12 >