< 1 Mbiri 12 >

1 Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
Og disse ere de, som kom til David i Ziklag, der han endnu maatte holde sig inde for Sauls, Kis's Søns, Ansigt; og de vare iblandt de vældige, som hjalp i Krigen;
2 Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
de vare rustede med Bue, kastede med Stene med højre og venstre Haand og skøde Pile med Buen; de vare af Sauls Brødre, af Benjamin.
3 Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
Ahieser var den ypperste, og Joas, Gibeathiten Semajas Sønner, og Jesiel og Peleth, Asmaveths Sønner, og Beraka og Jehu, Anathothiten.
4 ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
Og Jismaja, Gibeoniten, var vældig iblandt de tredive og sat over de tredive, og Jeremia og Jahasiel og Johanan og Josabad, Gederathiten,
5 Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
Elusaj og Jerimoth og Bealja og Semarja og Safatja, Harufiten,
6 Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
Elkana og Jisija og Asareel og Joeser og Jasobeam, Koriterne,
7 ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
og Joela, og Sebadja, Jerohams Sønner, af Gedor.
8 Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
Og af Gaditerne gik nogle over til David til Befæstningen i Ørken, vældige til Strid, Stridsmænd til Krigen, rustede med Skjold og Spyd; og deres Ansigter vare som Løvers Ansigter, og de vare snare til at løbe som Raadyr paa Bjergene.
9 Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
Eser var den første, Obadja den anden, Eliab den tredje,
10 wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
Mismanna den fjerde, Jeremia den femte,
11 wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
Athaj den sjette, Eliel den syvende,
12 wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
Johanan den ottende, Elisabad den niende,
13 wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
Jeremias den tiende, Makbannaj den ellevte.
14 Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
Disse vare af Gads Børn, Øverster for Hæren; den ringeste af dem var mere end hundrede, og den største mere end tusinde.
15 Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
Disse ere de, som gik over Jordanen i den første Maaned, da den var fuld over alle sine Bredder; og de dreve alle Dalenes Indbyggere paa Flugt imod Østen og imod Vesten.
16 Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
Der kom og af Benjamins og Judas Børn til Befæstningen til David.
17 Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
Og David gik ud til dem og svarede og sagde til dem: Dersom I komme med Fred til mig for at hjælpe mig, da skal mit Hjerte være forenet med eder; men dersom I komme for at bedrage mig og overgive mig til mine Fjender, enddog der ingen Uret er i mine Hænder, da se vore Fædres Gud til og straffe det!
18 Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
Og Aanden iførte sig Amasaj, den øverste af Høvedsmændene, og han sagde: Dig, David, tilhøre vi, og med dig, du Isajs Søn, ere vi; Fred, ja Fred være med dig og Fred med dem, som hjælpe dig! thi din Gud hjælper dig. Da tog David imod dem og satte dem til Øverster for Troppen.
19 Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
Og af Manasse vare nogle gaaede over til David, der han kom med Filisterne imod Saul til Krig, dog uden at hjælpe dem; thi Filisternes Fyrster lode ham fare efter en Raadslagning og sagde: Om han gik over til sin Herre Saul, maatte det koste os vore Hoveder.
20 Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
Der han drog til Ziklag, gik over til ham af Manasse: Adna og Josabad og Jediael og Mikael og Josabad og Elihu og Zilthaj, Øverster over de tusinde, som hørte til Manasse.
21 Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
Og de hjalp David imod Krigsfolkene, thi de vare alle vældige til Strid, og de bleve Høvedsmænd for Hæren.
22 Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
Thi der kom til den Tid daglig nogle til David for at hjælpe ham, indtil det blev til en stor Lejr, som Guds Lejr.
23 Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
Og dette er Tallet paa de Øverster over dem, som vare bevæbnede til Striden, de, som kom til David i Hebron for at skaffe ham Sauls Rige efter Herrens Mund:
24 Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
Judas Børn, som bare Skjold og Spyd, vare seks Tusinde og otte Hundrede, bevæbnede til Strid;
25 Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
af Simeons Børn, vældige til Strid, til Hæren, syv Tusinde og hundrede;
26 Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
af Levis Børn, fire Tusinde og seks Hundrede.
27 mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
Og Jojada var en Fyrste for Arons Børn, og der var tre Tusinde og syv Hundrede med ham.
28 ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
Og Zadok var en ung Mand, vældig til Strid, og af hans Faders Hus vare to og tyve Høvedsmænd;
29 Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
og af Benjamins Børn, Sauls Brødre, tre Tusinde; thi hidindtil havde den største Del af dem taget Vare paa, hvad der var at varetage i Sauls Hus.
30 Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
Og af Efraims Børn tyve Tusinde og otte Hundrede, vældige til Strid, navnkundige Mænd i deres Fædres Hus;
31 Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
og af den halve Manasses Stamme atten Tusinde, som vare nævnede ved Navn, for at komme at gøre David til Konge.
32 Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
Og af Isaskars Børn, som vare kyndige og forstandige paa Tiderne, saa at de vidste, hvad Israel skulde gøre, var der to Hundrede Øverster, og alle deres Brødre fulgte deres Ord.
33 Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
Af Sebulon, som droge ud til Strid, rustede til Krig med alle Haande Krigsvaaben, halvtredsindstyve Tusinde, og de stillede sig i Slagorden uden tvedelt Hjerte;
34 Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
og at Nafthali tusinde Høvedsmænd og med dem syv og tredive Tusinde, som førte Skjold og Spyd;
35 Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
og af Daniterne rustede til Krig otte og tyve Tusinde og seks Hundrede;
36 Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
og af Aser, som droge ud til Strid, at ruste sig til Krig, fyrretyve Tusinde;
37 Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
og af dem paa hin Side Jordanen, af Rubeniterne og Gaditerne og den halve Manasses Stamme, med alle Haande Stridsvaaben til Krig, hundrede og tyve Tusinde.
38 Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
Alle disse Krigsmænd, som stillede sig i Slagorden, kom med et retskaffent Hjerte til Hebron, at gøre David til Konge over hele Israel; og alle de øvrige af Israel havde ogsaa eet Hjerte til at gøre David til Konge.
39 Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
Og de vare der hos David i tre Dage, aade og drak; thi deres Brødre havde beredt Mad for dem.
40 Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.
Ogsaa de, som vare nær hos dem indtil Isaskar og Sebulon og Nafthali, førte Brød paa Asenerne og paa Kamelerne og paa Mulerne og paa Øksnene, Spise af Mel, Figenkager og Klaser Rosiner og Vin og Olie og Øksne og Faar i Mangfoldighed; thi der var Glæde i Israel.

< 1 Mbiri 12 >