< 1 Mbiri 11 >
1 Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu.
congregatus est igitur omnis Israhel ad David in Hebron dicens os tuum sumus et caro tua
2 Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
heri quoque et nudius tertius cum adhuc regnaret Saul tu eras qui educebas et introducebas Israhel tibi enim dixit Dominus Deus tuus tu pasces populum meum Israhel et tu eris princeps super eum
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.
venerunt ergo omnes maiores natu Israhel ad regem in Hebron et iniit David cum eis foedus coram Domino unxeruntque eum regem super Israhel iuxta sermonem Domini quem locutus est in manu Samuhel
4 Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko
abiit quoque David et omnis Israhel in Hierusalem haec est Iebus ubi erant Iebusei habitatores terrae
5 anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
dixeruntque qui habitabant in Iebus ad David non ingredieris huc porro David cepit arcem Sion quae est civitas David
6 Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.
dixitque omnis qui percusserit Iebuseum in primis erit princeps et dux ascendit igitur primus Ioab filius Sarviae et factus est princeps
7 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide.
habitavit autem David in arce et idcirco appellata est civitas David
8 Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu.
aedificavitque urbem in circuitu a Mello usque ad gyrum Ioab autem reliqua urbis extruxit
9 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.
proficiebatque David vadens et crescens et Dominus exercituum erat cum eo
10 Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera.
hii principes virorum fortium David qui adiuverunt eum ut rex fieret super omnem Israhel iuxta verbum Domini quod locutus est ad Israhel
11 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.
et iste numerus robustorum David Iesbaam filius Achamoni princeps inter triginta iste levavit hastam suam super trecentos vulneratos una vice
12 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu.
et post eum Eleazar filius patrui eius Ahoites qui erat inter tres potentes
13 Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele.
iste fuit cum David in Aphesdommim quando Philisthim congregati sunt ad locum illum in proelium et erat ager regionis illius plenus hordeo fugeratque populus a facie Philisthinorum
14 Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
hic stetit in medio agri et defendit eum cumque percussisset Philistheos dedit Dominus salutem magnam populo suo
15 Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
descenderunt autem tres de triginta principibus ad petram in qua erat David ad speluncam Odollam quando Philisthim fuerant castrametati in valle Raphaim
16 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
porro David erat in praesidio et statio Philisthinorum in Bethleem
17 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
desideravit igitur David et dixit o si quis daret mihi aquam de cisterna Bethleem quae est in porta
18 Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
tres ergo isti per media castra Philisthinorum perrexerunt et hauserunt aquam de cisterna Bethleem quae erat in porta et adtulerunt ad David ut biberet qui noluit sed magis libavit illam Domino
19 Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
dicens absit ut in conspectu Dei mei hoc faciam et sanguinem virorum istorum bibam quia in periculo animarum suarum adtulerunt mihi aquam et ob hanc causam noluit bibere haec fecerunt tres robustissimi
20 Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
Abisai quoque frater Ioab ipse erat princeps trium et ipse levavit hastam suam contra trecentos vulneratos et ipse erat inter tres nominatissimus
21 Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
inter tres secundos inclitus et princeps eorum verumtamen usque ad tres primos non pervenerat
22 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
Banaia filius Ioiadae viri robustissimi qui multa opera perpetrarat de Capsehel ipse percussit duos Arihel Moab et ipse descendit et interfecit leonem in media cisterna tempore nivis
23 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
et ipse percussit virum aegyptium cuius statura erat quinque cubitorum et habebat lanceam ut liciatorium texentium descendit ergo ad eum cum virga et rapuit hastam quam tenebat manu et interfecit eum hasta sua
24 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
haec fecit Banaia filius Ioiada qui erat inter tres robustos nominatissimus
25 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
inter triginta primus verumtamen ad tres usque non pervenerat posuit autem eum David ad auriculam suam
26 Ankhondo amphamvuwa anali: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
porro fortissimi in exercitu Asahel frater Ioab et Eleanan filius patrui eius de Bethleem
27 Samoti Mharori, Helezi Mpeloni.
Semmoth Arorites Helles Phallonites
28 Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiezeri wa ku Anatoti,
Iras filius Acces Thecuites Abiezer Anathothites
29 Sibekai Mhusati, Ilai Mwahohi,
Sobbochai Asothites Ilai Ahoites
30 Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,
Marai Netophathites Heled filius Baana Netophathites
31 Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini, Benaya Mpiratoni,
Ethai filius Ribai de Gabaath filiorum Beniamin Banaia Pharathonites
32 Hurai wa ku zigwa za Gaasi, Abieli Mwaribati,
Uri de torrente Gaas Abial Arabathites Azmoth Bauramites Eliaba Salabonites
33 Azimaveti Mbaharumi, Eliyahiba Msaaliboni,
filii Asom Gezonites Ionathan filius Sega Ararites
34 ana a Hasemu Mgizoni, Yonatani mwana wa Sage Mharari,
Ahiam filius Sachar Ararites
35 Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,
Eliphal filius Ur
36 Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,
Apher Mechurathites Ahia Phellonites
37 Heziro wa ku Karimeli Naara mwana wa Ezibai,
Asrai Carmelites Noorai filius Azbi
38 Yoweli mʼbale wa Natani, Mibihari mwana wa Hagiri,
Iohel frater Nathan Mabar filius Agarai
39 Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.
Sellec Ammonites Noorai Berothites armiger Ioab filii Sarviae
40 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
Iras Iethreus Gareb Iethreus
41 Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Ahilai,
Urias Ettheus Zabad filius Ooli
42 Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,
Adina filius Seza Rubenites princeps Rubenitarum et cum eo triginta
43 Hanani mwana wa Maaka, Yehosafati Mmitini,
Hanan filius Maacha et Iosaphat Mathanites
44 Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,
Ozias Astharothites Semma et Iaihel filii Hotam Aroerites
45 Yediaeli mwana wa Simiri, ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,
Iedihel filius Samri et Ioha frater eius Thosaites
46 Elieli Mhavati, Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, Itima Mmowabu,
Elihel Maumites et Ieribai et Iosaia filii Elnaem
47 Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.
et Iethma Moabites Elihel et Obed et Iasihel de Masobia