< San Mateo 25 >

1 AYO nae y raenon langet parejo yan dies na bitgen, ni jachule y lamparañija ya manmapos para ujatagam y nobio.
“Nthawi imeneyo ufumu wakumwamba udzafanizidwa ndi anamwali khumi amene anatenga nyale zawo napita kukakumana ndi mkwati.
2 Ya y sinco guiya sija manmejnalom, ya y sinco manaetiningo.
Asanu anali opusa ndipo asanu ena anali ochenjera.
3 Y manaetiningo, jachule y lamparañija, ya ti manmañule laña.
Opusawo anatenga nyale zawo koma sanatenge mafuta;
4 Lao y manmejnalom manmañule laña gui baso, yan y lamparañija.
koma ochenjerawo anatenga mafuta awo mʼmabotolo pamodzi ndi nyale zawo.
5 Ya anae atrasasao y nobio, manmatujog todo sija, ya manmaego.
Mkwati anachedwa ndipo onse anayamba kusinza nagona.
6 Ya y tatalopuenge majungog un inagang, na ilegña: Estagüe y nobio na mamamaela! fanjuyong ya inresibe!
“Pakati pa usiku kunamveka kufuwula kuti, ‘Onani Mkwati! Tulukani kuti mukakumane naye!’
7 Ayo nae todo y bitgen sija mangajulo ya jafamauleg y lamparañija.
“Pamenepo anamwali onse anadzuka nayatsa nyale zawo.
8 Ya y manaetiningo ilegñija ni manmejnalom: Naejam gui lañanmiyo sa y lamparanmame manmatae.
Opusawo anati kwa ochenjerawo, ‘Tipatseniko mafuta anu; nyale zathu zikuzima.’
9 Ya y manmejnalom manmanope ilegñija: Munga sa ti mannajongjit; lao janao fanmalag y manmanbebende ya infanmamajan para jamyo namaesa.
“Ochenjerawo anayankha, nati, ‘Ayi sangakwanire inu ndi ife. Pitani kwa ogulitsa mafuta ndi kukadzigulira nokha.’
10 Ya anae manmapos sija para ufanmamajan, mato y nobio; ya y estaba manlisto manjalom yan güiya gui guipot umasagua; ya majuchom y petta.
“Koma pamene ankapita kukagula mafutawo, mkwati anafika. Anamwali amene anali okonzeka aja analowa naye pamodzi mʼnyumba ya phwando la ukwati. Ndipo khomo linatsekedwa.
11 Despues manmato y palo na bitgen ya ilegñija: Señot, Señot, babayejam.
“Pambuyo pake enawo anabwera nati, ‘Ambuye! Ambuye! Titsekulireni!’
12 Lao güiya manope, ilegna; Magajet jusangane jamyo na ti jutungo jamyo.
“Koma iye anayankha kuti, ‘Zoonadi, ine ndikuwuzani kuti sindikukudziwani.’
13 Fanmagmata sa ti intingo y jaane ni y ora.
“Choncho khalani odikira, popeza simudziwa tsiku kapena nthawi.”
14 Sa uguaja parejo yan un taotao ni jumanao chago na tano, ya jaagang antes y tentagoña sija, ya jaentrega sija ni güinajaña.
“Komanso udzafanizidwa ndi munthu amene ankapita pa ulendo, ndipo anayitana antchito ake nawasiyira chuma chake.
15 Ya y uno janae sinco talento, ya y otro dos, ya y otro uno; ya cada uno taemano y guinefuloña; ya enseguidas mapos.
Wina anamupatsa ndalama 5,000, kwa wina 2,000 ndi kwa wina 1,000. Aliyense monga mwa nzeru zake. Pamenepo anapita pa ulendo wake.
16 Ya y rumesibe y sinco na talento, janacometsio, ya jagana talo sinco na talento.
Munthu amene analandira ndalama 5,000 uja, anapita nthawi yomweyo nachita nazo malonda napindula 5,000 zina.
17 Parejo locue yan y rumesibe dos, mangana talo dos.
Chimodzimodzinso amene analandira 2,000 uja anapindula 2,000 zina.
18 Lao y rumesibe y uno, jumuyong ya jaguadog y eda, ya janaatog y salape y senotña.
Koma munthu amene analandira 1,000 uja, anapita nakumba dzenje nabisapo ndalama ya mbuye wake.
19 Despues di apmam na tiempo, mato y señot ayo sija na tentago, ya manacuentas yan sija.
“Patapita nthawi yayitali, mbuye wa antchitowo anabwera nawayitana kuti afotokoze chimene anachita ndi ndalama zija.
20 Ya mato ayo y rumesibe sinco na talento, yan mañuñule talo sinco talento, ya ilegña: Señot, sinco na talento unnaeyo; estagüe talo sinco na junafangana.
Munthu amene analandira ndalama 5,000 uja anabweretsa 5,000 zina nati, ‘Ambuye munandisungitsa 5,000, taonani ndapindula 5,000 zinanso.’
21 Y senotña ilegña nu güiya: Mauleg chechomo, jago mauleg na tentago yan guesmanosguejao: guine unfatinas mauleg gui didide, bae jupoluyejao megae: jalom gui minagof y señotmo.
“Ambuye ake anayankha nati, ‘Wachita bwino, wantchito wabwino ndi wokhulupirika iwe! Wakhala wokhulupirika pa zinthu zochepa; ndidzakuyika iwe kukhala woyangʼanira zinthu zambiri. Bwera, udzakondwere pamodzi ndi mbuye wako!’
22 Mato locue ayo y rumesibe dos na talento, ya ilegña: Señot, dos na talento unnaeyo; estagüe talo dos talento na junafangana.
“Munthu amene anali ndi ndalama 2,000 uja anabweranso nati, ‘Ambuye munandisungitsa 2,000, onani, ndapindula 2,000 zinanso.’
23 Y señotña ilegña nu güiya: Mauleg chechomo, jago mauleg na tentago yan guesmanosguejao: guine unfatinas mauleg gui didide, bae jupoluyejao megae; jalom gui minagof y señotmo.
“Mbuye wake anayankha nati, ‘Wachita bwino, wantchito wabwino ndi wokhulupirika! Wakhala wokhulupirika pa zinthu zochepa; ndidzakuyika kukhala woyangʼanira zinthu zambiri. Bwera, udzakondwere pamodzi ndi mbuye wako!’
24 Mato locue ayo y rumesibe un talento, ya ilegña: Señot, guajo jutungo na jago majetogjao na taotao; sa mangongoco jao gui anae ti mananom jao, ya manrecocoje jao gui anae ti mañalapon jao;
“Kenaka munthu amene analandira ndalama 1,000 uja anabwera nati, ‘Ambuye ndinadziwa kuti ndinu munthu wowuma mtima, amene mumakolola pamene simunadzale ndi kututa kumene simunafese.
25 Ya maañaoyo, ya maposyo ya junaatog y talentomo gui jalom y tano: estagüe ni iyomo.
Choncho ndinachita mantha ndipo ndinapita ndi kukabisa ndalama yanuyo pa dzenje. Onani, si iyi ndalama yanu ija.’
26 Lao y señotña inepe güe ilegña: Taelayejao na tentago yan gago. Untungoja na mangongoco yo gui anae ti mananom yo, ya manrecocoje yo gui anae ti mañalapon yo;
“Mbuye wake anayankha nati, ‘Iwe wantchito woyipa ndi waulesi! Iwe umadziwa kuti ndimakolola pamene sindinadzale, ndi kututa kumene sindinafese.
27 Enao mina jago nesesita unnae y banquero sija ni salapejo, ya yaguin matoyo, juresibe y iyoco yan ganansia.
Bwanji sunayike ndalama yanga kwa osunga ndalama kuti ine pobwera ndidzalandire ndalama yangayo pamodzi ndi chiwongoladzanja?
28 Enao mina umanajanao ayo na talento guiya güiya, ya umannae ayo y guaja dies na talento.
“‘Mulandeni ndalamayo, ndipo patsani iye amene ali ndi ndalama 10,000.
29 Sa jayeja y guaja, umannae güe, ya uguaja megae; lao y taya iyoña, achogja guaja güinajaña umanajanao.
Pakuti aliyense amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, ndipo adzakhala nazo zochuluka. Aliyense amene alibe adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho.
30 Ya y taebalenña na tentago, yute juyong gui jalom jomjom, ayo nae uguaja tumanges yan chegcheg nifen.
Ndipo muponyeni wantchito wopanda phinduyu kunja, ku mdima kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.’”
31 Yaguin y Lajin taotao mato gui minalagña, yan todo y angjetña sija, ayo nae ufatachong gui jilo y tachong y minalagña;
“Pamene Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wake, pamodzi ndi angelo ake onse, adzakhala pa mpando waufumu mu ulemerero wakumwamba.
32 Ya umanafandaña gui menaña todo y nasion sija; ya umanafañajnge y uno gui otro, calang y pastot yan janasajnge y quinilo sija gui chiba;
Mitundu yonse ya anthu idzasonkhanitsidwa pamaso pake, ndipo adzawalekanitsa iwo wina ndi mnzake monga mʼbusa amalekanitsa nkhosa ndi mbuzi.
33 Ya japolo y quinilo sija gui agapaña, ya y chiba gui acagüeña.
Adzayika nkhosa ku dzanja lake lamanja ndi mbuzi ku lamanzere.
34 Ayo nae y ray ualog ni mangaegue gui agapaña: Maela jamyo mandichoso gui Tatajo, ya inereda y raeno ni esta listo para jamyo desde y mafatinas y tano;
“Pamenepo mfumu idzati kwa a ku dzanja lamanja, ‘Bwerani inu odalitsika ndi Atate anga; landirani ufumu umene unakonzedwa chifukwa cha inu kuyambira pachiyambi cha dziko.
35 Sa anae ñalangyo, innachocho yo; anae majoyo, innaguimen yo; anae taotaojuyong yo, innajalom yo;
Pakuti ndinali ndi njala ndipo munandipatsa chakudya, ndinali ndi ludzu ndipo munandipatsa madzi akumwa, ndinali mlendo ndipo munandilandira,
36 Anae taya magagojo, innaminagago yo. Anae malangoyo, inbesita yo; anae gaegue yo gui calaboso, manmato jamyo guiya guajo.
ndinali wausiwa ndipo munandiveka, ndinali wodwala ndipo munandisamalira, ndinali ku ndende ndipo inu munandiyendera.’
37 Ayo nae y manunas manmanope güe ilegñija: Señot, ngaean nae inliijao ñalang, ya innachocho jao? pat majo, ya innaguimen jao?
“Ndipo olungamawo adzamuyankha kuti, ‘Ambuye ndi liti tinakuonani muli ndi njala ndipo tinakudyetsani, kapena ludzu ndipo tinakupatsani madzi akumwa?
38 Ngaean nae inliijao taotaojuyong, ya innajalom jao? pat anae taya magagomo, ya innaminagago jao?
Ndi liti tinakuonani muli mlendo ndipo tinakulandirani, kapena wa usiwa ndipo tinakuvekani?
39 Pat ñgaean nae inliijao malango, pat y calaboso, ya manmatojam guiya jago?
Ndi liti tinakuonani mutadwala kapena ku ndende ndipo tinakuyenderani?’
40 Y ray ujaope ilegña nu sija: Magajet jusangane jamyo, taemanoja na y infatinas ni uno güine gui mandiquique na mañelujo, infatinasja locue nu guajo.
“Mfumu idzayankha kuti, ‘Zoonadi, ndikuwuzani kuti chilichonse chimene munachitira mmodzi wa abale anga onyozekawa munandichitira Ine.’
41 Ayo nae ilegña locue ni y mangaegue gui acagüeña: Fanjanao guiya guajo, jamyo matdito, fanmalag y taejinecog na guafe, ni esta manalisto ni anite yan y anjetña sija; (aiōnios g166)
“Pamenepo adzanena kwa akumanzere kwake kuti, ‘Chokani kwa Ine, inu otembereredwa, pitani ku moto wosatha wokonzedwera mdierekezi ndi angelo ake. (aiōnios g166)
42 Sa anae ñalangyo, ti innachocho yo; anae majoyo, ti innaguimen yo;
Pakuti ndinali ndi njala ndipo simunandipatse chakudya, ndinali ndi ludzu ndipo simunandipatse madzi akumwa,
43 Anae taotaojuyong yo, ti innajalom yo; anae taya magagojo, ti innaminagago yo; malangoyo, yan gaegue yo gui calaboso, lao ti inbesita yo.
ndinali mlendo koma inu simunandilandire, ndinali wa usiwa koma simunandiveke, ndinali wodwala komanso ku ndende simunandisamalire.’
44 Ayo nae ufanmanope locue sija, ilegñija: Señot, ngaean nae inliijao ñalang, pat majo, pat taotaojuyong, pat taya magagomo, pat malango, pat gui calaboso, ya ti insetbejao?
“Iwo adzayankha kuti, ‘Ambuye ndi liti tinakuonani muli ndi njala kapena ludzu kapena mlendo kapena wausiwa kapena wodwala kapena mʼndende, ndipo kuti sitinakuthandizeni?’
45 Ayo nae ujaope sija, ilegña: Magajet jusangane jamyo, na taemanoja ti infatinas nu uno güine gui mas mandiquique, ti infatinas nu guajo.
“Iye adzayankha kuti, ‘Zoonadi, ndikuwuzani kuti chilichonse chimene simunachitire mmodzi wa abale anga onyozekawa simunandichitire Ine.’
46 Ya esta sija manmapos para y taejinecog na minasapet; lao y manunas para y taejinecog na linala. (aiōnios g166)
“Amenewa adzapita ku chilango chosatha pamene olungama ku moyo wosatha.” (aiōnios g166)

< San Mateo 25 >