< San Marcos 6 >

1 YA anae jumanao güije mato gui tanoña; ya y disipuluña sija madalalag güe.
Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
2 Ya anae mato y sábado na jaane, jatutujon mamanagüe gui sinagoga; ya megae ni jumungog güe ninafanmanman, ya ilegñija: Mano nae guaja este taotao este sija na güinaja? Yan jafa este na tiningo y esta manae güe? ya jaftaemano este sija na ninámanman ni mafatinas ni canaeña?
Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
3 Ada ti este y catpintero, lajin Maria, chelun Santiago, yan si Joses, yan si Juda, yan si Simon? Ada ti manjijita yan y mañeluña famalaoan güine? Ya maninefefende nu güiya.
Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
4 Lao si Jesus ilegña nu sija: Taya profeta sin onraña lao y tanoñaja, yan entre y parientesña sija, ya y guimaña.
Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
5 Ya ti siña jafatinas güije jafa na námanman, na japolo y canaeña gui jilo palo manmalango sija, ya janajomlo.
Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
6 Ya güiya ninámanman ni ti manmanjongguenñija; ya malilicue gui y sengsong sija mananagüe.
Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
7 Ya jaagang y dose sija, y jatutujon tumago dos en dos, ya janae ninasiñañija gui jilo manáplacha na espiritu sija;
Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
8 Ya jatago sija na chañija fanmañuñule ni jafa para y chalan, na un bastoñija; ni costat, ni pan, ni salape gui betsanñija;
Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
9 Lao ufanchenancleta; ya munga manminagago dos na magago.
Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
10 Ya ilegña nu sija: Manoja na guma nae manjalom jamyo; fañaga güije, asta gui manjanao jamyo güije na lugat.
Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
11 Ya todo ayo sija y ti rumesibe jamyo, ni ti maninecungog jamyo, fanjanao güije, sacude y petbos ni gaegue gui papa adengmiyo para testimonio contra sija. Magajet jusangane jamyo, na mas sungunon na castigon Sodoma, yan Gomora gui jaanin y sentensia, qui ayo na sidua.
Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
12 Ya manmapos jasetmon na y taotao sija ufanmañotsot.
Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
13 Ya jayute juyong megae na anite sija, ya japapalae laña megae na manmalango sija, ya janafanjomlo.
Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
14 Ya jajungog y ray Herodes y faman Jesus (sa afamao y naanña), ya ilegña: Si Juan Bautista cajulo guine y manmatae sija; ya pot este mangaeninasiña na chocho, esta fumatinas nu güiya.
Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
15 Palo ilegñija: Si Elias. Y palo ilegñija: Profeta güe, pat uno gui profeta sija.
Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
16 Ya anae jajungog si Herodes, ilegña: Este si Juan ni guine judegüeya: güiya cajulo guine y manmatae sija.
Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
17 Sa güiyaja si Herodes manago na umamantiene si Juan, ya umapreso gui catset pot si Herodias, asaguan y cheluña as Felipe, sa jacone para asaguaña.
Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
18 Sa si Juan ilegña as Herodes: Ti cabales na uncone y asaguan y chelumo.
Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
19 Ya pot este si Herodias uninaguaguat contra güiya, ya jadesesao na upuno, lao ti janasiña.
Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
20 Sa si Herodes maañao as Juan, jatungo na tunas yan Santos na taotao ya jaguefadaje. Ya anae jajungog, gosbumuebuente gui corasonña; ya jaecungogjao ni minagofña.
chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
21 Ya anae mato un jaane na si Herodes gumupot ni mafañaguña, ya mamatinas sena para y prinsipeña sija yan y capitan sija, yan y manmagas sija guiya Galilea;
Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
22 Ya jumalom y jagan Herodias, ya bumaela, ya janamagof si Herodes, yan ayo sija y mangachochongña gui lamasa; ya y ray ilegña ni patgon na palaoan: Gagaoyo ni malagomo, ya junaejao.
Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
23 Ya manjula: Todo y ungagaoyo, junae asta lamita gui raenoco.
Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
24 Ya mapos güe, ya ilegña as nanaña: Jafa jugagao? Si nanaña ilegña: Y ilun Juan Bautista.
Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
25 Ayo nae jumalom enseguidas gui ray ya jagagao, ilegña: Malagoyo pago na unnaeyo gui un plato ni ilun Juan Bautista.
Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
26 Ya y ray ninagostriste; lao pot y juramentoña, yan ayo sija y mangachongña gui lamasa, ti malago japune.
Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
27 Ya enseguidas y ray manago uno gui guatdia, jatago na ujanao ya uchinilie ni iluña. Ya mapos, ya jadegüeya gui jalom catset.
Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
28 Ya machule guato y iluña gui un plato, ya manae y patgon palaoan, ya y patgon palaoan janae y nanaña.
nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
29 Ya anae majungog ni disipuluña sija, manmato, ya machule y tataotaoña, ya mapolo gui un naftan.
Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
30 Ya y apostoles mandaña gui as Jesus, ya masangane güe todo ni chechoñija, yan y finanagüenñija.
Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
31 Ya güiya ilegña su sija: Maela jamyo apatte gui un lugat desierto, ya infandescansa didide; sa megae sija manjajanao, yan manmafato, ya manaelugat mañocho.
Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
32 Ya manmapos gui un batco gui un lugat desierto apatte.
Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
33 Ya y lumie sija na manjanao megae, ya matungo güe; ya manmalalago para ayo megae manmamomocat gui siuda sija, ya manmato antes qui sija, ya mandaña guiya güiya.
Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
34 Ya anae jumuyong si Jesus jalie y linajyan taotao ya ninamaase nu sija, sa manparejoja yan y quinilo sija ni taya pastotñija; ya jatutujon fumanagüe megae na güinaja.
Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 Ya anae estaba pupuenge, y disipuluña sija manmato guiya güiya, ilegñija: Y lugat desierto este, ya esta pupuenge.
Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
36 Najanao sija para ufanmalag y campo yan y sengsong sija gui oriya, ya ujafanmamajan pan para sija.
Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 Lao manope, ilegña nu sija: Nae sija mañija. Ya sija ilegñija nu güiya: Infanjanao ya infanmamajan pan pot dosientos na denario, para innae sija nañija?
Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 Ya güiya ilegña nu sija: Cuanto na pan guaja jamyo? Janao, ya inlie. Ya anae jatungo sija, ilegñija: Sinco, yan dos na güijan.
Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 Ya jatago, sija na ujanafanmatachong todos pot mangachong gui jilo y manbetde na chaguan.
Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
40 Ya manmatachong pot mangachong, siento yan siento, yan sincuenta yan sincuenta.
Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
41 Ya jachule y sinco na pan yan y dos na güijan, ya manatan julo gui langet, ya jabendise, ya jaipe y pan sija; ya janae y disipuluña sija para ujaplanta gui sanmenañija; ya y dos na güiyan manmapatte todos.
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
42 Ya mañocho todos, ya manjaspog.
Onse anadya ndipo anakhuta,
43 Ya jajatsa y pedaso sija dose na canastra manbula; yan pedaso y güijan sija locue.
ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
44 Ya ayo sija y mañocho ni pan, sinco mit na lalaje sija.
Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
45 Ya enseguidas jaapura y disipuluña sija na ufangajulo gui batco, ya ufanjanao gui menaña gui otro banda guiya Betsaida, mientras janajanao y linajyan taotao.
Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
46 Ya despues, anae munjayan janajanao sija, mapos malag y egso para ufanaetae.
Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
47 Ya anae esta pupuenge, y batco estaba gui talo gui tase, ya güiyaja namaesa gui tano.
Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
48 Ya jalie sija na manmachochocho mapot manmamómogsae, sa y manglo contrario para sija; ya jijot gui mina cuatro na guatdia gui puenge, mato güe guiya sija, mamómocat gui jilo tase; ya malago na ufalofan gui oriyañija.
Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
49 Ya anae malie nu sija, na mamómocat gui jilo tase, jinasoñija na pantasma, ya managang;
koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
50 Sa todos lumie güe, ya ninafañatsaga. Lao enseguidas jacuentuse sija, ya ilegña nu sija: Angoco jamyo, guajoyo; chamiyo fanmaaañao.
pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
51 Ya cajulo guiya sija gui batco, ya y manglo mapos: ya sija ninafangosmanman;
Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
52 Sa sija ti jatungo y milagron y pan sija; sa y corasonñija estaba mangosmajetog.
popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
53 Ya anae manmalofan para y otro banda, manmato gui tano Genesaret, ya manmalag y puetto.
Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
54 Ya anae manjuyong sija gui batco, enseguidas matungo güe.
Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
55 Ya manmalago gui oriyan todo ayo na tano, ya matutujon mañule gui todo y patte, manmalango sija gui cama, mano nae majungog na estaba güije.
Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
56 Ya manuja nae jumalom, songsong, pat suida, pat fangualuan, mapolo papa y malango sija gui chalan, y matayuyut güe na upacha y canton y magaguña, ya todo ayo sija y japacha, manjomlo.
Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.

< San Marcos 6 >