< San Juan 15 >

1 GUAJO y magajet na trongconubas ya si Tatajo güiya y magas y fangualuan.
“Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda.
2 Todo y ramas guiya guajo nu y taetinegcha, janajanao; ya todo ayo y ramas nu y gaetinegcha, janagasgas, para umegae tinegchaña.
Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri.
3 Pago nae jamyo mangasgas pot y finijo nu y jusangane jamyo.
Inu ndinu oyera kale chifukwa cha mawu amene ndayankhula inu.
4 Fañaga guiya guajo, ya guajo guiya jamyo. Taegüije y ramas ti siña mañogcha güiya namaesa, yaguin ti sumaga gui trongconubas, parejoja yan jamyo yaguin ti infañaga guiya guajo.
Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.
5 Guajo y trongconubas, jamyo y ramas. Y sumaga guiya guajo, ya guajo guiya güiya, güiya ufañogcha megae; sa apatte di guajo taya siña infatinas.
“Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu.
6 Yaguin un taotao ti sumaga guiya guajo, umanajanao güe parejoja yan y ramas, ya umalayo, ya jajojoca, ya japopolo gui guafe, ya ufanmasonggue.
Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa.
7 Yaguin mañaga jamyo guiya guajo, ya y finojo sumaga guiya jamyo, infanmangagao todo y malagomiyo ya jufatinas para jamyo.
Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa.
8 Este uninamalag si Tatajo, ya infanmanogcha megae; ya taegüenao jamyo y udisipulojo.
Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.
9 Taegüenao si Tata jaguaeya yo, guajo parejoja juguaeya jamyo locue; ya fañaga jamyo gui güinaeyaco.
“Monga momwe Atate amandikondera Ine, Inenso ndakukondani. Tsopano khalani mʼchikondi changa.
10 Yaguin inadadaje y tinagojo sija, jamyo infañañaga gui güinaeyaco; parejoja yan guajo juadadaje y tinago y Tatajo ya sumasasaga yo gui güinaeyaña.
Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo.
11 Estesija jusangane jamyo, para minagofjo usaga guiya jamyo, ya y minagofmiyo ubula.
Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira.
12 Este y tinagojo, na infanguaeya entre jamyo uno yan otro, calang y juguaeya jamyo.
Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’
13 Taya uno guaja güinaeyaña mas dangculo qui este, na y taotao japolo y linâlâfia pot y amiguña sija.
Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.
14 Jamyo y amigujo sija, yaguin infatinas jafa y jutago jamyo.
Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani.
15 Ti jagasja jufanaan jamyo tentago sija, sa y tentago ti jatungo jafa checho y magasña; lao jufanaan jamyo amigo sija; sa todosija ni jujungog gui as Tata, junatungoja jamyo.
Ine sindikutchulaninso antchito, chifukwa wantchito sadziwa zimene bwana wake akuchita. Mʼmalo mwake Ine ndakutchani abwenzi pakuti zilizonse zimene ndinaphunzira kwa Atate, Ine ndakudziwitsani.
16 Ti jamyo umayig yo, lao guajo jamyo umayig ya jutago jamyo, na infanjanao ya infanmanogcha, ya y tinegchanmiyo usaga; sa todosija y ingagao si Tata pot y naanjo, güiya infanninae.
Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
17 Estesija jutago jamyo, na infanaguaeya entre jamyo uno yan otro.
Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’
18 Yaguin manchinatlie jamyo nu y tano, intingoja na guajo finena chinatlie antes qui jamyo.
“Ngati dziko lapansi lidana nanu, dziwani kuti linayamba kudana ndi Ine.
19 Yaguin iyon y tano jamyo y tano uguaeya iyoña: lao ti iyon y tano jamyo, ya guajo jamyo umayig gui tano, ayo muna manchinatlie jamyo nu y tano.
Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani.
20 Jaso jamyo y sinangan ni munjayan jusangane jamyo: Y tentago ti dangculoña qui y magasña. Yaguin mapetsigue yo, infanmapetsigue jamyo locue; yaguin manadaje y sinanganjo, umanadaje y sinanganmiyo locue.
Kumbukirani mawu amene ndinayankhula nanu akuti, ‘Palibe wantchito amene amaposa bwana wake.’ Ngati anandizunza Ine, iwo adzakuzunzaninso inu. Ngati anamvera chiphunzitso changa, iwo adzamvera chanunso.
21 Lao todo estesija umafatinas guiya jamyo pot causan y naanjo; sa ti matungo ayo y tumagoyo.
Iwo adzakuchitani zimenezi chifukwa cha dzina langa, popeza sakudziwa amene anandituma Ine.
22 Yaguin ti matoyo, ya ti jusangane sija, taya isaoñija; lao pago taya escusañija pot y isaoñija.
Ine ndikanapanda kubwera ndi kuyankhula nawo, sakanakhala ndi mlandu. Koma tsopano alibe choti nʼkukanira mlandu wawo.
23 Ayo y chumatlie yo, güiya chumatlie si Tata locue.
Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga.
24 Yaguin ti jufatinas gui entaloñija chochosija na taya ni uno fumatinas, taya isaoñija; lao pago esta jalie ya jachatlie yo yan si Tata.
Ine ndikanapanda kuchita pakati pawo zinthu zimene wina aliyense sanachitepo, iwo sakanakhala ochimwa. Koma tsopano aona zodabwitsa izi, komabe akundida Ine pamodzi ndi Atate anga.
25 Lao este ususede, sa para umacumple y sinangan nu y matugue gui tinagoñija: sija chumatlie yo, sin jafa.
Koma zatere kuti zikwaniritse zimene zinalembedwa mʼmalamulo awo: ‘Iwo anandida Ine popanda chifukwa.’
26 Lao yaguin mato y Consoladot, ni y junamamaela guinin as Tata, y Espiritu y minagajet nu y mamaela guinin as Tata, güiya infanninae testimonio pot guajo.
“Nkhoswe ikadzabwera imene Ine ndidzakutumizireni kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu Woyera wachoonadi amene achokera kwa Atate, Iyeyo adzandichitira umboni Ine.
27 Ya jamyo locue infanmannae testimonio, sa guinin manjijita desde y tutujonña.
Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”

< San Juan 15 >