< Y Checho Y Apostoles Sija 7 >

1 AYONAE ilegña y magas mamale: Taegüine este sija?
Kenaka mkulu wa ansembe anafunsa Stefano kuti, “Kodi zimene akukunenerazi ndi zoona?”
2 Ya güiya ilegña: Mañelujo lalaje yan mañaena, ecungog. Si Yuus y minalag fumatoigüe y tatata as Abraham anae estatabaja guiya Mesopotamia, antes di usaga Charran.
Stefano anayankha kuti, “Abale ndi makolo, tamverani! Mulungu waulemerero anaoneka kwa kholo lathu Abrahamu pamene ankakhala ku Mesopotamiya, asanakakhale ku Harani.
3 Ya ilegña nu güiya: Suja gui tanomo yan y manparientesmo, ya maela jalom gui tano ni y finanuejo nu jago.
Mulungu anati, ‘Tuluka mʼdziko lako, siya abale ako, ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.’
4 Ya güiya jumanao juyong gui tano y Chaldeosija, ya sumaga Charran: ya desde ayo, anae matae si tataña, ninamalofangüe as Yuus güine mague na tano anae mañasaga jamyo pago.
“Ndipo iye anatulukadi mʼdziko la Akaldeya ndi kukakhala ku Harani. Atamwalira abambo ake, Mulungu anamuchotsa kumeneko ndi kumubweretsa mʼdziko lino limene inu mukukhalamo tsopano.
5 Ya ti ninae güe jafa na erensiaña güije, aje, taya ni para upolo y adengña gui jiloña: lao prinemete güe na uninae para güinajaña, yan y semiyaña despues di güiya, sa güiyaja trabia tataepatgon.
Mulungu sanamupatse cholowa kuno, ngakhale kadera kakangʼono kadziko. Koma Mulungu anamulonjeza kuti adzapereka dziko lino kwa iye ndi kwa zidzukulu zake, ngakhale kuti pa nthawi imeneyi analibe mwana.
6 Ya si Yuus jasangan taegüine, Na y semiyaña utaotao juyong gui ti tanoña; yan manmacone ya manmancautiba, ya manmatrata taelaye cuatro sientes años.
Mulungu anayankhula motere kwa iye: ‘Zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo, ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.’
7 Ya y nasion ni y manmancautiba, bae jujusga, ilegña si Yuus; na despues di ayo, ufanmamaela juyong ya guajo jumasetbe güine na lugat.
Mulungu anati, ‘Ine ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo, ndipo pambuyo pake akadzatuluka mʼdzikolo adzandipembedza Ine pamalo pano.’
8 Yan manae güe ni y traton sirconsision: ya si Abraham jalilis si Ysaac, ya masirconsida güe gui mina ocho na jaane; ya si Ysaac jalilis si Jacob; ya si Jacob jalilis y dose na patriarcasija.
Kenaka Mulungu anachita pangano la mdulidwe ndi Abrahamu. Ndipo Abrahamu, anabereka Isake, namudula ali ndi masiku asanu ndi atatu. Ndipo Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka makolo khumi ndi awiri aja.
9 Ya y patriarca sija pot y inigoñija, mabende si José guiya Egipto: lao si Yuus estaba guiya güiya,
“Makolo athu anachita nsanje ndi Yosefe ndipo anamugulitsa kuti akakhale kapolo ku Igupto. Koma Mulungu anali naye
10 Ya ninalibre güe todo gui chinatsaga, yan ninae güe finaborese yan tiningo, gui menan Faraon, ray guiya Egipto; yan ninamagalaje güe guiya Egipto, yan todo y guimaña.
ndipo anamupulumutsa iye kumasautso ake onse. Mulungu anamupatsa Yosefe nzeru ndi chisomo pamaso pa Farao mfumu ya ku Igupto, kotero mfumuyo inamuyika iye kukhala nduna yayikulu ya dziko la Igupto ndiponso nyumba yake yonse yaufumu.
11 Ayonae mato niñalang todo gui tano Egipto yan Charran, yan dangculon chinatsaga: ya y mañaenata ti manmañoda nengcanoñija.
“Kenaka munalowa njala mʼdziko la Kanaani, kotero kuti anthu anavutika kwambiri, ndipo makolo athu sanathe kupeza chakudya.
12 Lao anae si Jacob jajungog na guaja trigo guiya Egipto, jatago y mañaenata finenana na biaje.
Pamene Yakobo anamva kuti ku Igupto kunali tirigu, iye anatuma makolo athu ulendo woyamba.
13 Ya y mina dos biaje, matungo si José ni y mañeluña: ya y parientes José janatungo si Faraon.
Pa ulendo wawo wachiwiri, Yosefe anadziwulula kwa abale akewo ndipo Farao anadziwa za banja la Yosefe.
14 Ya manago si José na umaagange si tataña as Jacob para iya güiya, yan todo y manparientesña, setentaisinco na taotao.
Izi zinachitika, Yosefe anayitanitsa abambo ake Yakobo ndi banja lonse, onse pamodzi analipo 75.
15 Ya si Jacob jumanao papa Egipto, ya matae güije yan y mañaenata sija.
Motero Yakobo anapita ku Igupto, kumene iye ndiponso makolo athu anamwalira.
16 Ya manmachule guato Siquem, ya manmapolo gui naftan, ni y finajan Abraham pot salape, gui famaguon Emmor guiya Siquem.
Mitembo yawo anayinyamula ndi kupita nayo ku Sekemu kumene inayikidwa mʼmanda amene Abrahamu anagula kochokera kwa ana a Hamori ku Sekemuko.
17 Lao anae esta jijot y tiempon y promesa, ni y si Yuus manjula as Abraham, ya y taotao lumamegae, yan manlajyan guiya Egipto,
“Nthawi itayandikira yakuti Mulungu achite zimene analonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu unakula ndi kuchuluka kwambiri mu Igupto.
18 Asta qui y otro ray cajulo, ya ti jatungo si José.
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
19 Este jausa y malamañaña gui manparientesta, yan jatrata taelaye y mañaenata, sa janafanmayute y famaguonñija ni y pago finañago para chañija fanlalâlâ.
Mfumuyo inachita mwachinyengo ndi mtundu wathu ndi kuwazunza kuti ataye ana awo akhanda kuti afe.
20 Ya ayo na tiempo nae mafañago si Moises, ya sumenbonito; ya mapogsae gui guima tataña tres meses.
“Pa nthawi imeneyo Mose anabadwa, ndipo anali wokongola kwambiri. Iye analeredwa mʼnyumba ya abambo ake kwa miyezi itatu.
21 Ya anae mayute, y jagan Faraon jumoca, ya pinegsae para lajiña.
Atakamutaya, mwana wamkazi wa Farao anamutola nakamulera ngati mwana wake.
22 Ya si Moises, maeyag ni y todo y tiningo y taotao Egipto, ya mangaeninasiñaña y finoña yan y chechoña sija.
Mose anaphunzira nzeru zonse za Aigupto, ndipo anali wamphamvu mʼmawu ndi ntchito zake.
23 Ya anae cana jacumple cuarenta años y sacaña, mato gui corasonña na ubisita y mañeluña ni y famaguon Israel.
“Mose ali ndi zaka makumi anayi, anaganizira zokayendera abale ake Aisraeli.
24 Ya jalie uno guiya sija ni y japadese y maltrato, ya jadefiende y mumatrata, ya japuno y taotao Egipto.
Iye ataona mmodzi wa iwo akuzunzidwa ndi Mwigupto, anatchinjiriza Mwisraeliyo, namupha Mwiguptoyo.
25 Sa pineluña na jatungo y mañeluña na uninafanlibre as Yuus ni y canaeña; lao ti jatungo sija.
Mose anaganiza kuti abale ake adzazindikira kuti Mulungu anamuyika kuti awapulumutse koma iwo sanazindikire.
26 Ya y inagpaña na jaane, jafanue sija nu güiya anae managuaguat, ya malago na unaunoja talo sija, ilegña: Señores, jamyo mañelo; jafa na mananataelaye y uno yan y otro?
Mmawa mwake Mose anaona Aisraeli awiri akukangana. Iye anayesa kuwayanjanitsa ponena kuti, ‘Amuna inu, ndinu abale; chifukwa chiyani mukufuna kupwetekana?’
27 Lao ayo y minalalamen y tiguangña, jachonegñaejon, ilegña: Jaye munamagas jao gui jilo mame?
“Koma munthu amene amavutitsa mnzakeyo anakankha Mose ndipo anati, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza.
28 Malago jao unpunoyo taegüije anae unpuno nigap y taotao Egipto?
Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja dzulo?’
29 Ya ninafalago si Moises ni este na sinangan, ya tumaotao juyong gui tano Madian, gui anae jalilis y dos na lajiña.
Mose atamva mawu awa anathawira ku Midiyani, kumene anakhala mlendo ndipo anabereka ana amuna awiri.
30 Ya anae jacumple cuarenta años, mato guiya güiya un angjet gui jalomtano gui egso Sinae, gui mañila y guafe gui jalom y trongcon chaguan.
“Ndipo patapita zaka makumi anayi mngelo anaonekera kwa Mose mʼmalawi amoto pa chitsamba mʼchipululu pafupi ndi Phiri la Sinai.
31 Ya anae jalie ayo si Moises, ninagosmanman ni y liniiña; ya anae lumajijot para ugueslie, y inagang y Señot mato guiya güiya,
Iye ataona zimenezi, anadabwa. Akupita kuti akaonetsetse pafupi, Mose anamva mawu a Ambuye:
32 Ilegña: Guajo y Yuus y mañaenamo, y Yuus Abraham, yan y Yuus Ysaac, yan y Yuus Jacob. Lao si Moises manlalaolao, ya ti siña jaatan.
‘Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.’ Mose ananjenjemera chifukwa cha mantha ndipo sanalimbe mtima kuyangʼananso.
33 Ya y Señot ilegña nu güiya: Pula y sapatosmo gui adengmo; sa y lugat anae tumotojgue jao, santos na oda.
“Ndipo Ambuye anati kwa Mose, ‘Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.
34 Sa seguro julie, y manmasapet y taotaojo guiya Egipto, yan jujungog y inigongñiñija, ya tumunogyo para junafanlibre sija. Ya pago maela jao, sa jutago jao guato Egipto.
Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse. Tsopano tiye ndikutume ku Igupto.’
35 Este y as Moises ni y jarechasa ilegñija: Jaye munamagas jao yan unjues? Güiya tinago as Yuus na umagas yan uninafanlibre pot y canae y angjet ni y mafato guiya güiya gui jalomtano.
“Uyu ndi Mose yemwe uja amene Aisraeli anamukana ndi kunena kuti, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza?’ Iyeyo anatumidwa ndi Mulungu mwini kuti akakhale wowalamulira ndiponso mpulumutsi, mothandizidwa ndi mngelo amene anamuonekera pa chitsamba.
36 Güiya chumule sija juyong, ya despues manfinanue ni y namanman, yan señat sija gui tano Egipto, yan y Tasen Agaga, yan y jalomtano cuarenta anos.
Iye anawatulutsa mu Igupto ndipo anachita zodabwitsa ndi zizindikiro zozizwitsa mu Igupto, pa Nyanja Yofiira, ndiponso mʼchipululu kwa zaka makumi anayi.
37 Este ayo y as Moises, ni y ilegña ni y famaguon Israel: Y Yuusmiyo janacajulo un profeta guiya jamyo gui mañelunmiyo taegüine iya guajo.
“Uyu ndi Mose uja amene anati kwa Aisraeli, ‘Mulungu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine.’
38 Este ayo y estaba gui inetnon, gui jalomtano, yan y angjet ni y cumuentuse güe gui egso Sinae, yan y mañaenata; ni y rumesibe y nalâlâ na tinago para ufanmanaejit.
Iyeyu anali mʼgulu la Aisraeli mʼchipululu pamodzi ndi mngelo amene anamuyankhula pa phiri la Sinai ndiponso makolo athu; ndipo Mose analandira mawu amoyo kuti atipatse ife.
39 Ni y mañaenata ti manmalago jaosgue lao mayute juyong guiya sija, ya y corasonñija manalo tate Egipto,
“Koma makolo athu anakana kumumvera iye. Iwo anamukana iye ndipo mʼmitima mwawo anatembenukira ku Igupto.
40 Ilegñija as Aaron: Fatinasejam Yuus para ujanao gui menanmame, as este y as Moises ni y cumonejam juyong gui tano Egipto, ti intingo jafa ujuyong.
Iwo anati kwa Aaroni, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitsogolera kutuluka mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.
41 Ya sija manmamatinas un tatnero, ya machule y inefrese para idolo sija, güije sija na jaane, ya ninafansenmagof ni y checho y canaeñija.
Iyi ndi nthawi imene anapanga fano la mwana wangʼombe. Anapereka nsembe kwa fanoli nachita chikondwerero kulemekeza ntchito ya manja awo.
42 Ayonae jabira si Yuus, ya japolo na ujaadora y inetnon y langet; taegüije esta matugue gui leblon y profeta: O jamyo ni y guima Israel, inofreseyo pinino gâgâ sija yan inefrese sija gui cuarenta años gui jalomtano?
Koma Mulungu anawafulatira, nawapereka kuti apembedze zolengedwa zakumwamba. Zimenezi zikugwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la aneneri kuti, “‘Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?’
43 Yan injatsa y tabemaculon Moloc, yan y estreyas y Yuus Refán, jechura sija ni y infatinas para inadora sija; ya guajo juchule jamyo mas chago qui Babilonia.
Ayi, inu mwanyamula tenti ya Moloki ndi nyenyezi ya mulungu wanu Refani, mafano amene munapanga kuti muziwapembedza. Chifukwa chake, Ine ndidzakutumizani kutali, kupitirira dziko la Babuloni.
44 Y mañaenata, guaja ni y tabernaculon y testimonio gui jalomtano, taegüije tinanchoña ni ilegña as Moises na ufatinas taemanoja na jechura y liniiña.
“Makolo athu anali ndi tenti ya msonkhano pakati pawo mʼchipululu. Anayipanga monga momwe Mulungu anawuzira Mose, molingana ndi chithunzi chimene Mose anachiona.
45 Ni y mañaenata locue gui tiempoñija a machule jalom yan si Josué anae jumalom gui erensian y Gentiles, ni y si Yuus yumute juyong gui menan y mañaenata, asta y jaanen David;
Makolo athu, atayilandira Tentiyo, anabwera nayo motsogozedwa ndi Yoswa pamene analanda dziko la mitundu imene Mulungu anayipirikitsa pamaso pawo. Tentiyo inakhala mʼdzikomo mpaka nthawi ya Davide,
46 Ni y sumoda finaborese gui menan Yuus, yan jagagao na ualiligao tabernaculo para si Yuus Jacob.
amene anapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndipo anapempha kuti amʼmangire nyumba Mulungu wa Yakobo.
47 Lao si Salomon fumatinase güe un guma.
Koma anali Solomoni amene anamanga nyumbayo.
48 Sa y Gueftaquilo, ti sumasaga gui guima sija ni y finatinas canae; taegüije y sinangan y profeta.
“Komatu, Wammwambamwambayo sakhala mʼnyumba zomangidwa ndi anthu. Monga mneneri akunena kuti,
49 Y langet tronujo, ya y tano fañajangan y papa adengjo; jafa na guma injatsayeyo? ilegña y Señot; pat jafa na sagayan nae jusaga?
“‘Kumwamba ndi mpando wanga waufumu, ndipo dziko lapansi ndi chopondapo mapazi anga. Kodi mudzandimangira nyumba yotani? Akutero Ambuye. Kapena malo opumuliramo Ine ali kuti?
50 Ada ti y canaejo fumatinas todo este sija na güinaja?
Kodi si dzanja langa linapanga zonsezi?’
51 Jamyo ni y gaetongjo tiso, yan ti manmasirconsida y corason yan y talanga, sa siempre incontra y Espiritu Santo; taegüije y checho y mañaenanmiyo inchechegüe.
“Anthu wokanika inu, osachita mdulidwe wa mu mtima ndi a makutu ogontha! Inu ofanana ndi makolo anu. Nthawi zonse mumakana kumvera Mzimu Woyera:
52 Jaye gui profeta ti japetsigue y mañaenanmiyo? ya japuno ayo sija y manmañangangane antes ni y mamamaela Uno na Tunas; ya jamyo pago inentrega, yan inpino;
Kodi analipo mneneri amene makolo anu sanamuzunze? Iwo anapha ngakhale amene ananeneratu za kubwera kwa Wolungamayo. Ndipo tsopano inu munamupereka ndi kumupha Iye.
53 Ni y inresibe y tinago pot y inareglan y angjet, ya ti inadaje.
Inu amene munalandira Malamulo amene anaperekedwa ndi angelo ndipo simunawamvere.”
54 Ya anae jajungog estesija, manchinachat asta y corasonñija, ya janafañegcheg y nifenñija guiya güiya.
Atamva zimenezi, iwo anakwiya kwambiri ndipo anamukukutira mano.
55 Lao güiya, bula ni y Espiritu Santo, ya jaatan meton y langet, ya jalie y minalag Yuus, yan si Jesus na tumotojgue gui agapa na canae Yuus.
Koma Stefano, wodzaza ndi Mzimu Woyera, anayangʼana kumwamba ndipo anaona ulemerero wa Mulungu ndiponso Yesu atayimirira ku dzanja lamanja la Mulungu.
56 Ya ilegña, Estagüe na julie y langet na mababa, ya y Lajin taotao tumotojgue gui agapa na canae Yuus.
Stefano anati, “Taonani, ndikuona kumwamba kotsekuka ndiponso Mwana wa Munthu atayimirira ku dzanja la manja la Mulungu.”
57 Ayonae sija managang ni y dangculo na inagangñija, yan jatampe y talanganñija, ya manmalago guato guiya güiya;
Koma iwo anatseka mʼmakutu mwawo, ndipo anafuwula kolimba, onse anathamangira kwa iye,
58 Ya mayute juyong gui siuda, ya mafagas ni y acho: ya y testigo sija, japolo papa y magagoñija gui adeng un patgon na taotao na y naanña si Saulo.
anamukokera kunja kwa mzinda ndipo anayamba kumugenda miyala. Mboni zinasungitsa zovala zawo kwa mnyamata otchedwa Saulo.
59 Ya mafagas ni y acho si Esteban, ya jaaagang ni Yuus, ilegña: Señot, Jesus, resibe y Espiritujo.
Akumugenda miyala, Stefano anapemphera kuti, “Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.”
60 Ya dumimo papa, ya umagang ni y dangculo na inagangña, ilegña: Señot, chamo pumopolo este na isao gui cuentanñija; ya anae munjayan jasangan este, maego.
Ndipo anagwada pansi nafuwula mwamphamvu kuti, “Ambuye musawawerengere tchimoli.” Atanena mawu amenewa anamwalira.

< Y Checho Y Apostoles Sija 7 >