< Софоний 3 >
1 Горко на бунтовния и скверен град, На насилническия град!
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 Той не послуша гласа, Не прие поправление, Не упова на Господа, Не се приближи при своя Бог.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Първенците всред него са рикаещи лъвове, Съдиите му вечерни вълци, Които не остават нищо за заранта.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Пророците му са вятърничави коварници; Свещениците му оскверниха светилището, Извратиха закона.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 Господ всред него е праведен; Няма да извърши неправда; Всяка заран изкарва на видело правосъдието си - неизменно; Но неправедният не знае срам.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 Изтребих народи; ъглените им кули са запустели; Запустих пътищата им, тъй че никой не минава; Градовете им се разориха, Тъй че няма човек в тях, няма жител.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 Рекох си: Ти непременно ще се убоиш от мене, Ще приемеш поправление; И така селището му не щеше да се изтреби Според всичко онова, което му определих; Но те подраниха да извратят всичките си дела.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 За това, чакайте Мене, казва Господ, До деня, когато се повдигна, за да обират. Защото решението ми е да събера народите, И да прибера царствата, За да излея върху тях негодуванието си, Всичкия си лют гняв; Понеже цялата земя ще бъде погълната От огъня на ревнивостта ми.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 Защото тогава ще възвърна на племената чисти устни, За да призовават всичките името Господне, Да му слугуват единодушно.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Изотвъд Етиопските реки поклонниците ми, Разсеяните ми юлде, Ще ми донесат принос.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 В оня ден няма да бъдеш засрамен Поради многото дела, Чрез които си беззаконствал против Мене; Защото до тогава ще съм махнал отсред тебе ония от тебе, Които горделиво тържествуват; И ти няма вече да се носиш надемнно в светия Ми хълм.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 Но ще оставя всред тебе Люде съкрушени и нищи, Които ще уповават на името Господне.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 Останалите от Израиля няма да беззаконстват, Нито да лъжат, Нито ще се намери в устата им измамлив език; Защото те ще пасат и ще лежат, И никой няма да ги плаши.
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 Пей, Сионова Дъщерьо, Вьзкликнете, Израилю, Весели се и радвай се от все сърце, Ерусалимска дъщерьо;
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 [Защото] Господ отмени присъдите за тебе, Изхвърли неприятеля ти; Цар Израилев, да! Господ, е всред тебе; Няма вече да видиш зло.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 В оня ден ще се рече на Ерусалим - Не бой се, И на Сион - да не отслабват ръцете ти.
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 Господ твой Бог е всред тебе, Силният, който ще те спаси; Ще се развесели за тебе с радост, Ще се успокои в любовта си, Ще се весели за тебе с песни.
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 Ще събера ония, които бяха от тебе, Които скърбят за празниците, И на които тежи укора му.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Ето, в онова време ще се разправя с всички, които те угнетяват, Ще избавя куцата, ще прибера изгонената, И ще направя ония за хвала и слава, Чийто срам е бил в целия свят.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 В онова време ще ви доведа пак, И в онова време ще ви събера; Защото ще ви направя именити и похвални Между всичките племена на земята, Когато върна пленниците ви пред очите ви, казва Господ.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.