< Захария 9 >

1 Господното слово наложено на мене за земята Адрах, което ще се изпълни над Дамаск, (защото Господните очи са върху всички човеци както и върху всичките Израилеви племена),
Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
2 Още и над Емат, който граничи с него, и над Тир и Сидон, ако и да са много мъдри.
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
3 Тир си съгради крепост, И натрупа сребро като пръст, И чисто злато като калта по пътищата.
Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
4 Ето, Господ ще го изтощи, И ще порази силата му по морето, И той ще бъде погълнат от огън;
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
5 Аскалон ще види и ще се уплаши; И Газа, и ще се наскърби много; И Акарон, защото ще се посрами за това, което очакваше, Царят ще погине от Газа, И Аскалон няма да се насели.
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
6 Узурпаторско племе ще седне като цар на Азот; И Аз ще прекратя гордостта на филистимците.
Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
7 Ще отнема кръвта от устата им, И гнусотиите измежду зъбите им; И който остане ще бъде и той за нашия Бог, И ще бъде като хилядник в Юда, И Акарон като невусецът.
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
8 Около дома Си ще разположа Своя стан в защита против войска, Та да не премине никой или се върне; И никой насилник няма вече да замине през тях, Защото сега видях с очите Си.
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
9 Радвай се много синова дъщерьо; Възклицавай ерусалимска дъщерьо; Ето, твоят цар иде при тебе; Той е праведен, и спасява, Кротък и възседнал на осел, Да! На осле, рожба на ослица.
Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
10 Аз ще изтребя колесница из Ефрема, И кон из Ерусалим И ще се отсече бойният лък; Той ще говори мир на народите; И владението Му ще бъде от море до море, И от Ефрат до земните краища.
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11 А колкото за тебе, Израилю, по причина на кръвта на сторения от тебе завет с Мене, Аз извадих затворниците ти Из безводния ров.
Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12 Върнете се в крепостта, Вие обнадеждени затворници; Още днес възвестявам, Че ще ти въздам двойно;
Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13 Защото ще запъна Юда за Себе Си като лък, Ще туря Ефрема като стрела; И ще възбудя чадата ти, Сионе, Против твоите чада Гърцио, И ще те направя като меч на силен дъжд.
Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
14 Господ ще се яви над тях, И стрелата Му ще излезе като мълния; И Господ Иеова ще затръби, И ще върви с южни вихрушки.
Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15 Господ на Силите ще ги защищава; И те ще погълнат противниците, и ще ги повалят с камъни от прашка; И ще пият, ще правят шум като от вино, И ще се изпълнят като паница, Като ъглите на олтара.
ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
16 И в оня ден Господ техният Бог ще ги избави Като Свои люде, за да бъдат Негово стадо; Понеже ще бъдат като камъни на корона Блестящи над земята Му.
Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17 Защото колко велика е благостта Му, И колко голяма красотата Му! Житото ще направи юношите да цъфтят, И мъстът девиците.
Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.

< Захария 9 >