< Захария 2 >

1 След това, подигнах очите си и видях, и ето човек с връв за мерене в ръката му.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
2 Тогава рекох: Къде отиваш? А той ми рече: Да измеря Ерусалим, за да видя каква е широчината му и каква е дължината му.
Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
3 ето, ангелът, който говореше с мене, излезе; и друг ангел излезе да го посрещне, и му рече:
Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
4 Тичай, говори на тоя юноша, като кажеш: Ерусалим ще се насели без стени, поради многото човеци и добитък в него;
ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
5 защото Аз, казва Господ, ще бъда огнена стена около него, и ще бъда славата всред него.
Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
6 О! о! бягайте от северната земя, казва Господ, защото ще ви разширя към четирите небесни ветрища, казва Господ.
“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
7 О! отърви се, сионова дъщерьо, която живееш със вавилонската дъщеря.
“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
8 Защото така казва Господ на Силите: След възстановяването на славата Той ме изпрати при народите, които ви ограбиха; понеже който докача вас, докача зеницата на окото Му.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
9 Защото ето, аз ще помахам с ръката си върху тях, и ще станат корист на ония, които им са работили: и ще познаете, че Господ на Силите ме е изпратил.
Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
10 Пей и радвай се, Сионова дъщерьо; защото, ето, Аз ида, и ще обитавам всред тебе, казва Господ.
“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
11 И в оня ден много народи ще се прилепят при Господа, и ще бъдат Мои люде и Аз ще обитавам всред тебе, и ще познаеш, че Господ на Силите ме е изпратил при тебе.
“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
12 И Господ ще наследи Юда за Свой дял в светата земя, и пак ще избере Ерусалим.
Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
13 Млъкни, всяка твар, пред Господа; защото Той се е събудил от своето Си обиталище.
Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”

< Захария 2 >