< Песен на песните 1 >

1 Соломоновата песен на песните.
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 Нека ме целуне с целувките на устата си, Защото любовта ти е по-желателна от виното.
Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Твоите масла са благоуханни; Името ти е ароматно като изляно масло; Затова те обичат девиците.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Привлечи ме; ние ще тичаме след тебе. Царят ме въвежда във вътрешните си стаи; Ще се радваме и ще веселим за тебе, Ще спомняме твоята любов повече от виното; С право те обичат!
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 Черна съм, но хубава, ерусалимски дъщери, Като кидарските шатри, като Соломоновите завеси.
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 Не ме гледайте, че съм почерняла, Понеже слънцето ме е припърлило. Синовете на майка ми, като се разгневиха на мене, Поставиха ме пазачка на лозята; Но своето лозе но опазих.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Кажи ми ти, кого люби душата ми, Где пасеш стадото си, где го успокояваш на пладне; Че защо да съм като една, която се скита Край стадата на твоите другари?
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
8 Ако ти не знаеш, хубавице между жените, Излез по дирите на стадата И паси яретата си при шатрите на овчарите.
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
9 Уподобих те, любезна моя, На конете от Фараоновите колесници.
Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Красиви са твоите бузи с плетенки, И шията ти с огърлици.
Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Ще ти направим златни плетеници Със сребърни копчета.
Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
12 Докато царят седи на трапезата си, Нардът ми издава благоуханието си.
Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Възлюбеният ми е за мене като китка от смирна, Която лежи между гърдите ми.
Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Възлюбленият ми е за мене като кипрова китка В лозята на Енгади.
Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
15 Ето, хубава си, любезна моя, ето, хубава си; Очите ти са като на гълъбите.
Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
16 Ето, хубав си, любезни ми, да! Приятен си; И постелката ни е зеленината.
Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
17 Гредите на къщите ни са кедрови, Дъските ни са кипарисови.
Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.

< Песен на песните 1 >