< Рут 2 >

1 А Ноемин имаше един сродник по мъжа си, много имотен човек, от рода на Елимелеха, на име Вооз.
Naomi anali ndi mʼbale wake wolemera kwambiri wochokera ku banja la mwamuna wake Elimeleki, dzina lake Bowazi.
2 И моавката, Рут, каза на Ноемин: Да отида на нивата да събирам класове подир онзи, чието благоволение придобия. И тя й рече: Иди, дъщерьо моя.
Tsiku lina Rute, Mmowabu uja anati kwa Naomi, “Mundilole kuti ndikakunkhe barele ku munda wa munthu aliyense amene akandikomere mtima.” Naomi anati kwa iye, “Pita mwana wanga.”
3 И тя отиде, и като стигна, събираше класове в нивата подир жътварите; и случи се да попадне на нивата, която беше дал на Вооза, човекът от рода на Елимелеха.
Choncho Rute ananyamuka kupita kukakunkha ku minda yokololedwa kale. Tsono zinangochitika kuti Rute anafika mʼmunda wa Bowazi, yemwe anali wochokera ku banja la Elimeleki.
4 И, Ето, Вооз дойде от Витлеем та рече на жътварите: Господ с вас! И те му отговориха: Господ да те благослови!
Posakhalitsa Bowazi anafika kuchokera ku Betelehemu ndipo analonjera okolola aja kuti, “Yehova akhale nanu!” Iwo anayankha kuti, “Yehova akudalitseni.”
5 Тогава Вооз рече на слугата си, настойника на жътварите: Чия е тая млада жена?
Bowazi anafunsa kapitawo wake amene ankayangʼanira okolola aja kuti, “Mayi uyo ndi ndani?”
6 И слугата, настойникът на жътварите, рече в отговор: Тая млада жена е моавката, която се върна с Ноемин от Моавската земя;
Kapitawo uja anayankha kuti, “Mayiyu ndi Mmowabu amene anabwera ndi Naomi kuchokera ku dziko la Mowabu.
7 и тя рече: Да бера, моля, класове, и да събера нещо между снопите подир жътварите. И тъй, тя дойде та стоя от сутринта до сега, само че си почина малко в къщи.
Iye anandipempha kuti, ‘Chonde mundilole kuti ndikunkhe barele mʼminda moti akololamo kale.’ Iye wakhala akukunkha kuyambira mmawa mpaka tsopano lino osapuma nʼpangʼono pomwe.”
8 Тогава Вооз рече на Рут: Чуеш ли ме, дъщерьо моя? не ходи да събираш класове на друга нива, и да си не отидеш от тук, но стой тук при момичетата ми.
Choncho Bowazi anati kwa Rute, “Tamvera mwana wanga, usapite kukakunkha mʼmunda wina, ndipo usachoke mʼmunda uno. Koma uzitsata adzakazi angawa.
9 Нека очите ти бъдат в нивата, гдето ще жънат, и ходи подир тях; ето, аз заръчах на момчетата да се не досягат до тебе; и когато си жадна, иди при съдовете та пий от онова, което момчетата са налели.
Uziyangʼana munda akukolola anyamatawo akamakolola mʼmundamu, ndipo iwe uzitsata pambuyo pawo. Ndawawuza anyamatawo kuti asakuvutitse. Ndipo ukamva ludzu, uzipita ku mitsuko ndi kukamwa madzi amene anyamatawa atunga.”
10 И тя падна на лице та се поклони до земята, и рече му: Как придобих аз твоето благоволение, та да ме пригледаш, като съм чужденка?
Atamva zimenezi Rute anawerama nazolikitsa nkhope yake pansi. Kenaka anafunsa kuti, “Mwandikomera mtima chotere mlendo ngati ine chifukwa chiyani?”
11 А Вооз в отговор и рече: Каза ми се напълно всичко, що се сторила на свекърва си подир смъртта на мъжа си, и как си оставила баща си и майка си и родината си, та си дошла между люде, които по-преди не си познавала.
Bowazi anayankha kuti, “Ine ndawuzidwa zonse zimene wakhala ukuchitira apongozi ako chimwalirire mwamuna wako. Ndamvanso kuti unasiya abambo ndi amayi ako komanso dziko la kwanu ndi kubwera kudzakhala ndi anthu amene sumawadziwa ndi kale lonse.
12 Господ да ти отплати за делото ти, и пълна награда да ти се даде от Господа Израилевия Бог, под чиито крила си дошла да се подслониш.
Yehova akubwezere pa zimene wachitazi. Yehova Mulungu wa Israeli, amene wabwera pansi pa mapiko ake kuti akuteteze, akupatse mphotho yayikulu.”
13 И тя рече: Да придобия твоето благоволение, господарю мой; понеже ти ме утеши и понеже говори благосклонно на слугинята си, ако и да не съм като някоя от твоите слугини.
Rute anati, “Mwandikomera mtima, mbuye wanga. Ndipo mwandisangalatsa ndi kundiyankhula mwa chifundo ngakhale sindili mmodzi mwa adzakazi anu.”
14 И когато настана времето за ядене, Вооз й рече: Дойди тука, та яж от хляба, и натопи залъка си в оцета. Тя, прочее, седна до жътварите; а той й подаде пържена пшеница, та яде и се насити и остави нещо.
Nthawi ya chakudya cha masana Bowazi anati kwa iye, “Bwera kuno, utenge buledi ndi kusunsa nthongo mu vinyo.” Choncho anakhala pansi pafupi ndi okololawo, ndipo Bowazi anamupatsa chakudya ndi nyama yowotcha. Anadya chilichonse amafuna ndipo chakudya china chinatsalako.
15 А като стана да бере класове, Вооз заповяда на момчетата си, като каза: И между снопите нека събира класове; не я мъмрете;
Atanyamuka kuti azikakunkha, Bowazi analangiza anyamata ake kuti, “Ngakhale mayiyu azikunkha pakati pa mitolo musamuletse ndi kumuchititsa manyazi.
16 и даже изваждайте нещо за нея от ръкойките и оставяйте го, и нека го събира без да й забранявате.
Koma muzimusololerako ngala zina za mʼmitolo ndi kumusiyira kuti azikunkha ndipo musamukalipire.”
17 Така тя береше класове в нивата до вечерта; па очука събраното, и то беше около една ефа ечемик.
Choncho Rute anakunkha mʼmundamo mpaka madzulo. Kenaka anapuntha barele anakunkhayo, ndipo anakwanira pafupifupi makilogalamu khumi.
18 И взе това та влезе в града, и свекърва й видя колко класове бе събрала; и Рут извади та й даде онова, което беше оставила след като се бе наситила.
Anasenza barele uja kupita naye ku mudzi, nakaonetsa apongozi ake. Kenaka anatulutsa chakudya chimene chinatsalira atakhuta chija ndi kupatsa apongozi ake.
19 И свекърва й рече: Где събира днес класове? и где работи? Благословен да бъде оня, който те пригледа. И тя яви на свекърва си в чия нива бе работила, като каза: Името на човека, у когото работих днес, е Вооз.
Apongozi akewo anamufunsa kuti, “Kodi lero unakakunkha kuti? Unakagwira kuti ntchitoyi? Adalitsike munthu amene anakukomera mtimayo.” Ndipo Rute anawuza mpongozi wake za munthu amene ku malo ake anakagwirako ntchito. Iye anati, “Munthuyo dzina lake ndi Bowazi.”
20 И Ноемин рече на снаха си: Благословен от Господа оня, който не лиши от милостта си ни живите, ни умрелите. Рече и още Ноемин: Тоя човек е от нашия род, близък нам сродник.
Naomi anati kwa mpongozi wakeyo, “Munthu ameneyu amudalitse Yehova, amene sanasiye kuchitira chifundo anthu amoyo ndi akufa omwe. Anatinso munthu ameneyu ndi mnansi wapaphata. Ndiye ali ndi udindo wotisamalira.”
21 И Рут моавката каза: При това, той ми рече: Да не се делиш от момчетата ми докато не свършат цялата ми жътва.
Choncho Rute Mmowabuyo anati, “Iye anandiwuzanso kuti, ‘Uzitsata antchito angawa mpaka atamaliza kukolola munda wonse.’”
22 И Ноемин рече на снаха си Рут: Добре е, дъщерьо моя, да излизаш с неговите момчета, и да те не срещат в друга нива.
Naomi anati kwa Rute mpongozi wake, “Kuli bwino mwana wanga kuti uzipita ndi adzakazi ake kuopa kuti mʼmunda wa munthu wina angakuvute.”
23 И така, тя се привърза при момчетата на Вооза, за да бере класове догде се свърши ечемичната жътва и пшеничната жътва; и седеше със свекърва си.
Choncho Rute ankatsatira adzakazi a Bowazi namakunkha mpaka anthu atamaliza kudula barele ndi tirigu. Ndipo amakhalabe ndi mpongozi wakeyo.

< Рут 2 >