< Псалми 57 >
1 За първия певец, по не разорявай. Песен на Давида, когато побягна от Сауловото лице в пещерата. Смили се за мене, о Боже, смили се за мене, Защото при Тебе прибягва душата ми; Да! Под сянката но Твоите крила ще прибягна, Докато преминат тия бедствия.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Ще викам към Всевишния Бог, Към Бога, Който действува за мене.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Ще прати от небесата и ще ме избави, Когато ме укорява оня, който иска да ме погълне. (Села) Бог ще изпрати милостта Си и истината Си.
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Душата ми е всред лъвовете; Лежа между пламнали човеци, Между човешки чада, чиито зъби са копия и стрели, И чиито език е остър меч.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Възнеси се, Боже, над небесата; Славата Ти нека бъде по цялата земя.
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Мрежи приготви за стъпките ми; Душата ми се е навела; Изкопаха пред мене яма; Те сами паднаха всред тия. (Села)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Непоколебимо е сърцето ми, Боже, непоколебимо е сърцето ми; Ще пея, а ще славословя.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Събуди се, душе моя; Събуди се, псалтирю и арфо; сам аз ще се събудя на ранина.
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Ще те хваля, Господи, между племената; Ще те славословя между народите.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Защото Твоята милост е велика дори до небесата. И Твоята вярност до облаците.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Възнеси се, Боже, над небесата; Славата Ти нека бъде по цялата земя.
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.