< Псалми 27 >
1 Давидов псалом. Господ е светлина моя и избавител мой; От кого ще се боя? Господ е сила на живота ми; От кого ще се уплаша?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 Когато се приближиха при мене злосторници, Противниците ми и неприятелите ми, За да изядат плътта ми, Те се спънаха и паднаха.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 Ако се опълчи против мене и войска, Сърцето ми няма да се уплаши; Ако се подигне против мене война И тогава ще имам увереност.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 Едно нещо съм поискал от Господа, това ще търся, - Да живея в дома Господен през всичките дни на живота си. За да гледам привлекателността на Господа. И да Го диря в храма Му.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 Защото в зъл ден ще ме скрие под покрива Си, Ще ме покрие в скривалището на щита Си, Ще ме издигне на канара.
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 И сега главата ми ще се издигне Над неприятелите ми, които ме окръжават; И ще принеса в скинията Му жертва на възклицания, Ще пея, да! ще славословя Господа.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Слушай, Господи, гласа ми, когато викам; Смили се тоже за мене, и отговори ми.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 Когато Ти рече: Търсете лицето Ми, Моето сърце Ти каза: Лицето Ти ще търся, Господи.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Да не скриеш от мене лицето Си; Да не отхвърлиш с гняв слугата Си; Ти ми стана помощ; недей ме отхвърля, И недей ме оставя, Боже, Спасителю мой;
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Защото баща ми и майка ми са ме оставили: Господ, обаче, ще ме прибере.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Научи ме, Господи, пътя Си, И води ме по равна пътека поради ония, които ме причакват.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Да не ме предадеш на волята на противниците ми; Защото лъжливи свидетели са се дигнали против мене, Които дишат насилие.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 Ако не бях повярвал, че ще видя благостите Господни В земята на живите - бих премалял.
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Чакай Господа; Дерзай, и нека се укрепи сърцето ти; Да! чакай Господа.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.