< Псалми 2 >

1 Защо се разоряват народите, И племената намислюват суета?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Опълчват се земните царе, И управниците се наговарят заедно, Против Господа и против Неговия помазаник, като казват:
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Нека разкъсаме връзките им, И нека отхвърлим от себе си въжетата им.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Тоя, Който седи на небесата, ще се смее; Господ ще им се поругае.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Това ще им продума в гнева Си, И в тежкото Си негодувание ще ги смути, казвайки:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Но Аз поставих Царя Си На Сион, светия Мой хълм.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 Аз ще изявя постановлението; Господ ми каза: Ти си Мой Син; Аз днес те родих.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Поискай от Мене и Аз ще ти дам народите за твое наследство, И земните краища за твое притежание.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Ще ги съкрушиш с желязна тояга, Ще ги строшиш като грънчарски съд.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Сега, прочее, вразумете се, о царе; Научете се земни съдии.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Слугувайте на Господа със страх, И радвайте се с трепет.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Целувайте Избраника, за да се не разгневи, Та погинете в пътя; Защото скоро ще пламне Неговият гняв. Блажени са всички, които се надяват на Него.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Псалми 2 >