< Псалми 145 >
1 Давидово хваление. По еврейски азбучен псалом. Ще Те превъзнасям, Боже мой, Царю мой, И ще благославям Твоето име от века до века.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Всеки ден ще Те благославям, И ща хваля Твоето име от века и до века.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Велик е Господ и твърде достохвален, И величието Му е неизследимо.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Едно поколение ще хвали делата Ти на друго, И ще разказват Твоето могъщество,
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Ще размишлявам за славното величие на Твоето достойнство, И за Твоите чудесни дела;
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 И когато човеците говорят за мощта на Твоите страшни дела, То и аз ще разказвам Твоето величие.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Ще разгласяват спомена на Твоята голяма благост, И ще възпяват Твоята правда.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Благодатен и жалостив е Господ, Дълготърпелив и многомилостив.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Благ е Господ към всички; И благите Му милости са върху всичките Му творения.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Всичките Твои творения ще Те хвалят, Господи, И Твоите светии ще Те благославят;
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Ще говорят за славата на царството Ти, И ще разказват Твоето могъщество,
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 За да изявят на човешките чада мощните Му дела, И славното величие на Неговото царство.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Твоето царство е вечно, И владичеството Ти трае през всички родове.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Господ подкрепя всичките падащи, И изправя всичките сгърбени.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Очите на всички гледат към Тебе; И Ти им даваш храна на време.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Отваряш ръката Си И удовлетворяваш желанието на всичко живо.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Праведен е Господ във всичките Си пътища, И благодатен във всичките Свои дела.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Господ е близо при всички, Които Го призовават, При всички, които с истина Го призовават.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Изпълнява желанието на тия, които Му се боят, Слуша викането им и ги избавя,
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Господ пази всички, които Го любят; А ще изтреби всичките нечестиви.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Устата ми ще изговарят хваление на Господа; И всяка твар нека благославя Неговото свето име от века и до века.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.