< Притчи 6 >
1 Сине мой, ако си станал поръчител на ближния си, Или си дал ръка за някой чужд,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 Ти си се впримчил с думите на устата си, Хванат си с думите на устата си.
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Затова, сине мой, направи това и остави се, Тъй като си паднал в ръцете на ближния си, - Иди, припадни и моли настоятелно ближния си.
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Не давай сън на очите си, Нито дрямка на клепачите си,
Usagone tulo, usawodzere.
5 Догдето не се отървеш, като сърна от ръката на ловеца, И като птица от ръката на птицоловец.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Иди при мравката, о ленивецо, Размишлявай за постъпките й и стани мъдър,
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 Който, макар че няма началник, Надзирател, или управител,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 Приготвя си храната лете, Събира яденето си в жътва.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 До кога ще спиш лицемерецо? Кога ще станеш от съня си?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Още малко спане, малко дрямка, Малко сгъване на ръце за сън,
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 Така ще дойде сиромашия върху тебе, като разбойник, И немотия, като въоръжен мъж.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 Човек нехранимайко, човек беззаконен, Е оня който ходи с извратени уста,
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 Намигва с очите си, говори с нозете си, Дава знак с пръстите си;
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 Който има извратено сърце, Непрестанно крои зло, сее раздори,
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Затова погубването му ще дойде внезапно; Изведнъж ще се съкруши, и то непоправимо.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 Шест неща мрази Господ, Даже седем са мерзост за душата Му:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 Надменни очи, лъжлив език, Ръце, които проливат невинна кръв,
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 Сърце, което крои лоши замисли, Нозе, които бърже тичат да вършат зло,
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 Неверен свидетел, който говори лъжа, И оня, който сее раздори между братя.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 Сине, мой, пази заповедта на баща си, И не отстъпвай от наставлението на майка си,
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Вържи ги за винаги за сърцето си, Увий ги около шията си.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 Когато ходиш наставлението ще те води, Когато спиш, ще те пази; Когато се събудиш ще се разговаря с тебе,
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 Защото заповедта им е светилник, И наставлението им е светлина, И поучителните им изобличения са път към живот.
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 За да те пазят от лоша жена, От ласкателния език на чужда жена.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Да не пожелаеш хубостта й в сърцето си; Да не те улови с клепачите си;
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 Защото поради блудница човек изпада в нужда за парче хляб; А прелюбодейката лови скъпоценната душа.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Може ли някой да тури огън в пазухата си, И дрехите му да не изгорят?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Може ли някой да ходи по разпалени въглища, И нозете му да се не опекат?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 Така е с оня, който влиза при жената на ближния си; Който се допре до нея не ще остане ненаказан.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Дори крадецът не се пропуска ненаказан, Даже ако краде да насити душата си, когато е гладен;
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 И ако се хване, той трябва да възвърне седмократно, Трябва да даде целия имот на къщата си.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Оня, който прелюбодействува с жена е безумен. Който прави това би погубил душата си.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Биене и позор ще намери, И срамът му няма да се изличи,
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 Защото ревнуването на мъжа е една ярост; И той няма да пожали в деня на възмездието;
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 Не ще иска да знае за никакъв откуп, Нито ще се умилостиви, ако и да му дадеш много подаръци.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.