< Притчи 24 >
1 Не завиждай на злите хора, Нито пожелавай да си с тях,
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 Защото сърцето им размишлява насилие, И устните им говорят за пакост
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 С мъдрост се гради къща, И с разум се утвърждава,
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 И чрез знание стаите се напълват С всякакви скъпоценни и приятни богатства.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 Мъдрият човек е силен, И човек със знание се укрепява в сила,
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 Защото с мъдър съвет ще водиш войната си, И чрез множеството съветници бива избавление.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Мъдростта е непостижима за безумния, Той не отваря устата си в портата.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 Който намисля да прави зло, Ще се нарече пакостен човек;
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 Помислянето на такова безумие е грях, И присмивателят е мерзост на човеците.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 Ако покажеш малодушие в усилно време, Силата ти е малка.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Избавяй ония, които се влачат на смърт, И гледай да задържиш ония, които политат към клане.
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Ако речеш: Ето, ние не знаехме това! То Оня, Който претегля сърцата, не разбира ли? Оня, Който пази душата ти, на знае ли, И не ще ли въздаде на всеки според делата му?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Сине мой, яж мед, защото е добър, И медена пита, защото е сладка на вкуса ти.
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 И ще знаеш, че такава е мъдростта за душата ти, Ако си я намерил; и има бъдеще, И надеждата ти няма да се отсече.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Не поставяй засада, о нечестиви човече, против жилището на праведния, Не разваляй мястото му за почивка.
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 Защото праведният ако седем пъти пада, пак става, Докато нечестивите се препъват в злото.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Не се радвай когато падне неприятелят ти, И да се не весели сърцето ти, когато се подхлъзне той.
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 Да не би да съгледа Господ, и това да Му се види зло, И Той да оттегли гнева Си от него.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Не се раздразвай, поради злодейците, Нито завиждай на нечестивите,
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 Защото злите не ще имат бъдеще; Светилникът на нечестивите ще изгасне.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Сине мой, бой се от Господа и от царя, И не се сношавай с непостоянните,
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 Защото бедствие ще се издигне против тях внезапно, И кой знае какво наказание ще им се наложи и от двамата?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 И тия са изречения на мъдрите: - Лицеприятие в съд не е добро.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 Който казва на нечестивия: Праведен си, Него народи ще кълнат, него племена ще мразят;
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 Но който го изобличават, към тях ще се показва благоволение, И върху тях ще дойде добро благословение.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 Който дава прав отговор, Той целува в устни.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Нареди си работата навън, И приготви си я на нивата, И после съгради къщата си.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Не бивай свидетел против ближния си без причина, Нито мами с устните си.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Не казвай: Както ми направи той, така ще му направя и аз, Ще въздам на човека според делата му.
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 Минах край нивата на ленивия И край лозето на нехайния човек,
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 И всичко бе обрасло с тръни, Коприва беше покрила повърхността му, И каменната му ограда беше съборена
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Тогава, като прегледах, размислих в сърцето си, Видях и взех поука.
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 Още малко спане, малко дрямка, Малко сгъване на ръце за сън,
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 И сиромашията ще дойде върху тебе, като крадец И немотията - като въоръжен мъж,
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.