< Притчи 19 >

1 По-добър е сиромахът, който ходи в непорочността си, Нежели оня, който е с извратени устни а при това безумен.
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 Наистина ожидане без разсъдък не е добро, И който бърза с нозете си, обърква пътя си.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 Безумието на човека изкривява пътя му, И сърцето му негодува против Господа.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Богатството притуря много приятели, А сиромахът бива оставен от приятеля си,
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 Лъжливият свидетел няма да остане ненаказан, И който издиша лъжи няма да избегне.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Мнозина търсят благоволението на щедрия, И всеки е приятел на онзи, който дава подаръци.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 Всичките братя на сиромаха го мразят, - Колко повече отбягват от него приятелите му! - Той тича след тях с умолителни думи, но тях ги няма.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 Който придобива ум обича своята си душа; Който пази благоразумие ще намери добро.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 Лъжлив свидетел няма да остане ненаказан, И който издиша лъжи ще загине.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Изнежеността не прилича на безумен, - Много по-малко на слуга да властвува над началници.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 Благоразумието на човека възпира гнева му, И слава е за него да се не взира в престъпление.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 Гневът на царя е като реване на лъв, А благоволението му е като роса на тревата.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 Безумен син е бедствие за баща си, И препирните на жена са непрестанно капене.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 Къща и богатство се оставят наследство от бащите, Но благоразумна жена е от Господа.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Леноста хвърля в дълбок сън, И бездейна душа ще гладува
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 Който пази заповедта пази душата си, А който немари пътищата си ще загине.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 Който показва милост към сиромаха заема Господу, И Той ще му въздаде за благодеянието му.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Наказвай сина си докато има надежда, И не закоравявай сърцето си да го оставиш да загине.
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 Яростен човек ще понесе наказание, Защото, ако и да го избавиш, трябва пак същото да направиш.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Слушай съвет и приемай поука, За да останеш мъдър в сетнините си.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 Има много помисли в сърцето на човека, Но намерението Господно, то ще устои.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 Милосърдието на човека е чест нему, И сиромах човек е по-добър от този, който разорява.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 Страхът от Господа спомага към живот; Който го има ще си ляга наситен и не ще срещне зло.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 Ленивият затопява ръката си в паницата И не ще нито в устата си да я повърне.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 Ако биеш присмивателя, простият ще стане внимателен; И ако изобличиш благоразумния, той ще придобие знание.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 Който опропастява баща си и пропъжда майка си, Той е син, който причинява срам и нанася позор.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 Престани, сине мой, да слушаш съвети, Които те отклоняват от мъдростта.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 Лошият свидетел се присмива на правосъдието; И устата на нечестивите поглъщат беззаконие.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Присъди се приготвят за присмивателите, И бой за гърба на безумните.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< Притчи 19 >