< Числа 14 >
1 Тогава цялото общество извика с висок глас, и людете плакаха през оная нощ.
Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
2 И всичките израилтяни роптаеха против Моисея и Аарона; и цялото общество им рече: Да бяхме измрели в Египетската земя! или в тая пустиня да бяхме измрели!
Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
3 И защо ни води Господ в тая земя да паднем от нож, и жените ни и децата ни да бъдат разграбени? Не щеше ли да ни е по-добре да се върнем в Египет?
Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
4 И рекоха си един на друг: Да си поставим началник и да се върнем в Египет.
Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
5 Тогава Моисей и Аарон паднаха на лицата си пред цялото множество на обществото израилтяни.
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
6 И Исус Навиевият син и Халев Ефрониевият син, от ония, които съгледаха земята, раздраха дрехите си,
Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
7 и говориха на цялото общество израилтяни, казвайки: Земята, през която минахме, за да я съгледаме, е много добра земя.
ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
8 Ако бъде благоволението на Господа към нас, тогава Той ще ни въведе в тая земя и ще ни я даде, - земя гдето текат мляко и мед.
Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
9 Само недейте въстава против Господа, нито се бойте от людете на земята, защото те са ястие за нас; защитата им се оттегли от върху тях; а Господ е с нас; не бойте се от тях.
koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
10 Но цялото общество рече да ги убият с камъни. Тогава Господната слава се яви в шатъра за срещане пред всичките израилтяни.
Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
11 И Господ рече на Моисея: До кога ще Ме презират тия люде? и до кога няма да Ме вярват, въпреки всичките знамения, които съм извършил пред тях?
Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
12 Ще ги поразя с мор и ще ги изтребя; а тебе ще направя народ по-голям и по-силен от тях.
Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
13 Но Моисей рече на Господа: Тогава египтяните ще чуят; защото Ти със силата Си си извел тия люде изсред тях;
Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
14 и ще кажат това на жителите на тая земя, които са чули, че Ти, Господи, си между тия люде, - че Ти, Господи, се явяваш лице с лице, и че облакът Ти стои над тях, и че Ти вървиш пред тях денем в облачен стълб, а нощем в огнен стълб.
Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
15 И ако изтребиш тия люде, като един човек, тогава народите, които са чули за Тебе, ще говорят казвайки:
Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
16 Понеже не можа Иеова да въведе тия люде в земята, за която им се кле, за това ги погуби в пустинята.
‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
17 И сега, моля Ти се, нека се възвеличи силата на Господа мой, както си говорил, казвайки;
“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
18 Господ е дълготърпелив и многомилостив, прощава беззаконие и престъпление, и никак не обезвинява виновния, и въздава беззаконието на бащите върху чадата до третия и четвъртия род.
‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
19 Прости, моля Ти се, беззаконието на тия люде, и според както си прощавал на тия люде от Египет до тука.
Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
20 И рече Господ: Прощавам им, според както си казал;
Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
21 но наистина заклевам се в живота Си, че ще се изпълни целия свят с Господната слава.
Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
22 Понеже от всички тия мъже, които са виждали славата Ми и знаменията, които извърших в Египет и в пустинята, и са Ме раздразвали до сега десет пъти, и не послушаха гласа Ми,
palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
23 наистина ни един от тях няма да види земята, за която се клех на бащите им, нито ще я види един от ония, които Ме презряха.
palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
24 Но понеже слугата ми Халев има в себе си друг дух, и той напълно Ме последва, за това него ще въведа в земята, в която влезе, и потомството му ще я наследва.
Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
25 (А амаличаните и ханаанците живеят в долината). Утре се върнете та идете в пустинята към Червеното море.
Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
26 Господ говори още на Моисея и Аарона, казвайки:
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
27 До кога ще търпя това нечестиво общество, което роптае против Мене? Чух роптанията на израилтяните, с които роптаят против Мене.
“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
28 Кажи им: Заклевам се в живота Си, казва Господ, невярно ще направя на вас така, както вие говорихте в ушите Ми;
Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
29 труповете ви ще паднат в тая пустиня; и от преброените между вас, колкото сте на брой от двадесет години и нагоре, които сте роптали против Мене,
Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
30 ни един не ще влезе в земята, за която се клех да ви заселя в нея, освен Халев Ефониевият син и Исуса Навиевият син.
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
31 Но децата ви, за които рекохте, че ще бъдат разграбени, тях ще въведа; и те ще познаят земята, която вие презряхте.
Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
32 А вашите трупове ще паднат в тая пустиня.
Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
33 И децата ви ще скитат по пустинята четиридесет години, и ще теглят поради вашите блудствувания, докато се изпоядат труповете ви в пустинята.
Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
34 Според числото на дните, през които съгледахте земята, четиридесет дена, всеки ден за една година, четиридесет години ще теглите поради беззаконията си, и ще познаете какво значи Аз да съм неблагоразположен.
Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
35 Аз Господ говорих; наистина така ще направя на цялото това нечестива общество, което се е събрало против Мене; в тая пустиня ще се довършат, и в нея ще измрат.
Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
36 И ония мъже, които Моисей изпрати да съгледат земята, които, като се върнаха, направиха цялото общество да роптае против него, и зле представиха земята,
Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
37 тия мъже, които зле представиха земята, измряха от язвата пред Господа.
Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
38 А Исус Навиевият син и Халев Ефониевият син останаха живи измежду ония мъже, които ходиха да съгледат земята.
Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
39 Тогава Моисей каза тия думи на всичките израилтяни; и людете плакаха горчиво.
Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
40 И сутринта, като станаха рано, изкачиха се на планинския връх и казаха: Ето ни; и ще вървим напред на мястото, което Господ ни е обещал; защото съгрешихме.
Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
41 А Моисей рече: Защо престъпвате така Господното повеление, тъй като това няма да успее?
Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
42 Не вървете напред, защото Господ не е между вас, да не би да ви поразят неприятелите ви.
Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
43 Защото амаличаните и ханаанците са там пред вас, и вие ще паднете от нож. Понеже отстъпихте и не следвахте Господа, затова Господ няма да бъде с вас.
chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
44 Обаче те дръзнаха да се изкачат на планинския връх; но ковчегът на Господния завет и Моисей не излязоха изсред стана.
Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
45 Тогава амаличаните и ханаанците, които живееха на оная планина, слязоха та ги разбиха, и поразяваха ги дори до Хорма.
Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.