< Михей 1 >
1 Господното слово, което дойде към моресетеца Михей в дните на Юдовите царе Иотам, Ахаз, Езекия, което чу във видение за Самария и Ерусалим:
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Слушайте, всички племена, И ти, земльо, и всичко що има в тебе; И нека бъде Господ Иеова свидетел против вас, Господ из светия Си храм.
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
3 Защото, ето, Господ излиза от мястото Си, И като слезе ще стъпи на земните височини.
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 Планините ще се стопят под Него, И долините ще се разпуснат, Като восък пред огъня, И като води, които се изливат низ стръмнина.
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 Поради нечестието на Якова е всичко това, И поради греховете на Израилевия дом. Кое е нечестието на Якова? Не е ли Самария? И кои са високите Юдови места? Не е ли Ерусалим?
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
6 Затова, ще направя Самария като грамада камъни в нива, Място за садене лозе; Ще изсипя камъните й в долината, И ще оголя основите й.
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
7 Всичките й ваяни идоли ще се изпотрошат, Всичките дадени ней в заплата ще се изгорят в огън, Да! всичките й идоли ще погубя; Защото ги е събрала от заплата на блудство, И в заплата на блудство ще се върнат.
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
8 Затова ще ридая и плача, Ще ходя съблечен и гол; Ще вия като чакалите, И ще жалея като камилоптиците.
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
9 Защото раната й е неизцелима, Тъй като дойде и до Юда, Стигна до портата на людете Ми, до Ерусалим.
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 Не възвестявайте това в Гет; никак не плачете; Във Вит-арфа се оваляй в праха.
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
11 Бягай, жителко на Сафир срамно заголена; Жителката на Саанан не е излязла; Риданието на Вит-езил ще оттегли от вас своето покровителство.
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
12 Защото жителката на Марот
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Впрегни бързия кон в колесницата, ти жителко на Лахис, Която беше първа причина за грях на сионовата дъщеря; Защото в тебе се намериха Израилевите нечестия.
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
14 Затова, ще дадеш прощални подаръци на Моресет-гет; Домовете на Ахзив ще излъжат Израилевите царе,
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
15 Още ще ти доведа едного, който ще те владее, о жителко на Мариса; Израилевата слава ще дойде и до Одолам.
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
16 Оплешивей, и острижи главата си За милите си чада; Разшири плешивостта си като лешояд, Защото отидоха от тебе в плен.
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.