< Съдии 12 >

1 Тогава Ефремовите мъже се събраха и, като преминаха към север, рекоха на Ефтая: Ти защо отиде да воюваш против амонците, а нас не повика да дойдем с тебе? Ние ще изгорим къщата ти с огън, и тебе в нея.
Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
2 А Ефтай им рече: Аз и людете ми имахме голям спор с амонците; и аз ви повиках, и вие не ме избавихте от ръката им.
Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
3 И като видях, че не ме избавихте, турих в опасност живота си, като отидох против амонците; и Господ ги предаде в ръката ми. И сега защо сте дошли при денес да се биете против мене?
Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
4 Тогава Ефтай събра всичките галаадски мъже, та се би против Ефрема; и галаадските мъже поразиха ефремците, защото тия рекоха: Бежанци от Ефрема сте вие, галаадци, живеещи между ефремците и манасийците!
Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
5 Галаадците взеха бродовете на Иордан към Ефремовата земя; и когато някой от ефремските бежанци кажеше: Оставете ме да премина, тогава галаадските мъже му казваха: Ти ефремец ли си?
Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
6 Ако речеше: Не съм, тогава му думаха: Речи Шиболет, а той казваше: Сиболет, защото не можеше да го произнесе право. Тогава го хващаха, та го заколваха при бродовете на Иордан. И в онова време паднаха от Ефрема четиридесет и две хиляди души.
Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
7 И Ефтай съди Израиля шест години. Тогава Ефтай, галаадецът, умря, и бе погребан в един от галаадските градове.
Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
8 А подир него, Ивцан от Витлеем стана съдия в Израиля.
Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
9 Той имаше тридесет сина, и тридесет дъщери, които омъжиха навън; и взе от вън тридесет дъщери за синовете си. И съди Израиля седем години.
Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 И Ивцан умря, и бе погребан във Витлеем.
Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
11 След него, завулонецът Елон стана съдия в Израиля, и съди Израиля десет години.
Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
12 И Елон завулонецът умря, и бе погребан в Еалон в Завулоновата земя.
Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
13 А след него, Авдон, син на пиратонеца Илела, стана съдия в Израиля.
Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
14 Той имаше четиридесет сина и тридесет внуци, които яздеха на седемдесет ослета; и съди Израиля осем години.
Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
15 И Авдон, син на пиратонеца Илела, умря, и бе погребан в Пиратон в Ефремовата земя, на амаликската хълмиста страна.
Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.

< Съдии 12 >