< Иоил 3 >

1 Защото, ето, в ония дни и в онова време, Когато върна Юдовите и Ерусалимските пленници,
“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
2 Ще събера всичките народи Та ще ги сведа в Иософатовата (Т. е., Господ съди) долина, И там ще се съдя с тях Поради людете си и наследството си Израиля, Когото разпръснаха между народите. Те си разделиха земята ми
ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
3 И хвърлиха жребия за людете ми; Даваха момче заблудница, И продаваха момиче, за да пият вино.
Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
4 Да! и що имате с мене вие, Тире, Сидоне, И всички Филистимски предели? Искате ли да ми въздадете възмездие? А ако ми въздадете, То аз без забава бързо ще ви върна възмездието ви върху главите ви.
“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
5 Понеже взехне среброто ми и и златото ми, И занесохте в капищата си отбраните ми блага,
Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
6 А продадохте на Гърците, Юдейците и Ерусалимците, За да ги отдалечите от пределите им,
Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
7 За това аз ще ги повдигна от мясото, За което ги продадохте, И ще върна възмездието ви на собствената ви глава;
“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
8 Още ще продам вашите синове и вашите дъщери В ръката на Юдейците, А те ще ги продадат на Савците, - на далечен народ; Защото Господ изговори това.
Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
9 Прогласете това между народите; Пригответе война; повдигнете юнаците; Нека се приближат всички военни мъже; Нека възлизат.
Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
10 Изковете палечниците си на ножове, И сърповете си на копия; Слабият нека каже - Аз съм юнак!
Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
11 Съберете се и дойдете отвред всички народи, Та се натрупайте заедно; Господи, нарави да слезнат там юнаците ти.
Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
12 Нека станат народите и дойдат В Иосафатовата долина; Защото там ще седна да съдя всичките околни народи.
“Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
13 Пускайте сърпа в жетвата, защото е узряла; Дойдете, тъпчете, защото линът е пълен, И каците се преливат; Понеже нечестието им е голямо.
Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
14 Множества, множества в долината, дето ще се отсъди за тях; Защото близо е денят Господен в долината дето ще се даде присъдата.
Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
15 Слънцето и луната ще потъмнеят, И звездите ще оттеглят светенето си.
Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
16 И Господ ще изрикае от Сион, И ще издаде гласа си от Ерусалим; Небето и земята ще се потресат; Но Господ ще бъде прибежище на людете си, И крепост на Израиляните.
Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
17 Така ще познаете, че Аз Съм Господ вашият Бог, Който обитавам в светия си хълм Сион; Тогава Ерусалим ще бъде свет, И чужденци няма вече да минават през него.
“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
18 В оня ден От планините ще капе мъст, И от хълмите ще тече мляко, И по всичките Юдови дерета ще текат води; А из дома Господен ще избликне извор, Който ще пои Ситимската долина.
“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
19 Египет ще запустее, И Едом ще бъде гола пустиня, Поради насилието, сторено към Юдейците; Защото са пролели невинна кръв в земята им.
Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
20 А Юда ще бъде населен до века, И Ерусалим из род в род.
Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
21 И чрез наказание ще изкарам за чиста кръвта, която още не съм изкарал; Защото Господ обитава в Сион.
Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”

< Иоил 3 >