< Йов 36 >

1 И Елиу продължавайки рече:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Потърпи ме малко, и ще ти явя, Защото имам още нещо да ти кажа за Бога.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Ще черпя знанието си от далеч, И ще дам правда на Създателя си;
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Защото наистина думите ми не ще бъдат лъжливи; Един, който е усъвършенствуван в знание, стои пред тебе.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Ето, макар Бог да е мощен, не презира никого, - Макар да е мощен в силата Си да разсъждава.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Той не запазва живота на нечестивия, А на сиромасите отдава правото.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Не оттегля очите Си от праведните, Но даже ги туря и с царе да седят на престол за винаги, И те биват възвишени.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 А във вериги, ако са вързани, И хванати с въжета на наскърбление,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Тогава им явява делата им И престъпленията им, че са се възгордели,
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Отваря и ухото им за поука, И заповядва да се върнат от беззаконието;
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 И ако послужат и служат на Него, Ще прекарат дните си в благополучие И годините си във веселия;
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Но ако не послушат, ще загинат от меч, И ще умрат без мъдрост.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 А нечестивите в сърце питаят яд, Не викат към Бога за помощ когато ти връзва;
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Те умират в младост, И животът им угасва между мръсните.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Той избавя наскърбения чрез скръбта му, И чрез бедствие отваря ушите им
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 И така би извел и тебе из утеснение В широко място, гдето няма теснота; И слаганото на трапезата ти било би пълно с тлъстина.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Но ти си пълен със съжденията на нечестивия; Затова съдбата и правосъдието те хващат,
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Внимавай да не би жегата на страданията ти да те подигне против удара; Тогава нито голям откуп би те отървал.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Ще важи ли викането ти да те извади от бедствие, Или всичките напрежения на силата ти?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Не пожелавай нощта, Когато людете изчезват от мястото си.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Внимавай! Не пожелавай беззаконието; Защото ти си предпочел това повече от наскърблението.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Ето, Бог е възвишен в силата Си; Кой е господар като Него?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Кой Му е предписал пътя Му? Или кой може да Му рече: Извършил си беззаконие?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Помни да възвеличаваш Неговото дело, Което човеците възпяват,
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 В което всичките човеци се взират, Което човекът гледа от далеч.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Ето, Бог е велик, и ние Го не познаваме; Числото на годините Му е неизследимо.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Той привлича водните капки, Които таят в дъжд от парите Му,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Които облаците изливат И оросяват върху множество човеци.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Може ли, даже, някой да разбере как се разпростират облаците, Или се произвеждат гърмежите на скинията Му?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Ето, простира светлината Си около Себе Си, И се покрива с морските дъна.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 (Понеже чрез тия неща съди народите; Дава храна изобилно),
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Покрива ръцете Си със светкавицата, И заповядва й где да удари;
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Шумът й известява за това, И добитъкът - за пламъка, който възлиза.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Йов 36 >