< Йов 32 >
1 И така, тия трима човека престанаха да отговарят на Иова, защото беше праведен пред своите си очи.
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 Тогава пламна гневът на вузеца Елиу, син на Варахиила, от Арамовото семейство. Гневът му пламна против Иова, защото оправдаваше себе си наместо Бога
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 тоже против тримата му приятели пламна гневът му, защото бяха осъдили Иова без да му намерят отговор.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 А Елиу беше чакал да говори на Иова, защото другите бяха по-стари от него.
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 Но когато Елиу видя, че нямаше отговор в устата на тия трима мъже, гневът му пламна.
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 Тогава вузецът Елиу, син на Варахиила, в отговор рече: - Аз съм млад, а вие много стари; Затова се посвених, и не смеех да ви явя моето мнение.
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 Аз рекох: Дните нека говорят, И многото години нека учат мъдрост.
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 Но има дух в човека; Вдъхновението на Всемогъщия го вразумява.
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 Не че човеците са велики, за това ще са и мъдри, Нито че са стари, за това ще разбират правосъдието.
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 Прочее, казвам: Слушайте мене; Нека явя и аз мнението си.
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Ето, чаках докато вие говорехте, Слушах разсъжденията ви, Когато търсехте какво да кажете;
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 Внимателно ви слушах, И ето, ни един от вас не убеди Иова, Нито отговори на думите му;
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 За да не речете: Ние намерихме мъдрост. Бог ще го свали, а не човек.
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Понеже той не е отправил думите си против мене, То и аз няма да му отговоря според вашите речи.
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 Те се смайват, не отговарят вече, Не намират ни дума да кажат.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 А да чакам ли аз понеже те не говорят, - Понеже стоят и не отговарят вече?
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 Нека отговоря и аз от моя страна, Нека явя и аз мнението си.
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 Защото съм пълен с думи; Духът в мене дълбоко ме притиска.
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 Ето коремът ми е като вино неотворено, Близо е да се разпукне като нови мехове.
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 Ще проговоря, за да ми стане по-леко; Ще отворя устните си и ще отговоря.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Далеч от мене да гледам на лице, Или да полаская човека.
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 Защото не зная да лаская; Иначе Създателят ми би ме отмахнал веднага.
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”