< Йов 13 >

1 Ето, моето око е видяло всичко това, Ухото ми е чуло и го е разбрало.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Което знаете вие, това зная и аз; Не съм по-долен от вас.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 Но аз бих говорил на Всемогъщия, И желая да разисквам с Бога;
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 Защото вие сте измислители на лъжа; Всинца сте безполезни лекари.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 Дано млъкнехте съвсем! И това щеше да ви бъде за мъдрост.
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Слушайте сега доводите ми, И дайте внимание в жалбата на устните ми.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Заради Бога несправедливо ли ще говорите? Заради Него измама ли ще изкажете?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Заради Него пристрастие ли ще покажете? Заради Бога ще се съдите ли?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Добро ли е да ви изпита Той? Или ще можете да Го излъжете, както лъжат човека?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Той непременно ще ви изобличи, Ако тайно показвате пристрастие.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Величието Му не ще ли ви уплаши? И ужасът Му не ще ли да ви нападне?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Вашите паметни думи стават пред Него поговорки от пепел; Защитата ви става укрепление от кал.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Млъкнете! оставете ме и аз да говоря; И нека дойде върху мене каквото ще.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Каквото и да стане, ще взема месата си в зъбите си, И ще туря живота в шепата си.
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Ако и да ме убие Той, аз ще Го чакам; Но пак ще защитя пътищата си пред Него.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 Даже това ще ми бъде спасение, Че нечестив човек няма да дойде пред Него.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Послушайте внимателно думата ми; И изявлението ми нека бъде в ушите ви.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Ето сега, аз съм наредил делото си; Зная, че ще се оправдая.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Кой е оня, който ще се съди с мене? Защото, ако млъкна, сега ще издъхна.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Само две неща не ми направяй, Тогава не ще се скрия от лицето Ти,
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Не отказвай да оттеглиш ръката Си от мене, И нека ме не уплаши ужасът Ти.
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Тогава Ти повикай, и аз ще Ти отговоря; Или аз да говоря, и ти ми отговори.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Колко са беззаконията ми и греховете ми? Яви ми престъплението ми и греха ми.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Защо криеш лицето Си, И ме считаш за Свой неприятел?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Ще изморяваш ли лист отвяван? И ще гониш ли суха плява?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 Защо пишеш горести против мене, И ме правиш да наследявам беззаконията на младостта си,
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 И туряш нозете ми в клада, И наблюдаваш всичките ми пътища, Забелязваш дирите на нозете ми?
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 При все, че аз като гнила вещ тлея, Като дреха от молец изядена.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Йов 13 >