< Исая 51 >

1 Слушайте Мене, вие, които следвате правдата, Които търсите Господа; Погледнете на канарата, от която сте отсечени, И в дупката на ямата, из която сте изкопани,
“Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
2 Погледнете на баща си Авраама, И на Сара, която ви е родила; Защото, когато беше само един го повиках, Благослових го и го умножих.
taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
3 Защото Господ ще утеши Сиона Той ще утеши всичките му запустели места, И ще направи пустотата му като Едем, И запустялостта му като Господната градина; Веселие и радост ще се намери в него, Славословие и глас на хваление.
Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
4 Внимавайте на Мене, люде Мои, И слушайте Ме, народе Мой; Защото закон ще излезе от Мен И Аз ще поставя правосъдието Си за светлина на народите.
“Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
5 Правдата Ми наближава, Спасението Ми се яви, И мишците Ми ще съдят племената; Островите ще ме чакат, И ще уповават на мишцата Ми.
Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
6 Подигнете очите си на небето, И погледнете на земята долу, Защото небето ще изчезне като дим, И земята ще овехтее като дреха, И ония, които живеят на нея, подобно ще измрат; Но Моето спасение ще трае до века, И правдата Ми няма да се отмени.
Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
7 Слушайте Мене, вие, които знаете правда, Люде, които имате в сърцето си закона Ми; Не бойте се от укорите на човеците, Нито се смущавайте от ругатните им.
“Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
8 Защото молецът ще ги пояде като дреха, И червеят ще ги пояде като вълна; Но Моята правда ще пребъде до века, И спасението Ми из родове в родове.
Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
9 Събуди се, събуди се, облечи се с сила, мишца Господна! Събуди се както в древните дни, в отдавнашните родове! Не си ли ти, която си съсякла Раав, И смъртно си пробола змея?
Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
10 Не си ли ти която си изсушила морето, Водите на голямата бездна, И си направила морските дълбочини Път за преминаването на изкупените
Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
11 Изкупените от Господа ще се върнат И ще дойдат с възклицание в Сион Вечно веселие ще бъде на главата им; Ще придобият радост и веселие, А скръб и въздишане ще побягнат.
Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
12 Аз Аз съм, Който ви утешавам: Кой си ти та се боиш от смъртен човек, И от човешки син, който ще стане като трева;
Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
13 А си забравил Господа Създателя си, Който разпростря небето и основа земята, И непрестанно всеки ден се боиш От яростта на притеснителя Като че се приготвяше да изтреби? И где е сега яростта на притеснителя?
Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
14 Вързаният в заточение скоро ще бъде развързан, И няма да умре в ямата, Нито ще се лиши от хляба си;
Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
15 Защото Аз съм Господ твоят Бог, Който уталожвам морето, когато бучат вълните му; Господ на Силите е името Ми.
Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Турих словата Си в устата ти, И те покрих в сянката на ръката Си, За да река на Сиона: Ти си Мой народ.
Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
17 Събуди се, събуди се, стани, дъщерьо ерусалимска, Която си пила от ръката на Господа чашата на яростта Му; Пила си, и изпразнила си до дъно Чашата на омайването.
Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
18 От всичките синове, които е родила, Няма кой да я води; Нито има, който да я държи за ръка.
Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
19 Двете тия беди те сполетяха, - Кой ще те пожали? Разорение и погибел, глад и нож, - Как да те утеша?
Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
20 Синовете ти примряха: Лежат по всичките кръстопътища Както антилопа в мрежа; Пълни са с яростта Господна, С изобличението на твоя Бог.
Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
21 Прочее, слушай сега това Ти наскърбена и пияна, но не с вино:
Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
22 Така казва Господ Иеова, Твоят Бог, Който защитава делото на людете Си: Ето, взех от ръката ти чашата на омайването, Дори до дъно чашата на яростта Си; Ти няма вече да я пиеш.
Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
23 Аз ще я туря в ръката на притеснителите ти, Които рекоха на душата ти: Падни ничком, за да минем над тебе; И ти си сложила гърба си като земя И като път за ония, които минават.
Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”

< Исая 51 >