< Исая 1 >
1 Видението на Амосовия син Исаия, което видя за Юда и Ерусалим в дните на Юдовите царе Озия, Иотам, Ахаз и Езекия:
Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
2 Чуйте, небеса, и дай ухо, земьо. Защото Господ говорил, казвайки: Чада отхраних и възпитах; Но те се разбунтуваха против Мене.
Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
3 Волът познава стопанина си, И оселът яслите на господаря си; Но Израил не знае. Людете Ми не разсъждават.
Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
4 Уви, грешни народе, люде натоварени с беззаконие, Роде на злодейци, чада, които постъпвате разтлено! Оставиха Господа, Презряха Светия Израилев. Отделиха се и се върнаха назад.
Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
5 Защо да бъдете още бити, че се бунтувате повече и повече? Вече всяка глава е болна и всяко сърце изнемощяло;
Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
6 От стъпалото на ногата дори до главата няма в никое тяло здраво място. Но струпеи, и посинения, и гноясали рани. Които не са изстискани, нито превързани, Нито омекчени с масло.
Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
7 Страната ви е пуста, градовете ви изгорени с огън; Земята ви - чужденци я пояждат пред очите ви, И тя е пуста като разорена от чужденци.
Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
8 И сионовата дъщеря е оставена като колиба в лозе, Като пъдарница в градина с краставици, Като обсаден град.
Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9 Ако Господ на Силите не би ни оставил малък остатък, Като Содом бихме станали, на Гомор бихме се оприличили.
Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
10 Чуите словото Господно, князе содомски; Слушайте поуката на нашия Бог, люде гоморски.
Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
11 Защо Ми е множеството на жертвите ви? Казва Господ; Сит съм от всеизгаряне на овни И от тлъстина на угоени; И не ми е угодна кръв от юнци, Или от агнета или от едни козли.
Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12 Когато дохождате да се явявате пред мене, Кой е поискал от вас това, да тъпчете дворовете Ми?
Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13 Не принасяйте вече суетни приноси; Темянът е мерзост за Мене, Тоже и новолунията, и съботите, и свикването на събранията; Не мога да търпя беззаконието заедно с тържественото събрание.
Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14 Душата ми мрази новолунията ви и празниците ви; Досада са на Мене; дотегна Ми да ги търпя.
Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
15 И когато простирате ръцете си, Ще крия очите Си от вас; Даже когато принасяте много молитви не ще да слушам; Ръцете ви са пълни с кръв.
Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16 Измийте се, очистете се, Отмахнете от очите Ми злото на делата си, Престанете да вършите зло,
sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
17 Научете се да струвате добро, Настоявайте за правосъдие, поправяйте угнетителя, Отсъждайте право на сирачето, застъпвайте се за вдовицата.
phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
18 Дойдете сега та да разискаме, казва Господ; Ако са греховете ви като мораво, Ще станат бели като сняг; Ако са румени като червено, Ще станат като бяла вълна.
Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
19 Ако слушате драговолно, Ще ядете благото на земята;
Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20 Но ако откажете и се разбунтувате, Ще бъдете изпоядени от нож, Защото устата Господни изговориха това.
koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
21 Как стана блудница верният град, Който беше пълен с правосъдие! Правда обитаваше в него, а сега - убийци.
Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Среброто ти стана шлак; Виното ти се смеси с вода.
Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 Твоите князе са бунтовници и съучастници на крадци; Всеки от тях обича подаръци и тича след възнаграждения; Те не осъждат право сирачето, Нито дохожда при тях делото на вдовицата.
Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24 Затова, казва Господ, Иеова на Силите, Всемогъщият Израилев: Ах! ще се облекча от противниците Си, И ще отдам възмездие на враговете Си;
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25 И пак ще туря ръката Си върху тебе, И ще очистя шлака ти като с луга, И ще отделя от тебе всеки примес;
Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26 И ще възстановя съдиите ти както по-преди, И съветниците ти както отначало; Подир което ще се наречеш Град на правда, Верен град,
Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
27 Сион ще се изкупи чрез правосъдие, И тия, които се върнат в него, чрез правда.
Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28 А беззаконниците и грешниците ще се съкрушат заедно, И тия, които са оставили Господа, ще загинат.
Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
29 Защото ще се посрамят поради дъбовете, които пожелахте; И ще се смутите поради градините, които избрахте
“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
30 Понеже ще стана като дъб, чиито листа вехнат, И като градина, която няма вода.
Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31 И силният ще бъде като кълчища, И делото му като искра; И то ще изгори заедно с него, Без да има кой да го гаси.
Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”