< Авакум 1 >

1 Наложеното пророчество, което пророк Авакум чу във видение:
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 Докога, Господи, ще викам, а ти не щеш да слушаш? Викам към тебе за насилие, но не щеш да избавиш.
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Защо ми показваш беззаконие, И ме правиш да гледам извращение? Защото грабителство и насилие има пред мене, Има и каране, и препирня се повдига.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Затова, законът е отслабнал, И правосъдието не излиза към победа; Защото нечестивите окръжават праведния, Та правосъдието излиза извратено.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Погледнете между народите, вникнете, И се очудете много; Защото Аз ще извърша едно дело във вашите дни, Което няма да повярвате ако и да ви се разкаже.
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 Защото, ето, аз повдигам Халдейците, Оня лют и нетърпелив народ, Който минава през широчината на света, За да завладее селища, които не са негови.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 Страшни и ужасни са те; Съдът им и властта им произлизат от сами тях.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Конете им са по-бързи от леопарди, И по-свирепи от вечерни вълци; Конниците им скачат отпуснато, Да! конниците им идат от далеч, Летят като орел, който спеши да разкъсва.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 Всички идат да насилстват; Лицата им са насочени на напред, И събират пленници като пясък.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 Те се присмиват на царете, И първенците са за тях подигравка; Присмиват се на всяка крепост, Защото, като издигат грамади от пръст, превземат я.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Тогава духът му се изменя; Преминава като завоевател, и върши нечестие, Като прави силата си свой бог.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Не си ли ти от века, Господи Боже мой, Светий мой! Няма да умрем. Ти, Господи, си ги определил да извършат твоите съдби над нас; И ти Могъщи, си ги поставил за наше наказание.
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Тъй като очите ти са твърде чисти, за да гледаш злото, И не можеш да погледнеш извращението, Защо гледаш на беззаконниците, И мълчиш, когато нечестивият поглъща по-праведния от себе си,
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 И правиш човеците като морските риби, Като гадините, които си нямат управител?
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 Халдеецът изтръгва всичките с въдица, Влачи ги в мрежата си, И ги събира в невода си; За това се весели и се радва.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 По тая причина жертва на мрежата си, И гори тамян на невода си; Защото чрез тях делът му е тлъст, И ястието му отбрано.
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Но дали за това ще изпразва мрежата си, И престане от милост да убива постоянно народите?
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

< Авакум 1 >