< Езекил 33 >
1 И Господното слово дойде към мене и рече:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Сине човешки, говори на людете си и кажи им: Когато нанеса меча върху някоя земя, и людете на оная земя вземат някой човек изпомежду си и си го поставят за страж,
“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
3 и той, като види че мечът иде върху земята, затръби и предупреди людете,
Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
4 тогава, ако мечът дойде и постигне някого, който чуе гласа на тръбата, а не се пази, кръвта му ще бъде на главата му.
Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
5 Той е чул гласа на тръбата, а не се е свестил; кръвта му ще бъде върху него; когато, ако беше се свестил, той би избавил живота си:
Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
6 Но ако види стражът, че мечът иде и не затръби, и людете не се свестят, и мечът дойде и постигне някого от тях, той наистина биде постигнат поради беззаконието си; но кръвта му ще изискам от ръката на стража.
Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
7 Така е и с тебе, сине човешки; Аз те поставих страж на Израилевия дом; чуй, прочее, словото из устата Ми, и предупреди ги от Моя страна.
“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
8 Когато казвам на беззаконника: Беззаконнико, непременно ще умреш, а ти не проговориш, за да предупредиш беззаконника да се върне от пътя си, оня беззаконник ще умре за беззаконието си, обаче от твоята ръка ще изискам кръвта му.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
9 Но ако предупредиш беззаконника да се върне от пътя си, а не се върне от пътя си, той ще умре за беззаконието си, а ти си избавил душата си.
Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
10 Затова, сине човешки, речи на Израилевия дом: Вие така говорихте, казвайки: Престъпленията ни и греховете ни са върху нас, и ние тлеем поради тях; как тогава ще живеем?
“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
11 Речи им: Заклевам се в живота Си, казва Господ Иеова, не благоволя в смъртта на нечестивия, но да се върне нечестивият от пътя си и да живее. Върнете се, върнете се от лошите си пътища; защо да умрете, доме Израилев?
Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
12 Затова, сине човешки, кажи на людете си: Правдата на праведния няма да го избави в деня, когато престъпи; и нечестивият няма да падне поради нечестието си, също както праведният не ще може да живее поради правдата си в деня, когато съгреши.
“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
13 Когато река на праведния, че непременно ще живее, а той като уповае на правдата си, извърши неправда, то ни едно от неговите праведни дела няма да се спомни; а поради неправдата, която е извършил, той ще умре.
Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
14 И когато кажа на нечестивия: Непременно ще умреш; а той се върне от греха си и постъпи законно и праведно;
Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
15 ако нечестивият повърне залог, върне грабнатото, ходи в повеленията на живота, и не върши неправда, непременно ще живее; няма да умре;
monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
16 ни един от греховете, които е извършил няма да се помни против него; той е постъпил законно и праведно; непременно ще живее.
Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
17 Но твоите люде казват: Господният път не е прав. Обаче техният път не е прав.
“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
18 Когато праведният се върне от правдата си и извърши неправда, то поради нея ще умре.
Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
19 А когато беззаконникът се върне от беззаконието си и постъпи законно и праведно, той ще живее поради това.
Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
20 Вие обаче казвате: Господният път не е прав. Доме Израилев, ще ви съдя всекиго според постъпките му.
Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
21 В дванадесетата година от плена ни, в десетия месец, на петия ден от месеца, дойде при мене един бежанец от Ерусалим и каза: Градът се превзе.
Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
22 А вечерта, преди да дойде бежанецът, Господната ръка биде върху мене и отваряше устата ми, докле дойде той при мене заранта; и тъй, устата ми се отвориха, и не бях вече ням.
Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
23 И Господното слово дойде към мене и рече:
Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
24 Сине човешки, тия, които живеят в ония опустошени места в Израилевата земя, говорят, казвайки: Авраам бе само един, но пак наследи земята; а ние сме мнозина; нам се даде земята в наследство.
“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
25 Затова, кажи им: Така казва Господ Иеова: Вие ядете месо с кръвта му, подигате очи към идолите си и проливате кръв; и ще владеете ли земята?
Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
26 Вие се облягате на меча си, вършите мерзости, и осквернявате всеки жената на ближния си; и ще владеете ли земята?
Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
27 Кажи им това: Така казва Господ Иеова: Заклевам се в живота Си, ония, които са в опустошените места, непременно ще паднат от нож; и който е на отворено поле ще го предам на зверовете да го изядат; а които са в крепостите и в пещерите ще измрат от мор.
“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
28 И ще обърна земята на пустота и да бъде за удивление, и горделивата й сила ще престане; и Израилевите планини ще запустеят, та да няма кой да минава.
Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
29 Тогава ще познаят, че Аз съм Господ, който обърна земята на пустота и да бъде за удивление, поради всичките мерзости, които сториха.
Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
30 А колкото за тебе, сине човешки, твоите люде приказват за тебе при стените и вратите на къщите, и като говорят един на друг, всеки на брата си, казва: Дойдете сега та чуйте що е словото, което излиза от Господа.
“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
31 Те дохождат при тебе както дохождат людете, та седят пред тебе като Мои люде, и слушат твоите думи, но не ги изпълняват; защото с устата си показват много любов, но сърцето им отива след печалбите им.
Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
32 ето, ти им си като любима песен от човек, който има сладък глас и свири добре; защото слушат думите ти, а не ги изпълняват.
Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
33 А когато настане това, (и ето, иде), тогава ще познаят, че е имало пророк между тях.
“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”