< Изход 8 >

1 Тогава Господ рече на Моисея: Влез при Фараона и кажи му: Така казва Господ, пусни людете Ми, за да Ми послужат.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 Но ако откажеш да ги пуснеш, ето, Аз ще поразя всичките ти предели с жаби.
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 Реката ще кипне с жаби, които като излизат ще наскачат в къщата ти, в спалнята ти, по леглото ти, в къщата на слугите ти, върху людете ти, в пещите ти и по нощвите ти.
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 На тебе, на людете ти и на всичките ти слуги ще наскачат жабите.
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 И тъй, Господ рече на Моисея: Кажи на Аарона: Простри ръката си с жезъла си над реките, над потоците и над езерата, та стори да наскачат жаби по Египетската земя.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 И Аарон простря ръката си над египетските води и възлязоха жабите и покриха Египетската земя.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 Но и магьосниците сториха същото с баянията си, и направиха да наскачат жаби по Египетската земя.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Тогава Фараон повика Моисея и Аарона и рече: Помолете се Господу да махне жабите от мене и от людете ми; и ще пусна людете ви, за да пожертвуват Господу.
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 И Моисей рече на Фараона: Определи ми, кога да се помоля за тебе, за слугите ти и за людете ти, за да се изтребят жабите от тебе и от къщите ти, та да останат само в реката.
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 Фараон каза: Утре. А той рече: Ще бъде според както си казал, за да познаеш, че няма никой подобен на нашия Бог.
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 Жабите ще се махнат от тебе от къщите ти, от слугите ти и от людете ти; само в реката ще останат.
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Тогава Моисей и Аарон излязоха отпред Фараона; и Моисей викна към Господа относно жабите, които беше пратил върху Фараона.
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 И Господ стори според както викна Моисей; жабите измряха от къщите, от дворовете и от нивите.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 И събраха ги на купове: и земята се усмърдя.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 А Фараон като видя, че му дойде облекчение, закорави сърцето си и не ги послуша според както Господ беше говорил.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 След това Господ каза на Моисея: Речи на Аарона: Простри жезъла си та да удари земната пръст, за да се превърне на въшки в цялата Египетска земя.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 И сториха така; Аарон простря ръката си с жезъла си и удари земната пръст, и явиха се по човеците и по животните; всичката земна пръст се превърна на въшки из цялата Египетска земя.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 И магьосниците работеха да вършат същото с баянията си, за да произведат въшки, но не можаха; а въшките бяха по човеците и по животните.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 Тогава рекоха магьосниците на Фараона: Божий пръст е това. Но сърцето на Фараона се закорави, и той не ги послуша, според както Господ беше говорил.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 После Господ рече на Моисея: Стани утре рано та застани пред Фараона (ето, той излиза да отиде при водата), и кажи му: Така казва Господ: Пусни людете Ми, за да Ми послужат.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 Защото, ако не пуснеш людете Ми, ето, ще изпратя рояци мухи върху тебе, върху слугите ти, върху людете ти и върху къщите ти; тъй щото къщите на египтяните и земята, на която живеят, ще се пълнят с рояци мухи.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 Но в оня ден Аз ще отделя Гесенската земя, в която живеят людете Ми, щото да няма там рояци мухи, за да познаят, че Аз съм Господ всред земята.
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 Аз ще поставя преграда между Своите люде и твоите люде; утре ще стане това знамение.
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 И Господ стори така; навлязоха мъчителни рояци мухи във Фараоновата къща и в къщите на слугите му и в цялата Египетска земя; земята се развали от рояците мухи.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Тогава Фараон повика Моисея и Аарона и рече: Идете, принесете жертва на вашия Бог в тая земя.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 Но Моисей каза: Не е прилично да направим така, защото ние ще жертвуваме на Господа нашия Бог онова, от което египтяните се гнусят; ето, ако жертвуваме пред очите на египтяните онова, от което те се гнусят, няма ли да ни избият с камъни?
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 Ще отидем на тридневен път в пустинята и ще жертвуваме на Господа нашия Бог, според както би ни казал.
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 Тогава рече Фараон: Ще ви пусна да пожертвувате на Господа вашия Бог в пустинята, само да не отидете много далеч. Помолете се Богу за мене.
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 И Моисей рече: Ето, аз излизам отпред тебе, и ще се помоля Господу да се махнат утре рояците мухи от Фараона, от слугите му и от людете му; но нека не следва Фараон да лъже и да не пуска людете ни да пожертвуват Господу.
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 И тъй, Моисей излезе отпред Фараона и помоли се Господу.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 И Господ стори според както Моисей се молеше; той махна рояците мухи от Фараона, от слугите му и от людете му; не остана ни една.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 Но Фараон и тоя път закорави сърцето си и не пусна людете.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

< Изход 8 >